< Genesis 18 >
1 and to see: see to(wards) him LORD in/on/with terebinth Mamre and he/she/it to dwell entrance [the] tent like/as heat [the] day
Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
2 and to lift: look eye his and to see: see and behold three human to stand upon him and to see: see and to run: run to/for to encounter: meet them from entrance [the] tent and to bow land: soil [to]
Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
3 and to say lord my if please to find favor in/on/with eye: seeing your not please to pass from upon servant/slave your
“Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
4 to take: bring please little water and to wash: wash foot your and to lean underneath: under [the] tree
Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
5 and to take: bring morsel food: bread and to support heart your (after *L(S)*) to pass for as that: since as as to pass upon servant/slave your and to say so to make: do like/as as which to speak: speak
Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
6 and to hasten Abraham [the] tent [to] to(wards) Sarah and to say to hasten three seah flour fine flour to knead and to make bun
Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
7 and to(wards) [the] cattle to run: run Abraham and to take: take son: young animal cattle tender and pleasant and to give: give to(wards) [the] youth and to hasten to/for to make [obj] him
Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
8 and to take: take curd and milk and son: young animal [the] cattle which to make and to give: put to/for face: before their and he/she/it to stand: stand upon them underneath: under [the] tree and to eat
Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
9 and to say to(wards) him where? Sarah woman: wife your and to say behold in/on/with tent
Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
10 and to say to return: return to return: return to(wards) you like/as time alive and behold son: child to/for Sarah woman: wife your and Sarah to hear: hear entrance [the] tent and he/she/it after him
Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
11 and Abraham and Sarah old to come (in): advanced in/on/with day: year to cease to/for to be to/for Sarah way like/as woman
Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
12 and to laugh Sarah in/on/with entrails: among her to/for to say after to become old I to be to/for me delight and lord my be old
Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
13 and to say LORD to(wards) Abraham to/for what? this to laugh Sarah to/for to say also truly to beget and I be old
Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
14 to wonder from LORD word: thing to/for meeting: time appointed to return: return to(wards) you like/as time alive and to/for Sarah son: child
Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
15 and to deceive Sarah to/for to say not to laugh for to fear and to say not for to laugh
Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
16 and to arise: rise from there [the] human and to look upon face: surface Sodom and Abraham to go: went with them to/for to send: depart them
Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
17 and LORD to say to cover I from Abraham which I to make: do
Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
18 and Abraham to be to be to/for nation great: large and mighty and to bless in/on/with him all nation [the] land: country/planet
Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
19 for to know him because which to command [obj] son: child his and [obj] house: household his after him and to keep: obey way: conduct LORD to/for to make: do righteousness and justice because to come (in): bring LORD upon Abraham [obj] which to speak: promise upon him
Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
20 and to say LORD outcry Sodom and Gomorrah for to multiply and sin their for to honor: heavy much
Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
21 to go down please and to see: see like/as cry her [the] to come (in): come to(wards) me to make: do consumption and if not to know
choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
22 and to turn from there [the] human and to go: went Sodom [to] (and Abraham *L(S)*) still he to stand: stand to/for face: before (LORD *L(S)*)
Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
23 and to approach: approach Abraham and to say also to snatch righteous with wicked
Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
24 perhaps there fifty righteous in/on/with midst [the] city also to snatch and not to lift: bear to/for place because fifty [the] righteous which in/on/with entrails: among her
Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
25 forbid to/for you from to make: do like/as Chronicles [the] this to/for to die righteous with wicked and to be like/as righteous like/as wicked forbid to/for you to judge all [the] land: country/planet not to make: do justice
Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
26 and to say LORD if to find in/on/with Sodom fifty righteous in/on/with midst [the] city and to lift: bear to/for all [the] place in/on/with for the sake of them
Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
27 and to answer Abraham and to say behold please be willing to/for to speak: speak to(wards) Lord and I dust and ashes
Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
28 perhaps to lack [emph?] fifty [the] righteous five to ruin in/on/with five [obj] all [the] city and to say not to ruin if to find there forty and five
bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
29 and to add: again still to/for to speak: speak to(wards) him and to say perhaps to find [emph?] there forty and to say not to make: do in/on/with for the sake of [the] forty
Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
30 and to say not please to be incensed to/for Lord and to speak: speak perhaps to find [emph?] there thirty and to say not to make: do if to find there thirty
Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
31 and to say behold please be willing to/for to speak: speak to(wards) Lord perhaps to find [emph?] there twenty and to say not to ruin in/on/with for the sake of [the] twenty
Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
32 and to say not please to be incensed to/for Lord and to speak: speak surely [the] beat perhaps to find [emph?] there ten and to say not to ruin in/on/with for the sake of [the] ten
Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
33 and to go: journey LORD like/as as which to end: finish to/for to speak: speak to(wards) Abraham and Abraham to return: return to/for place his
Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.