< Genesis 12 >

1 and to say LORD to(wards) Abram to go: went to/for you from land: country/planet your and from relatives your and from house: household father your to(wards) [the] land: country/planet which to see: see you
Tsiku lina Yehova anamuwuza Abramu kuti, “Tuluka mʼdziko lako. Siya abale ako ndi banja la abambo ako ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.
2 and to make you to/for nation great: large and to bless you and to magnify name your and to be blessing
“Ndidzakusandutsa kholo la mtundu waukulu wa anthu ndipo ndidzakudalitsa; ndi kukusandutsa wotchuka kotero kuti udzakhala dalitso kwa anthu ambiri.
3 and to bless to bless you and to lighten you to curse and to bless in/on/with you all family [the] land: planet
Ndidzadalitsa amene adzadalitsa iwe, ndi kutemberera amene adzatemberera iwe; ndipo mafuko onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iwe.”
4 and to go: went Abram like/as as which to speak: speak to(wards) him LORD and to go: went with him Lot and Abram son: aged five year and seventy year in/on/with to come out: come he from Haran
Choncho Abramu ananyamuka monga momwe Yehova anamuwuzira, napita pamodzi ndi Loti. Pamene Abramu amachoka ku Harani nʼkuti ali ndi zaka 75.
5 and to take: take Abram [obj] Sarai woman: wife his and [obj] Lot son: child brother: male-sibling his and [obj] all property their which to gather and [obj] [the] soul: person which to make: offer in/on/with Haran and to come out: come to/for to go: went land: country/planet [to] Canaan and to come (in): come land: country/planet [to] Canaan
Abramu anatenga mkazi wake Sarai, Loti, mwana wamngʼono wake, pamodzi ndi chuma chawo chimene anapeza ndi antchito amene anali nawo ku Harani. Iwo ananyamuka ulendo mpaka kukafika ku dziko la Kanaani.
6 and to pass Abram in/on/with land: country/planet till place Shechem till terebinth Moreh and [the] Canaanite then in/on/with land: country/planet
Abramu anadutsa mʼdzikomo mpaka kukafika ku Sekemu pa mtengo wa thundu wa ku More. Nthawi imeneyo Akanaani analipobe mʼdzikomo.
7 and to see: see LORD to(wards) Abram and to say to/for seed: children your to give: give [obj] [the] land: country/planet [the] this and to build there altar to/for LORD [the] to see: see to(wards) him
Yehova anadza kwa Abramu nati, “Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko limeneli.” Choncho Abramu anamangira Yehova amene anadza kwa iye, guwa lansembe.
8 and to proceed from there [the] mountain: hill country [to] from front: east to/for Bethel Bethel and to stretch (tent his *Q(K)*) Bethel Bethel from sea: west and [the] Ai from front: east and to build there altar to/for LORD and to call: call to in/on/with name LORD
Atachoka pamenepo analowera cha ku mapiri a kummawa kwa Beteli namangako tenti yake pakati pa Beteli chakumadzulo ndi Ai chakummawa. Kumeneko anamangira Yehova guwa lansembe napemphera mʼdzina la Yehovayo.
9 and to set out Abram to go: continue and to set out [the] Negeb [to]
Kenaka Abramu ananyamuka kumalowera cha ku Negevi.
10 and to be famine in/on/with land: country/planet and to go down Abram Egypt [to] to/for to sojourn there for heavy [the] famine in/on/with land: country/planet
Kunagwa njala yayikulu mʼdzikomo, ndipo Abramu anapita ku Igupto kukakhala ngati mlendo kwa kanthawi kochepa popeza njalayo inakula kwambiri.
11 and to be like/as as which to present: come to/for to come (in): come Egypt [to] and to say to(wards) Sarai woman: wife his behold please to know for woman beautiful appearance you(f. s.)
Atatsala pangʼono kulowa mu Igupto, Abramu anamuwuza mkazi wake Sarai kuti, “Ndimadziwa kuti ndiwe mkazi wokongola kwambiri.
12 and to be for to see: see [obj] you [the] Egyptian and to say woman: wife his this and to kill [obj] me and [obj] you to live
Tsono Aigupto akakuona adzanena kuti ‘Ameneyu ndi mkazi wake.’ Tsono adzandipha ine nakusiya iwe ndi moyo.
13 to say please sister my you(f. s.) because be good to/for me in/on/with for the sake of you and to live soul: life my in/on/with because of you
Tsono udzikawawuza kuti iwe ndiwe mlongo wanga. Ukatero zidzandiyendera bwino ndipo ndidzapulumuka chifukwa cha iwe.”
14 and to be like/as to come (in): come Abram Egypt [to] and to see: see [the] Egyptian [obj] [the] woman for beautiful he/she/it much
Pamene Abramu anafika ku Igupto, Aigupto aja anaona kuti Sarai anali mkazi wokongoladi.
15 and to see: see [obj] her ruler Pharaoh and to boast: praise [obj] her to(wards) Pharaoh and to take: take [the] woman house: household Pharaoh
Pamene akuluakulu a ku nyumba ya Farao anamuona, anakamuyamikira pamaso pa Farao ndipo ananka naye ku nyumba ya Farao.
16 and to/for Abram be good in/on/with for the sake of her and to be to/for him flock and cattle and donkey and servant/slave and maidservant and she-ass and camel
Abramu naye zinthu zinkamuyendera bwino chifukwa cha Sarai. Farao anamupatsa nkhosa, ngʼombe, abulu aamuna ndi abulu aakazi, antchito aakazi pamodzi ndi ngamira.
17 and to touch LORD [obj] Pharaoh plague great: large and [obj] house: household his upon word: because Sarai woman: wife Abram
Koma Yehova anabweretsa matenda owopsa pa Farao pamodzi ndi banja lake lonse chifukwa cha Sarai mkazi wa Abramu.
18 and to call: call to Pharaoh to/for Abram and to say what? this to make: do to/for me to/for what? not to tell to/for me for woman: wife your he/she/it
Choncho Farao anayitanitsa Abramu namufunsa kuti, “Nʼchiyani wandichitirachi? Nʼchifukwa chiyani sunandiwuze kuti ameneyu ndi mkazi wako?
19 to/for what? to say sister my he/she/it and to take: take [obj] her to/for me to/for woman: wife and now behold woman: wife your to take: take and to go: went
Nʼchifukwa chiyani unati ndi mlongo wako, mpaka ine ndinamutenga kukhala mkazi wanga? Eko mkazi wako. Mutenge uzipita!”
20 and to command upon him Pharaoh human and to send: depart [obj] him and [obj] woman: wife his and [obj] all which to/for him
Farao analamula asilikali ake ndipo iwo anamutulutsa Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo.

< Genesis 12 >