< Ezekiel 46 >

1 thus to say Lord YHWH/God gate [the] court [the] inner [the] to turn east to be to shut six day [the] deed: work and in/on/with day [the] Sabbath to open and in/on/with day [the] month: new moon to open
“Ambuye Yehova akuti, Chipata chakummawa cha bwalo lamʼkati chizikhala chotseka pa masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito, koma chizitsekulidwa pa tsiku la sabata ndi pa tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano.
2 and to come (in): come [the] leader way: direction Portico [the] gate from outside and to stand: stand upon doorpost [the] gate and to make: offer [the] priest [obj] burnt offering his and [obj] peace offering his and to bow upon threshold [the] gate and to come out: come and [the] gate not to shut till [the] evening
Mfumu izilowa podzera mʼkhonde la mʼkati la chipata pochokera kunja, nʼkudzayima pafupi ndi nsanamira yapakhomo. Ansembe apereke nsembe yake yopsereza ndi nsembe yake yachiyanjano. Mfumuyo ipembedze pa chiwundo cha pa chipatacho kenaka nʼkutuluka. Koma chipatacho asachitseke mpaka madzulo.
3 and to bow people [the] land: country/planet entrance [the] gate [the] he/she/it in/on/with Sabbath and in/on/with month: new moon to/for face: before LORD
Anthu a mʼdziko azipembedza pamaso pa Yehova pa khomo la chipata chimenechi pa masiku a sabata ndi pa tsiku la mwezi watsopano.
4 and [the] burnt offering which to present: bring [the] leader to/for LORD in/on/with day [the] Sabbath six lamb unblemished and ram unblemished
Nsembe yopsereza imene mfumu iyenera kupereka kwa Yehova ikhale motere: pa tsiku la Sabata izipereka ana ankhosa aamuna asanu ndi mmodzi wopanda chilema, ndiponso nkhosa yayima yopanda chilema.
5 and offering ephah to/for ram and to/for lamb offering gift hand: expend his and oil hin to/for ephah
Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, mfumu izipereka nsembe ya chakudya yokwanira efa imodzi. Pamodzi ndi ana ankhosa, mfumu izipereka monga ikufunira kutero. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse ya tirigu.
6 and in/on/with day [the] month: new moon bullock son: young animal cattle unblemished and six lamb and ram unblemished to be
Pa tsiku la mwezi watsopano mfumuyo ipereke mwana wangʼombe wamwamuna, ana ankhosa asanu ndi mmodzi ndiponso nkhosa yayimuna, zonsezi zopanda chilema.
7 and ephah to/for bullock and ephah to/for ram to make: offer offering and to/for lamb like/as as which to overtake hand: themselves his and oil hin to/for ephah
Ipereke efa imodzi ya tirigu pa ngʼombe yayimuna iliyonse ndiponso efa ina pa nkhosa yayimuna iliyonse. Pa ana ankhosa ipereke tirigu monga ikufunira kutero. Pamodzi ndi efa ya tirigu, ipereke hini imodzi ya mafuta.
8 and in/on/with to come (in): come [the] leader way: direction Portico [the] gate to come (in): come and in/on/with way: direction his to come out: come
Pamene mfumu ikulowa, izidzera mʼkhonde lamʼkati la chipata chakummawa, izitulukiranso pomwepo.
9 and in/on/with to come (in): come people [the] land: country/planet to/for face: before LORD in/on/with meeting: festival [the] to come (in): come way: direction gate north to/for to bow to come out: come way: road gate south and [the] to come (in): come way: direction gate south to come out: come way: direction gate north [to] not to return: return way: road [the] gate which to come (in): come in/on/with him for before him (to come out: come *Q(K)*)
“Anthu a mʼdzikomo akabwera kudzapembedza Yehova pa masiku a chikondwerero, ngati munthu alowera pa chipata chakumpoto atulukire chipata chakummwera. Munthu wolowera chipata chakummwera, atulukire chipata chakumpoto. Munthu asatulukire pomwe walowera, koma atulukire pa chipata choyangʼanana nacho.
10 and [the] leader in/on/with midst their in/on/with to come (in): come they to come (in): come and in/on/with to come out: come they to come out: come
Mfumu izidzakhala pakati pawo. Anthu akamadzalowa mfumu idzalowa nawo. Anthu akamadzatuluka mfumu idzatuluka nawo.
11 and in/on/with feast and in/on/with meeting: festival to be [the] offering ephah to/for bullock and ephah to/for ram and to/for lamb gift hand: themselves his and oil hin to/for ephah
“Pa masiku achikondwerero ndi pa masiku ena osankhidwa, zopereka za chakudya zikhale zokwanira efa imodzi pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, efa imodzinso ndi nkhosa yayimuna, koma pa mwana wankhosa apereke monga angathere. Iperekenso hini imodzi ya mafuta pa efa iliyonse.
12 and for to make: offer [the] leader voluntariness burnt offering or peace offering voluntariness to/for LORD and to open to/for him [obj] [the] gate [the] to turn east and to make: offer [obj] burnt offering his and [obj] peace offering his like/as as which to make: do in/on/with day [the] Sabbath and to come out: come and to shut [obj] [the] gate after to come out: come he
Pamene mfumu ikufuna kupereka chopereka chaufulu kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena zopereka za chiyanjano, ayitsekulire chipata chakummawa. Iyo ipereke nsembe yopsereza kapena zopereka zake za chiyanjano monga imachitira pa tsiku la Sabata. Kenaka ituluke ndipo mfumuyo itatuluka, atseke chitsekocho.
13 and lamb son: aged year his unblemished to make: offer burnt offering to/for day: daily to/for LORD in/on/with morning in/on/with morning to make: offer [obj] him
“Tsiku lililonse nthawi ya mmawa azipereka kwa Yehova mwana wankhosa wa chaka chimodzi.
14 and offering to make: offer upon him in/on/with morning in/on/with morning sixth [the] ephah and oil third [the] hin to/for to moisten [obj] [the] fine flour offering to/for LORD statute forever: enduring continually
Pamodzi ndi nyamayo aziperekanso mmawa uliwonse chopereka cha chakudya chokwanira chimodzi mwa zigawo zisanu ndi chimodzi za efa. Aziperekanso chimodzi mwa zigawo zitatu za hini ya mafuta okandira ufa wosalala. Chopereka cha chakudya chimenechi chiziperekedwa kwa Yehova nthawi zonse mwa lamulo.
15 (to make: offer *Q(K)*) [obj] [the] lamb and [obj] [the] offering and [obj] [the] oil in/on/with morning in/on/with morning burnt offering continually
Motero azipereka mwana wankhosa ndi chopereka cha chakudya ndi mafuta mmawa uliwonse kuti zikhale nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku.
16 thus to say Lord YHWH/God for to give: make [the] leader gift to/for man: anyone from son: child his inheritance his he/she/it to/for son: child his to be possession their he/she/it in/on/with inheritance
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ngati kalonga apereka mphatso chigawo cha cholowa chake kwa mmodzi mwa ana ake, mphatsoyo idzakhala ya ana akewo. Idzakhala yawo chifukwa ndi cholowa chawo.
17 and for to give: give gift from inheritance his to/for one from servant/slave his and to be to/for him till year [the] liberty and to return: turn back to/for leader surely inheritance his son: child his to/for them to be
Koma ngati ipereka mphatso yotere kuchokera pa cholowa chake kwa mmodzi mwa antchito ake, mphatsoyo idzakhala ya wantchitoyo mpaka chaka chaufulu. Pambuyo pake idzabwereranso kwa kalongayo chifukwa cholowa chake ndi cha ana ake.
18 and not to take: take [the] leader from inheritance [the] people to/for to oppress them from possession their from possession his to inherit [obj] son: child his because which not to scatter people my man: anyone from possession his
Kalonga asalande cholowa chilichonse cha anthu, kuwachotsa mʼdera lawo la dziko. Iye apereke kwa ana ake cholowa chawo chochokera pa chuma chakechake, kuti pasapezeke ndi mmodzi yemwe mwa anthu anga wolandidwa chuma chake.’”
19 and to come (in): bring me in/on/with entrance which upon shoulder [the] gate to(wards) [the] chamber [the] holiness to(wards) [the] priest [the] to turn north [to] and behold there place (in/on/with flank *Q(K)*) sea: west [to]
Kenaka munthu uja anandidzeretsa pa khomo la pambali pa chipata nandilowetsa ku zipinda za ansembe zoyangʼana kumpoto. Ndipo ndinaona kumeneko malo chakumadzulo kwa zipindazo.
20 and to say to(wards) me this [the] place which to boil there [the] priest [obj] [the] guilt (offering) and [obj] [the] sin: sin offering which to bake [obj] [the] offering to/for lest to come out: send to(wards) [the] court [the] outer to/for to consecrate: holiness [obj] [the] people
Munthuyo anandiwuza kuti, “Awa ndi malo amene ansembe adzaphikirapo nsembe yopepesera kupalamula ndi nsembe yopepesera machimo. Kumenekonso azidzawotcherako chopereka cha chakudya. Sadzatuluka nazo zoyerazi mʼbwalo lakunja kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu ena.”
21 and to come out: send me to(wards) [the] court [the] outer and to pass me to(wards) four corner [the] court and behold court in/on/with corner [the] court court in/on/with corner [the] court
Pambuyo pake anandilowetsa mʼbwalo lakunja napita nane ku ngodya zinayi za bwalolo. Ndipo ndinaona mʼkati mwa ngodya iliyonse bwalo lina.
22 in/on/with four corner [the] court court to enclose forty length and thirty width measure one to/for four their to corner
Motero pa ngodya zinayi za bwalo panalinso mabwalo ena angʼonoangʼono. Mabwalo amenewa anali ofanana. Mulitali mwake munali mamita makumi awiri ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi ndi asanu.
23 and row around in/on/with them around to/for four their and hearth to make from underneath: under [the] encampment around
Kuzungulira mabwalo anayi angʼonoangʼono aja panali mpanda wamiyala, ndi malo asonkhapo moto omangidwa mʼmunsi mwa mpandawo mozungulira.
24 and to say to(wards) me these house: home [the] to boil which to boil there to minister [the] house: home [obj] sacrifice [the] people
Munthuyo anandiwuza kuti, “Izi ndi zipinda zophikiramo. Mʼmenemu anthu otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzaphikiramo nyama za nsembe za anthu.”

< Ezekiel 46 >