< Ezekiel 37 >
1 to be upon me hand: power LORD and to come out: send me in/on/with spirit LORD and to rest me in/on/with midst [the] valley and he/she/it full bone
Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
2 and to pass me upon them around around and behold many much upon face: surface [the] valley and behold dry much
Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
3 and to say to(wards) me son: child man to live [the] bone [the] these and to say Lord YHWH/God you(m. s.) to know
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
4 and to say to(wards) me to prophesy upon [the] bone [the] these and to say to(wards) them [the] bone [the] dry to hear: hear word LORD
Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
5 thus to say Lord YHWH/God to/for bone [the] these behold I to come (in): come in/on/with you spirit: breath and to live
Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
6 and to give: put upon you sinew and to ascend: rise upon you flesh and to cover upon you skin and to give: put in/on/with you spirit: breath and to live and to know for I LORD
Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
7 and to prophesy like/as as which to command and to be voice: sound like/as to prophesy I and behold quaking and to present: come bone bone to(wards) bone his
Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
8 and to see: see and behold upon them sinew and flesh to ascend: rise and to cover upon them skin from to/for above [to] and spirit: breath nothing in/on/with them
Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
9 and to say to(wards) me to prophesy to(wards) [the] spirit: breath to prophesy son: child man and to say to(wards) [the] spirit: breath thus to say Lord YHWH/God from four spirit: breath to come (in): come [the] spirit: breath and to breathe in/on/with to kill [the] these and to live
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
10 and to prophesy like/as as which to command me and to come (in): come in/on/with them [the] spirit: breath and to live and to stand: stand upon foot their strength: soldiers great: large much much
Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
11 and to say to(wards) me son: child man [the] bone [the] these all house: household Israel they(masc.) behold to say to wither bone our and to perish hope our to cut to/for us
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
12 to/for so to prophesy and to say to(wards) them thus to say Lord YHWH/God behold I to open [obj] grave your and to ascend: establish [obj] you from grave your people my and to come (in): bring [obj] you to(wards) land: soil Israel
Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
13 and to know for I LORD in/on/with to open I [obj] grave your and in/on/with to ascend: establish I [obj] you from grave your people my
Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
14 and to give: put spirit my in/on/with you and to live and to rest [obj] you upon land: soil your and to know for I LORD to speak: speak and to make: do utterance LORD
Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
15 and to be word LORD to(wards) me to/for to say
Yehova anandiyankhula kuti:
16 and you(m. s.) son: child man to take: take to/for you tree: stick one and to write upon him to/for Judah and to/for son: descendant/people Israel (companion his *Q(K)*) and to take: take tree: stick one and to write upon him to/for Joseph tree: stick Ephraim and all house: household Israel (companion his *Q(K)*)
“Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
17 and to present: come [obj] them one to(wards) one to/for you to/for tree: stick one and to be to/for one in/on/with hand your
Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
18 and like/as as which to say to(wards) you son: descendant/people people your to/for to say not to tell to/for us what? these to/for you
“Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
19 to speak: speak to(wards) them thus to say Lord YHWH/God behold I to take: take [obj] tree: stick Joseph which in/on/with hand Ephraim and tribe Israel (companion his *Q(K)*) and to give: put [obj] them upon him [obj] tree: stick Judah and to make them to/for tree: stick one and to be one in/on/with hand my
iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
20 and to be [the] tree: stick which to write upon them in/on/with hand your to/for eye their
Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
21 and to speak: speak to(wards) them thus to say Lord YHWH/God behold I to take: take [obj] son: descendant/people Israel from between: among [the] nation which to go: went there and to gather [obj] them from around and to come (in): bring [obj] them to(wards) land: soil their
udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
22 and to make [obj] them to/for nation one in/on/with land: country/planet in/on/with mountain: mount Israel and king one to be to/for all their to/for king and not (to be *Q(K)*) still to/for two nation and not to divide still to/for two kingdom still
Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
23 and not to defile still in/on/with idol their and in/on/with abomination their and in/on/with all transgression their and to save [obj] them from all seat their which to sin in/on/with them and be pure [obj] them and to be to/for me to/for people and I to be to/for them to/for God
Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
24 and servant/slave my David king upon them and to pasture one to be to/for all their and in/on/with justice: judgement my to go: walk and statute my to keep: careful and to make: do [obj] them
“‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
25 and to dwell upon [the] land: country/planet which to give: give to/for servant/slave my to/for Jacob which to dwell in/on/with her father your and to dwell upon her they(masc.) and son: child their and son: child son: child their till forever: enduring and David servant/slave my leader to/for them to/for forever: enduring
Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
26 and to cut: make(covenant) to/for them covenant peace covenant forever: enduring to be with them and to give: put them and to multiply [obj] them and to give: put [obj] sanctuary my in/on/with midst their to/for forever: enduring
Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
27 and to be tabernacle my upon them and to be to/for them to/for God and they(masc.) to be to/for me to/for people
Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
28 and to know [the] nation for I LORD to consecrate: consecate [obj] Israel in/on/with to be sanctuary my in/on/with midst their to/for forever: enduring
Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”