< Exodus 1 >

1 and these name son: child Israel [the] to come (in): come Egypt [to] with Jacob man: anyone and house: household his to come (in): come
Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
2 Reuben Simeon Levi and Judah
Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
3 Issachar Zebulun and Benjamin
Isakara, Zebuloni, Benjamini;
4 Dan and Naphtali Gad and Asher
Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
5 and to be all soul: person to come out: produce thigh Jacob seventy soul: person and Joseph to be in/on/with Egypt
Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
6 and to die Joseph and all brother: male-sibling his and all [the] generation [the] he/she/it
Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
7 and son: descendant/people Israel be fruitful and to swarm and to multiply and be vast in/on/with much much and to fill [the] land: country/planet with them
Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
8 and to arise: rise king new upon Egypt which not to know [obj] Joseph
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
9 and to say to(wards) people his behold people son: descendant/people Israel many and mighty from us
Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
10 to give [emph?] be wise to/for him lest to multiply and to be for to encounter: chanced battle and to add also he/she/it upon to hate us and to fight in/on/with us and to ascend: rise from [the] land: country/planet
Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
11 and to set: appoint upon him ruler taskworker because to afflict him in/on/with burden their and to build city storage to/for Pharaoh [obj] Pithom and [obj] Raamses
Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
12 and like/as as which to afflict [obj] him so to multiply and so to break through and to loathe from face: because son: descendant/people Israel
Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
13 and to serve Egyptian [obj] son: descendant/people Israel in/on/with severity
ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
14 and to provoke [obj] life their in/on/with service severe in/on/with clay and in/on/with brick and in/on/with all service: work in/on/with land: country [obj] all service: work their which to serve in/on/with them in/on/with severity
Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
15 and to say king Egypt to/for to beget [the] Hebrew which name [the] one Shiphrah and name [the] second Puah
Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
16 and to say in/on/with to beget you [obj] [the] Hebrew and to see: see upon [the] wheel if son: child he/she/it and to die [obj] him and if daughter he/she/it and to live
“Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
17 and to fear: revere [the] to beget [obj] [the] God and not to make: do like/as as which to speak: speak to(wards) them king Egypt and to live [obj] [the] youth
Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
18 and to call: call to king Egypt to/for to beget and to say to/for them why? to make: do [the] word: thing [the] this and to live [obj] [the] youth
Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
19 and to say [the] to beget to(wards) Pharaoh for not like/as woman [the] Egyptian [the] Hebrew for vigorous they(fem.) in/on/with before to come (in): come to(wards) them [the] to beget and to beget
Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
20 and be good God to/for to beget and to multiply [the] people and be vast much
Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
21 and to be for to fear: revere [the] to beget [obj] [the] God and to make: offer to/for them house: household
Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
22 and to command Pharaoh to/for all people his to/for to say all [the] son: child [the] born [the] Nile [to] to throw him and all [the] daughter to live [emph?]
Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”

< Exodus 1 >