< Exodus 3 >

1 and Moses to be to pasture [obj] flock Jethro relative his priest Midian and to lead [obj] [the] flock after [the] wilderness and to come (in): come to(wards) mountain: mount [the] God Horeb [to]
Tsono Mose amaweta ziweto za mpongozi wake Yetero, wansembe uja wa ku Midiyani. Tsiku lina iye anazitsogolera kupita ku chipululu ndipo anafika ku phiri la Mulungu lotchedwa Horebu.
2 and to see: see messenger: angel LORD to(wards) him in/on/with flame fire from midst [the] bush and to see: see and behold [the] bush to burn: burn in/on/with fire and [the] bush nothing he to eat
Kumeneko mngelo wa Yehova anaonekera kwa iye mʼmalawi amoto mʼchitsamba. Mose anaona kuti ngakhale chitsambacho chimayaka koma sichimanyeka.
3 and to say Moses to turn aside: turn aside please and to see: see [obj] [the] appearance [the] great: large [the] this why? not to burn: burn [the] bush
Tsono Mose anati mu mtima mwake, “Ine ndipita komweko ndikaone zodabwitsazi, chitsamba sichikunyeka chifukwa chiyani?”
4 and to see: see LORD for to turn aside: turn aside to/for to see: see and to call: call out to(wards) him God from midst [the] bush and to say Moses Moses and to say behold I
Yehova ataona kuti Mose anapatuka kuti adzaonetsetse, Mulungu anamuyitana Mose kuchokera mʼchitsambamo nati, “Mose! Mose!” Ndipo anayankha, “Wawa.”
5 and to say not to present: come here to slip sandal your from upon foot your for [the] place which you(m. s.) to stand: stand upon him land: soil holiness he/she/it
Mulungu anati, “Usayandikire kuno. Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.”
6 and to say I God father your God Abraham God Isaac and God Jacob and to hide Moses face his for to fear from to look to(wards) [the] God
Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.” Atamva zimenezi, Mose anaphimba nkhope yake chifukwa anaopa kuona Mulungu.
7 and to say LORD to see: see to see: see [obj] affliction people my which in/on/with Egypt and [obj] cry their to hear: hear from face: because to oppress him for to know [obj] pain his
Yehova anati, “Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo chifukwa cha anthu amene akuwapsinja, ndipo ndakhudzidwa ndi masautso awo.
8 and to go down to/for to rescue him from hand: power Egypt and to/for to ascend: establish him from [the] land: country/planet [the] he/she/it to(wards) land: country/planet pleasant and broad: wide to(wards) land: country/planet to flow: flowing milk and honey to(wards) place [the] Canaanite and [the] Hittite and [the] Amorite and [the] Perizzite and [the] Hivite and [the] Jebusite
Choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse mʼdzanja la Aigupto, kuwatulutsa mʼdzikolo ndi kukawalowetsa mʼdziko labwino ndi lalikulu, dziko loyenda mkaka ndi uchi, kwawo kwa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
9 and now behold cry son: descendant/people Israel to come (in): come to(wards) me and also to see: see [obj] [the] oppression which Egyptian to oppress [obj] them
Ine ndamva ndithu kulira kwa Aisraeli, ndipo ndaona mmene Aigupto akuwazunzira.
10 and now to go: come! [emph?] and to send: depart you to(wards) Pharaoh and to come out: send [obj] people my son: descendant/people Israel from Egypt
Kotero tsopano, pita. Ine ndikukutuma kwa Farao kuti ukatulutse anthu anga, Aisraeli mʼdziko la Igupto.”
11 and to say Moses to(wards) [the] God who? I for to go: went to(wards) Pharaoh and for to come out: send [obj] son: descendant/people Israel from Egypt
Koma Mose anafunsa Mulungu, “Ine ndine yani kuti ndipite kwa Farao ndi kukatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto?”
12 and to say for to be with you and this to/for you [the] sign: miraculous for I to send: depart you in/on/with to come out: send you [obj] [the] people from Egypt to serve: minister [emph?] [obj] [the] God upon [the] mountain: mount [the] this
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro kwa iwe kuti ndine amene ndakutuma; Ukadzatulutsa anthu anga mʼdziko la Igupto, udzapembedza Mulungu pa phiri lino.”
13 and to say Moses to(wards) [the] God behold I to come (in): come to(wards) son: descendant/people Israel and to say to/for them God father your to send: depart me to(wards) you and to say to/for me what? name his what? to say to(wards) them
Mose anati kwa Mulungu, “Ngati ndipita kwa Aisraeli ndi kukawawuza kuti, ‘Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu,’ ndipo iwo nʼkukandifunsa kuti ‘Dzina lake ndi ndani?’ Tsono ine ndikawawuze chiyani?”
14 and to say God to(wards) Moses to be which to be and to say thus to say to/for son: descendant/people Israel to be to send: depart me to(wards) you
Mulungu anati kwa Mose, “NDINE AMENE NDILI. Izi ndi zimene ukanene kwa Aisraeli: ‘NDINE wandituma kwa inu.’”
15 and to say still God to(wards) Moses thus to say to(wards) son: descendant/people Israel LORD God father your God Abraham God Isaac and God Jacob to send: depart me to(wards) you this name my to/for forever: enduring and this memorial my to/for generation generation
Mulungu anatinso kwa Mose, “Ukanene kwa Aisraeli kuti ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo, wandituma kwa inu.’ Ili ndilo dzina langa mpaka muyaya, ndipo mibado ya mʼtsogolomo izidzanditchula ndi dzina limeneli.
16 to go: went and to gather [obj] old: elder Israel and to say to(wards) them LORD God father your to see: see to(wards) me God Abraham Isaac and Jacob to/for to say to reckon: visit to reckon: visit [obj] you and [obj] [the] to make: do to/for you in/on/with Egypt
“Pita, ukawasonkhanitse akuluakulu a Israeli ndipo ukati kwa iwo, ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, anandionekera ndipo akuti Iye wadzakuyenderani ndipo waona mmene Aigupto akukuzunzirani.
17 and to say to ascend: establish [obj] you from affliction Egypt to(wards) land: country/planet [the] Canaanite and [the] Hittite and [the] Amorite and [the] Perizzite and [the] Hivite and [the] Jebusite to(wards) land: country/planet to flow: flowing milk and honey
Choncho wanenetsa kuti adzakutulutsani mʼdziko la Igupto, dziko la masautsoli kupita ku dziko la Akanaani, Ahiti, Aamori Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’
18 and to hear: hear to/for voice your and to come (in): come you(m. s.) and old: elder Israel to(wards) king Egypt and to say to(wards) him LORD God [the] Hebrew to meet upon us and now to go: went please way: journey three day in/on/with wilderness and to sacrifice to/for LORD God our
“Akuluakulu a Israeli akakumvera. Kenaka iwe ndi akuluakuluwo mukapite kwa mfumu ya Igupto ndipo mukanene kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri, wakumana nafe. Tsono tikukupemphani kuti mutilole tipite pa ulendo wa masiku atatu mʼchipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu.’
19 and I to know for not to give: allow [obj] you king Egypt to/for to go: went and not in/on/with hand: power strong
Koma Ine ndikudziwa kuti mfumu ya Igupto sikakulolani kuti mupite pokhapokha Ine nditayikakamiza.
20 and to send: reach [obj] hand my and to smite [obj] Egyptian in/on/with all to wonder my which to make: do in/on/with entrails: among his and after so to send: reach [obj] you
Tsono Ine ndidzatambasula dzanja langa ndi kukantha Aigupto ndi zodabwitsa zanga zimene ndidzazichita pakati pawo. Zikadzatha izi, Iye adzakulolani kuti mupite.
21 and to give: give [obj] favor [the] people [the] this in/on/with eye: seeing Egyptian and to be for to go: went [emph?] not to go: went emptily
“Ndipo ine ndidzafewetsa mtima wa Aigupto pa anthu anga, kotero kuti mukadzatuluka simudzapita wopanda kanthu.
22 and to ask woman from neighboring her and from to sojourn house: home her article/utensil silver: money and article/utensil gold and mantle and to set: put upon son: child your and upon daughter your and to rescue [obj] Egyptian
Mkazi aliyense adzapemphe Mwigupto woyandikana naye ndiponso mkazi amene akukhala mʼnyumba yake, kuti amupatse ziwiya za siliva ndi golide ndiponso zovala zimene mudzaveka ana anu aamuna ndi aakazi. Ndipo potero mudzawalanda zonse Aiguptowo.”

< Exodus 3 >