< Exodus 17 >

1 and to set out all congregation son: descendant/people Israel from wilderness Sin to/for journey their upon lip: word LORD and to camp in/on/with Rephidim and nothing water to/for to drink [the] people
Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku chipululu cha Sini, ndi kumayenda malo ndi malo monga momwe anawalamulira Yehova. Iwo anamanga misasa yawo ku Refidimu koma kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa.
2 and to contend [the] people with Moses and to say to give: give to/for us water and to drink and to say to/for them Moses what? to contend [emph?] with me me what? to test [emph?] [obj] LORD
Kotero iwo anakangana ndi Mose nati, “Tipatse madzi akumwa.” Mose anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukukangana ndi ine? Chifukwa chiyani mukumuyesa Yehova?”
3 and to thirst there [the] people to/for water and to grumble [the] people upon Moses and to say to/for what? this to ascend: establish us from Egypt to/for to die [obj] me and [obj] son: child my and [obj] livestock my in/on/with thirst
Koma anthu anali ndi ludzu pamenepo ndipo anangʼungʼudza pamaso pa Mose namufunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto kuti ife, ana athu pamodzi ndi ziweto zathu tife ndi ludzu?”
4 and to cry Moses to(wards) LORD to/for to say what? to make: do to/for people [the] this still little and to stone me
Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, “Kodi ndichite chiyani ndi anthu awa? Iwo atsala pangʼono kundigenda ndi miyala.”
5 and to say LORD to(wards) Moses to pass to/for face: before [the] people and to take: take with you from old: elder Israel and tribe: rod your which to smite in/on/with him [obj] [the] Nile to take: take in/on/with hand your and to go: went
Yehova anati kwa Mose, “Pita patsogolo pa anthuwo. Tenga ndodo imene unamenyera nyanja ya Nailo pamodzi ndi akuluakulu ena a Israeli ndi kunyamuka.
6 look! I to stand: stand to/for face: before your there upon [the] rock in/on/with Horeb and to smite in/on/with rock and to come out: come from him water and to drink [the] people and to make: do so Moses to/for eye: seeing old: elder Israel
Ine ndidzayima patsogolo pako pafupi ndi thanthwe la ku Horebu. Ukamenye thanthwelo, madzi adzatuluka kuti anthu amwe.” Motero Mose anachita zimenezi pamaso pa akuluakulu a Israeli.
7 and to call: call by name [the] place Massah and Meribah upon strife son: descendant/people Israel and upon to test they [obj] LORD to/for to say there LORD in/on/with entrails: among our if nothing
Ndipo iye anatcha malowo Masa ndi Meriba chifukwa Aisraeli anakangana ndi kuyesa Yehova ponena kuti, “Kodi pakati pathu pali Yehova kapena palibe?”
8 and to come (in): come Amalek and to fight with Israel in/on/with Rephidim
Amaleki anabwera ku Refidimu kudzamenyana ndi Aisraeli.
9 and to say Moses to(wards) Joshua to choose to/for us human and to come out: come to fight in/on/with Amalek tomorrow I to stand upon head: top [the] hill and tribe: rod [the] God in/on/with hand my
Mose anati kwa Yoswa, “Sankha amuna amphamvu ndipo upite ukamenyane ndi Amaleki. Mawa ndidzayima pamwamba pa phiri nditagwira ndodo ya Mulungu.”
10 and to make: do Joshua like/as as which to say to/for him Moses to/for to fight in/on/with Amalek and Moses Aaron and Hur to ascend: rise head: top [the] hill
Ndipo Yoswa anachitadi monga Mose anamulamulira. Iye anapita kukamenyana ndi Aamaleki ndipo Mose, Aaroni ndi Huri anapita pamwamba pa phiri.
11 and to be like/as as which to exalt Moses hand his and to prevail Israel and like/as as which to rest hand his and to prevail Amalek
Mose ankati akakweza manja ake, Aisraeli amapambana, koma akatsitsa manja akewo Amaleki amapambana.
12 and hand Moses heavy and to take: take stone and to set: put underneath: under him and to dwell upon her and Aaron and Hur to grasp in/on/with hand his from this one and from this one and to be hand his faithfulness till to come (in): (sun)set [the] sun
Manja a Mose atatopa, Aaroni ndi Huri anatenga mwala ndi kuyika pansi ndipo Mose anakhalapo. Aaroni ndi Huri anagwirizitsa manja a Mose wina mbali ina winanso mbali ina. Choncho manja a Mose analimba mpaka kulowa kwa dzuwa.
13 and to weaken Joshua [obj] Amalek and [obj] people his to/for lip: edge sword
Kotero Yoswa anagonjetsa asilikali ankhondo a Amaleki ndi lupanga.
14 and to say LORD to(wards) Moses to write this memorial in/on/with scroll: book and to set: make in/on/with ear Joshua for to wipe to wipe [obj] memorial Amalek from underneath: under [the] heaven
Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Lemba izi mʼbuku kuti zidzakumbukirike ndipo uwonetsetse kuti Yoswa amve zimenezi, chifukwa Ine ndidzafafaniziratu Amaleki pa dziko lapansi, kotero kuti palibe amene adzawakumbukire.”
15 and to build Moses altar and to call: call by name his LORD Banner my
Mose anamanga guwa lansembe ndipo analitcha Yehova Chipambano Changa (Yehova Nisi).
16 and to say for hand upon throne LORD battle to/for LORD in/on/with Amalek from generation generation
Ndipo anati, “Kwezani mbendera ya Yehova. Yehova adzachitabe nkhondo ndi mibado yonse ya Aamaleki.”

< Exodus 17 >