< Deuteronomy 7 >
1 for to come (in): bring you LORD God your to(wards) [the] land: country/planet which you(m. s.) to come (in): come there [to] to/for to possess: take her and to slip nation many from face: before your [the] Hittite and [the] Girgashite and [the] Amorite and [the] Canaanite and [the] Perizzite and [the] Hivite and [the] Jebusite seven nation many and mighty from you
Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu;
2 and to give: give them LORD God your to/for face: before your and to smite them to devote/destroy to devote/destroy [obj] them not to cut: make(covenant) to/for them covenant and not be gracious them
Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo.
3 and not be related in/on/with them daughter your not to give: give to/for son: child his and daughter his not to take: take to/for son: child your
Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi.
4 for to turn aside: depart [obj] son: child your from after me and to serve: minister God another and to be incensed face: anger LORD in/on/with you and to destroy you quickly
Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu.
5 for if: except thus to make: do to/for them altar their to tear and pillar their to break and Asherah their to cut down/off [emph?] and idol their to burn [emph?] in/on/with fire
Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto.
6 for people holy you(m. s.) to/for LORD God your in/on/with you to choose LORD God your to/for to be to/for him to/for people possession from all [the] people which upon face: surface [the] land: planet
Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.
7 not from to multiply you from all [the] people to desire LORD in/on/with you and to choose in/on/with you for you(m. p.) [the] little from all [the] people
Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse.
8 for from love LORD [obj] you (and from to keep: obey he *L(abh)*) [obj] [the] oath which to swear to/for father your to come out: send LORD [obj] you in/on/with hand: power strong and to ransom you from house: home servant/slave from hand: power Pharaoh king Egypt
Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto.
9 and to know for LORD God your he/she/it [the] God [the] God [the] be faithful to keep: obey [the] covenant and [the] kindness to/for to love: lover him and to/for to keep: obey (commandment his *Q(K)*) to/for thousand generation
Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake.
10 and to complete to/for to hate him to(wards) face his to/for to perish him not to delay to/for to hate him to(wards) face his to complete to/for him
Koma iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo; sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.
11 and to keep: careful [obj] [the] commandment and [obj] [the] statute: decree and [obj] [the] justice: judgement which I to command you [the] day to/for to make: do them
Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.
12 and to be consequence to hear: hear [emph?] [obj] [the] justice: judgement [the] these and to keep: obey and to make: do [obj] them and to keep: obey LORD God your to/for you [obj] [the] covenant and [obj] [the] kindness which to swear to/for father your
Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu.
13 and to love: lover you and to bless you and to multiply you and to bless fruit belly: womb your and fruit land: soil your grain your and new wine your and oil your offspring cattle your and young flock your upon [the] land: soil which to swear to/for father your to/for to give: give to/for you
Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu.
14 to bless to be from all [the] people not to be in/on/with you barren and barren and in/on/with animal your
Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka.
15 and to turn aside: remove LORD from you all sickness and all disease Egypt [the] bad: evil which to know not to set: put them in/on/with you and to give: put them in/on/with all to hate you
Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu.
16 and to eat [obj] all [the] people which LORD God your to give: give to/for you not to pity eye your upon them and not to serve: minister [obj] God their for snare he/she/it to/for you
Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.
17 for to say in/on/with heart your many [the] nation [the] these from me how? be able to/for to possess: take them
Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?”
18 not to fear from them to remember to remember [obj] which to make: do LORD God your to/for Pharaoh and to/for all Egypt
Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense.
19 [the] trial [the] great: large which to see: see eye your and [the] sign: miraculous and [the] wonder and [the] hand: power [the] strong and [the] arm [the] to stretch which to come out: send you LORD God your so to make: do LORD God your to/for all [the] people which you(m. s.) afraid from face of their
Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano.
20 and also [obj] [the] hornet to send: depart LORD God your in/on/with them till to perish [the] to remain and [the] to hide from face of your
Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani.
21 not to tremble from face of their for LORD God your in/on/with entrails: among your God great: large and to fear: revere
Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa.
22 and to slip LORD God your [obj] [the] nation [the] these from face: before your little little not be able to end: finish them quickly lest to multiply upon you living thing [the] land: wildlife
Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani.
23 and to give: give them LORD God your to/for face: before your and to confuse them tumult great: large till to destroy they
Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa.
24 and to give: give king their in/on/with hand: power your and to perish [obj] name their from underneath: under [the] heaven not to stand man: anyone in/on/with face: before your till to destroy you [obj] them
Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga.
25 idol God their to burn [emph?] in/on/with fire not to desire silver: money and gold upon them and to take: take to/for you lest to snare in/on/with him for abomination LORD God your he/she/it
Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo.
26 and not to come (in): bring abomination to(wards) house: home your and to be devoted thing like him to detest to detest him and to abhor to abhor him for devoted thing he/she/it
Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.