< Deuteronomy 12 >

1 these [the] statute: decree and [the] justice: judgement which to keep: careful [emph?] to/for to make: do in/on/with land: country/planet which to give: give LORD God father your to/for you to/for to possess: take her all [the] day which you(m. p.) alive upon [the] land: planet
Awa ndi malangizo ndi malamulo amene muyenera kusamalitsanso kuti muwatsatire mʼdziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani kuti mutenge pa nthawi yonse imene muti mudzakhale mʼdzikomo.
2 to perish to perish [emph?] [obj] all [the] place which to serve: minister there [the] nation which you(m. p.) to possess: take [obj] them [obj] God their upon [the] mountain: mount [the] to exalt and upon [the] hill and underneath: under all tree luxuriant
Muwonongeretu kwathunthu malo onse a pamwamba pa mapiri ataliatali ndi pa mapiri angʼonoangʼono ndi pansi pa mtengo uliwonse wotambalala pamene mitundu imene muyilande dzikolo ankapembedzerapo milungu yawo.
3 and to tear [obj] altar their and to break [obj] pillar their and Asherah their to burn [emph?] in/on/with fire and idol God their to cut down/off [emph?] and to perish [obj] name their from [the] place [the] he/she/it
Mugumule maguwa awo ansembe, ndi kuphwanya miyala yawo yachipembedzo ndipo mutenthe pa moto mafano awo a Asera: mugwetse mafano a milungu yawo ndi kufafaniza mayina awo mʼmalo amenewo.
4 not to make: offer [emph?] so to/for LORD God your
Musapembedze Yehova Mulungu wanu monga mmene amachitira iwowa.
5 that if: except if: except to(wards) [the] place which to choose LORD God your from all tribe your to/for to set: put [obj] name his there to/for to dwell his to seek and to come (in): come there [to]
Koma inu muzifunafuna kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu kuti ayikeko dzina lake ndi kukhalako. Ku malo amenewa muyenera kupitako.
6 and to come (in): bring there [to] burnt offering your and sacrifice your and [obj] tithe your and [obj] contribution hand: themselves your and vow your and voluntariness your and firstborn cattle your and flock your
Kumeneko muzipititsako zopereka zanu ndi nsembe zanu zopsereza, ndi chakhumi chanu ndi mphatso zapadera zimene munalonjeza kupereka ndi zopereka zanu zaufulu ndi ana oyamba a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu.
7 and to eat there to/for face: before LORD God your and to rejoice in/on/with all sending hand: undertake your you(m. p.) and house: household your which to bless you LORD God your
Kumeneko, pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi mabanja anu mudzadya ndi kusangalalako pa china chilichonse chimene mudzakhudza, chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani.
8 not to make: do [emph?] like/as all which we to make: do here [the] day man: anyone all [the] upright in/on/with eye: appearance his
Musadzachite monga tikuchitira lero lino, aliyense kumachita zimene akuona kuti ndi zoyenera,
9 for not to come (in): come till now to(wards) [the] resting and to(wards) [the] inheritance which LORD God your to give: give to/for you
pakuti simunafike ku malo opumulirako ndi ku cholowa chimene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
10 and to pass [obj] [the] Jordan and to dwell in/on/with land: country/planet which LORD God your to inherit [obj] you and to rest to/for you from all enemy your from around and to dwell security
Koma mudzawoloka Yorodani ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, ndipo Iye adzakupatsani inu mpumulo ku adani anu okuzungulirani kuti mukhale motchinjirizidwa.
11 and to be [the] place which to choose LORD God your in/on/with him to/for to dwell name his there there [to] to come (in): bring [obj] all which I to command [obj] you burnt offering your and sacrifice your tithe your and contribution hand: themselves your and all best vow your which to vow to/for LORD
Tsono kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuti azikhalako muzikabweretsako chilichonse chimene ndikulamulirani inu: zopereka ndi nsembe zanu zopsereza, chakhumi chanu ndi mphatso zapadera, ndi chuma chanu chonse chosankhika chimene munalonjeza kwa Yehova.
12 and to rejoice to/for face: before LORD God your you(m. p.) and son: child your and daughter your and servant/slave your and maidservant your and [the] Levi which in/on/with gate: town your for nothing to/for him portion and inheritance with you
Ndipo kumeneko inu mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamodzi ndi ana anu aamuna ndi ana anu aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi a mʼmidzi yanu, amene alibe gawo kapena cholowa chawochawo.
13 to keep: careful to/for you lest to ascend: offer up burnt offering your in/on/with all place which to see: see
Musamalitse kuti musakaphere nsembe zanu zopsereza paliponse pamene mungafune.
14 that if: except if: except in/on/with place which to choose LORD in/on/with one tribe your there to ascend: offer up burnt offering your and there to make: do all which I to command you
Mukaphere pa malo okhawo amene Yehova adzawasankhe mwa limodzi la mafuko anu, ndipo kumeneko mukasunge chilichonse chimene ndikulamulireni.
15 except in/on/with all desire soul: myself your to sacrifice and to eat flesh like/as blessing LORD God your which to give: give to/for you in/on/with all gate: town your [the] unclean and [the] pure to eat him like/as gazelle and like/as deer
Koma mukhoza kumapha ziweto zanu mʼmizinda iliyonse ndi kudya nyama yake mmene mungafunire, ngati kuti ndi agwape kapena mbawala, monga mwadalitso limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Woyeretsedwa ndi wosayeretsedwa akhoza kuyidya.
16 except [the] blood not to eat upon [the] land: soil to pour: pour him like/as water
Koma musamadye magazi. Muziwathira pansi ngati madzi.
17 not be able to/for to eat in/on/with gate: town your tithe grain your and new wine your and oil your and firstborn cattle your and flock your and all vow your which to vow and voluntariness your and contribution hand: themselves your
Musamadyere mʼmizinda yanu chakhumi cha tirigu wanu ndi vinyo watsopano ndi mafuta, kapena za ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu, kapena chilichonse chimene mwalonjeza kuchipereka, nsembe zanu zaufulu, kapena mphatso zapadera,
18 that if: except if: except to/for face: before LORD God your to eat him in/on/with place which to choose LORD God your in/on/with him you(m. s.) and son: child your and daughter your and servant/slave your and maidservant your and [the] Levi which in/on/with gate: town your and to rejoice to/for face: before LORD God your in/on/with all sending hand: undertake your
mʼmalo mwake, muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhira inu, ana anu aamuna ndi aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi ochokera mʼmizinda yanu, ndipo mudzasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa chilichonse chimene mudzachikhudza.
19 to keep: careful to/for you lest to leave: neglect [obj] [the] Levi all day: always your upon land: soil your
Muonetsetse kuti musawataye Alevi pa masiku onse amene mukhale mʼdziko lanumo.
20 for to enlarge LORD God your [obj] border: area your like/as as which to speak: promise to/for you and to say to eat flesh for to desire soul: appetite your to/for to eat flesh in/on/with all desire soul: appetite your to eat flesh
Yehova Mulungu wanu akadzakulitsa dziko lanu monga anakulonjezerani, ndipo mukapukwa nyama mumanena kuti, “Ndikufuna nyama,” pamenepo mudzadya mmene mungafunire.
21 for to remove from you [the] place which to choose LORD God your to/for to set: put name his there and to sacrifice from cattle your and from flock your which to give: give LORD to/for you like/as as which to command you and to eat in/on/with gate: town your in/on/with all desire soul: myself your
Ngati malo amene Yehova Mulungu wanu awasankha kuti ayike Dzina lake ali kutali kwambiri ndi inu, mukhoza kupha ziweto pakati pa ngʼombe ndi nkhosa zimene Yehova wakupatsani, monga ndinakulamulani, ndipo mʼmizinda yanuyanu mukhoza kuzidya mmene mungafunire.
22 surely like/as as which to eat [obj] [the] gazelle and [obj] [the] deer so to eat him [the] unclean and [the] pure together to eat him
Muzidye ngati mukudya gwape kapena mbawala. Onse oyeretsedwa monga mwa mwambo ndi osayeretsedwa omwe akhoza kudya.
23 except to strengthen: ensure to/for lest to eat [the] blood for [the] blood he/she/it [the] soul: life and not to eat [the] soul: life with [the] flesh
Koma muonetsetse kuti musadye magazi, chifukwa magazi ndi moyo, ndipo musamadye moyo pamodzi ndi nyama.
24 not to eat him upon [the] land: soil to pour: pour him like/as water
Inu musamadye magazi, muziwathira pansi ngati madzi.
25 not to eat him because be good to/for you and to/for son: child your after you for to make: do [the] upright in/on/with eye: seeing LORD
Musamadye magazi kuti zikuyendereni bwino inu pamodzi ndi ana anu a pambuyo panu, popeza mudzakhala mukuchita zoyenera pamaso pa Mulungu.
26 except holiness your which to be to/for you and vow your to lift: raise and to come (in): come to(wards) [the] place which to choose LORD
Koma mutenge zinthu zanu zoyeretsedwa ndi china chilichonse chimene munalumbira kupereka, ndi kupita kumalo kumene Yehova adzasankhe.
27 and to make: offer burnt offering your [the] flesh and [the] blood upon altar LORD God your and blood sacrifice your to pour: pour upon altar LORD God your and [the] flesh to eat
Mupereke nsembe zanu zopsereza pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, nyama pamodzi ndi magazi omwe. Magazi a nsembe zanu athiridwe pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyamayo mukhoza kudya.
28 to keep: careful and to hear: obey [obj] all [the] word [the] these which I to command you because be good to/for you and to/for son: child your after you till forever: enduring for to make: do [the] pleasant and [the] upright in/on/with eye: seeing LORD God your
Onetsetsani kuti muzimvera mawu onsewa amene ndikukupatsani kuti zinthu zizikuyenderani bwino nthawi zonse inu ndi ana anu chifukwa mudzakhala mukuchita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 for to cut: eliminate LORD God your [obj] [the] nation which you(m. s.) to come (in): come there [to] to/for to possess: take [obj] them from face: before your and to possess: take [obj] them and to dwell in/on/with land: country/planet their
Yehova Mulungu wanu adzachotsa pamaso panu mitundu ya anthu amene mukufuna kuwathira nkhondo ndi kuwalanda dzikolo. Koma mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼdziko lawo,
30 to keep: careful to/for you lest to snare after them after to destroy they from face: before your and lest to seek to/for God their to/for to say how? to serve: minister [the] nation [the] these [obj] God their and to make: do so also I
ndipo pamene iwo awonongeka pamaso panu, samalirani kuti musakodwe mu msampha pa kufufuza za milungu yawo, nʼkumati, “Kodi anthu a mitunduwa amatumikira bwanji milungu yawo? Ifenso tichita momwemo.”
31 not to make: offer so to/for LORD God your for all abomination LORD which to hate to make: do to/for God their for also [obj] son: child their and [obj] daughter their to burn in/on/with fire to/for God their
Musapembedze Yehova Mulungu wanu momwe amachitira iwowo, chifukwa popembedza milungu yawoyo amachita zonyansa zamitundumitundu zimene Yehova amadana nazo. Amatentha ngakhale ana awo aamuna ndi aakazi pa moto ngati nsembe za kwa milungu yawo.
32 [obj] all [the] word: thing which I to command [obj] you [obj] him to keep: careful to/for to make: do not to add upon him and not to dimish from him
Onetsetsani kuti mukuchita zimene ndikukulamulirani. Musawonjezerepo kapena kuchotserapo.

< Deuteronomy 12 >