< 2 Samuel 24 >
1 and to add: again face: anger LORD to/for to be incensed in/on/with Israel and to incite [obj] David in/on/with them to/for to say to go: went to count [obj] Israel and [obj] Judah
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 and to say [the] king to(wards) Joab ruler [the] strength: soldiers which with him to rove please in/on/with all tribe Israel from Dan and till Beersheba Beersheba and to reckon: list [obj] [the] people and to know [obj] number [the] people
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 and to say Joab to(wards) [the] king and to add LORD God your to(wards) [the] people like/as them and like/as them hundred beat and eye lord my [the] king to see: see and lord my [the] king to/for what? to delight in in/on/with word: thing [the] this
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 and to strengthen: prevail over word [the] king to(wards) Joab and upon ruler [the] strength: soldiers and to come out: come Joab and ruler [the] strength: soldiers to/for face: before [the] king to/for to reckon: list [obj] [the] people [obj] Israel
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 and to pass [obj] [the] Jordan and to camp in/on/with Aroer right: south [the] city which in/on/with midst [the] torrent: valley [the] Gad and to(wards) Jazer
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
6 and to come (in): come [the] Gilead [to] and to(wards) land: country/planet Kadesh Kadesh and to come (in): come Dan [to] Jaan and around to(wards) Sidon
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 and to come (in): come fortification Tyre and all city [the] Hivite and [the] Canaanite and to come out: come to(wards) Negeb Judah Beersheba Beersheba
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 and to rove in/on/with all [the] land: country/planet and to come (in): come from end nine month and twenty day Jerusalem
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 and to give: give Joab [obj] number appointment [the] people to(wards) [the] king and to be Israel eight hundred thousand man strength to draw sword and man Judah five hundred thousand man
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 and to smite heart David [obj] him after so to recount [obj] [the] people and to say David to(wards) LORD to sin much which to make: do and now LORD to pass: bring please [obj] iniquity: crime servant/slave your for be foolish much
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 and to arise: rise David in/on/with morning and word LORD to be to(wards) Gad [the] prophet seer David to/for to say
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
12 to go: went and to speak: speak to(wards) David thus to say LORD three I to lift upon you to choose to/for you one from them and to make: do to/for you
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 and to come (in): come Gad to(wards) David and to tell to/for him and to say to/for him to come (in): come to/for you seven year famine in/on/with land: country/planet your if: surely no three month to flee you to/for face: before enemy your and he/she/it to pursue you and if: surely no to be three day pestilence in/on/with land: country/planet your now to know and to see: select what? to return: return to send: depart me word: speaking
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 and to say David to(wards) Gad distress to/for me much to fall: fall please in/on/with hand: power LORD for many (compassion his *Q(K)*) and in/on/with hand: power man not to fall: fall
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 and to give: give LORD pestilence in/on/with Israel from [the] morning and till time meeting: time appointed and to die from [the] people from Dan and till Beersheba Beersheba seventy thousand man
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 and to send: reach hand his [the] messenger: angel Jerusalem to/for to ruin her and to be sorry: relent LORD to(wards) [the] distress: harm and to say to/for messenger: angel [the] to ruin in/on/with people many now to slacken hand your and messenger: angel LORD to be with threshing floor ([the] Araunah *Q(K)*) [the] Jebusite
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 and to say David to(wards) LORD in/on/with to see: see he [obj] [the] messenger: angel [the] to smite in/on/with people and to say behold I ([the] to pasture *X*) to sin and I to pervert and these [the] flock what? to make: do to be please hand your in/on/with me and in/on/with house: household father my
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 and to come (in): come Gad to(wards) David in/on/with day [the] he/she/it and to say to/for him to ascend: rise to arise: raise to/for LORD altar in/on/with threshing floor (Araunah *Q(K)*) [the] Jebusite
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 and to ascend: rise David like/as word Gad like/as as which to command LORD
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 and to look Araunah and to see: see [obj] [the] king and [obj] servant/slave his to pass upon him and to come out: come Araunah and to bow to/for king face his land: soil [to]
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 and to say Araunah why? to come (in): come lord my [the] king to(wards) servant/slave his and to say David to/for to buy from from with you [obj] [the] threshing floor to/for to build altar to/for LORD and to restrain [the] plague from upon [the] people
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 and to say Araunah to(wards) David to take: take and to ascend: offer up lord my [the] king [the] pleasant (in/on/with eye: appearance his *Q(K)*) to see: behold! [the] cattle to/for burnt offering and [the] threshing sled and article/utensil [the] cattle to/for tree: wood
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 [the] all to give: give Araunah [the] king to/for king and to say Araunah to(wards) [the] king LORD God your to accept you
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 and to say [the] king to(wards) Araunah not for to buy to buy from [obj] you in/on/with price and not to ascend: offer up to/for LORD God my burnt offering for nothing and to buy David [obj] [the] threshing floor and [obj] [the] cattle in/on/with silver: money shekel fifty
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 and to build there David altar to/for LORD and to ascend: offer up burnt offering and peace offering and to pray LORD to/for land: country/planet and to restrain [the] plague from upon Israel
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.