< 2 Samuel 23 >

1 and these word David [the] last utterance David son: child Jesse and utterance [the] great man to arise: raise height anointed God Jacob and musical song Israel
Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
2 spirit LORD to speak: speak in/on/with me and speech his upon tongue my
“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
3 to say God Israel to/for me to speak: speak rock Israel to rule in/on/with man righteous to rule fear God
Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
4 and like/as light morning to rise sun morning not cloud from brightness from rain grass from land: soil
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
5 for not so house: household my with God for covenant forever: enduring to set: make to/for me to arrange in/on/with all and to keep: guard for all salvation my and all pleasure for not to spring
“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
6 and Belial like/as thorn to wander all their for not in/on/with hand to take: take
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
7 and man: anyone to touch in/on/with them to fill iron and tree: stake spear and in/on/with fire to burn to burn in/on/with seat
Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
8 these name [the] mighty man which to/for David Josheb-basshebeth Josheb-basshebeth Tahchemonite head: leader [the] officer he/she/it `wielded` ([the] Eznite *Q(K)*) upon eight hundred slain: killed in/on/with beat (one *Q(K)*)
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
9 (and after him *Q(k)*) Eleazar son: child (Dodo *Q(K)*) son: child Ahohite in/on/with three ([the] mighty man *Q(K)*) with David in/on/with to taunt they in/on/with Philistine to gather there to/for battle and to ascend: rise man Israel
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
10 he/she/it to arise: rise and to smite in/on/with Philistine till for be weary/toil hand: power his and to cleave hand: power his to(wards) [the] sword and to make: do LORD deliverance: victory great: large in/on/with day [the] he/she/it and [the] people: soldiers to return: return after him surely to/for to strip
Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
11 and after him Shammah son: child Agee Hararite and to gather Philistine to/for community and to be there portion [the] land: soil full lentil and [the] people: soldiers to flee from face: before Philistine
Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
12 and to stand in/on/with midst [the] portion and to rescue her and to smite [obj] Philistine and to make: do LORD deliverance: victory great: large
Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
13 and to go down (three *Q(K)*) from [the] thirty head: leader and to come (in): come to(wards) harvest to(wards) David to(wards) cave Adullam and community Philistine to camp in/on/with Valley (of Rephaim) (Valley of) Rephaim
Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
14 and David then in/on/with fortress and station Philistine then Bethlehem Bethlehem
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
15 and to desire David and to say who? to water: drink me water from cistern Bethlehem Bethlehem which in/on/with gate
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
16 and to break up/open three [the] mighty man in/on/with camp Philistine and to draw water from cistern Bethlehem Bethlehem which in/on/with gate and to lift: bear and to come (in): bring to(wards) David and not be willing to/for to drink them and to pour [obj] them to/for LORD
Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
17 and to say forbid to/for me LORD from to make: do I this blood [the] human [the] to go: went in/on/with soul: life their and not be willing to/for to drink them these to make: do three [the] mighty man
Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
18 and Abishai brother: male-sibling Joab son: child Zeruiah he/she/it head: leader ([the] three *Q(K)*) and he/she/it to rouse [obj] spear his upon three hundred slain: killed and to/for him name in/on/with three
Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
19 from [the] three for to honor: honour and to be to/for them to/for ruler and till [the] three not to come (in): come
Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
20 and Benaiah son: child Jehoiada son: warrior man (strength *Q(K)*) many work from Kabzeel he/she/it to smite [obj] two Ariel Moab and he/she/it to go down and to smite [obj] ([the] lion *Q(K)*) in/on/with midst [the] pit in/on/with day [the] snow
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
21 and he/she/it to smite [obj] man Egyptian (man *Q(K)*) appearance and in/on/with hand [the] Egyptian spear and to go down to(wards) him in/on/with tribe: staff and to plunder [obj] [the] spear from hand [the] Egyptian and to kill him in/on/with spear his
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
22 these to make: do Benaiah son: child Jehoiada and to/for him name in/on/with three [the] mighty man
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
23 from [the] thirty to honor: honour and to(wards) [the] three not to come (in): come and to set: appoint him David to(wards) guard his
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
24 Asahel Asahel brother: male-sibling Joab in/on/with thirty Elhanan son: child Dodo Bethlehem Bethlehem
Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
25 Shammah [the] Harodite Elika [the] Harodite
Sama Mharodi, Elika Mherodi,
26 Helez [the] Paltite Ira son: child Ikkesh [the] Tekoa
Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
27 Abiezer [the] Anathoth Mebunnai [the] Hushathite
Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
28 Zalmon [the] Ahohite Maharai [the] Netophathite
Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
29 Heleb son: child Baanah [the] Netophathite Ittai son: child Ribai from Gibeah son: descendant/people Benjamin
Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
30 Benaiah Pirathon Hiddai from torrent: river Gaash
Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
31 Abi-albon Abi-albon [the] Arbathite Azmaveth [the] Bahurite
Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
32 Eliahba [the] Shaalbonite son: child Jashen Jonathan
Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
33 (son: child *X*) Shammah [the] Hararite Ahiam son: child Sharar [the] Hararite
mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
34 Eliphelet son: child Ahasbai son: child [the] Maacathite Eliam son: child Ahithophel [the] Gilonite
Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
35 (Hezro *Q(K)*) [the] Carmelite Paarai [the] Arbite
Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
36 Igal son: child Nathan from Zobah Bani [the] Gad
Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
37 Zelek [the] Ammon Naharai [the] Beerothite (to lift: bearing(armour) *Q(K)*) article/utensil Joab son: child Zeruiah
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
38 Ira [the] Ithrite Gareb [the] Ithrite
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
39 Uriah [the] Hittite all thirty and seven
ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.

< 2 Samuel 23 >