< 2 Samuel 18 >
1 and to reckon: list David [obj] [the] people: soldiers which with him and to set: appoint upon them ruler thousand and ruler hundred
Davide anasonkhanitsa anthu amene anali naye ndipo anasankha atsogoleri ena olamulira ankhondo 1,000 ndi ena olamulira ankhondo 100.
2 and to send: depart David [obj] [the] people: soldiers [the] third in/on/with hand: power Joab and [the] third in/on/with hand: power Abishai son: child Zeruiah brother: male-sibling Joab and [the] third in/on/with hand: power Ittai [the] Gittite and to say [the] king to(wards) [the] people: soldiers to come out: come to come out: come also I with you
Davide anatumiza asilikaliwo atawagawa patatu: gulu loyamba limalamulidwa ndi Yowabu, gulu lachiwiri limalamulidwa ndi Abisai ndipo gulu lachitatu limalamulidwa ndi Itai Mgiti. Mfumu inawuza asilikaliwo kuti, “Inenso ndipita nanu ndithu.”
3 and to say [the] people: soldiers not to come out: come for if to flee to flee not to set: consider to(wards) us heart and if to die half our not to set: consider to(wards) us heart for now like us ten thousand and now pleasant for to be to/for us from city (to/for to help *Q(K)*)
Koma anthuwo anati, “Inu musapite nafe. Ngati tidzathamangitsidwa, iwowo sadzasamala za ife. Ngakhale theka la ife litafa, iwo sadzasamalako. Koma inuyo ndinu ofunika kuposa asilikali 10,000. Nʼkwabwino kwambiri kuti inu muzititumizira chithandizo kuchokera ku mzindako.”
4 and to say to(wards) them [the] king which be good in/on/with eye: appearance your to make: do and to stand: stand [the] king to(wards) hand: to [the] gate and all [the] people: soldiers to come out: come to/for hundred and to/for thousand
Mfumu inayankha kuti, “Ine ndichita chimene chili chokukomerani.” Kotero mfumu inayima pambali pa chipata pamene ankhondo onse amayenda mʼmagulu a anthu 100 ndi a 1,000.
5 and to command [the] king [obj] Joab and [obj] Abishai and [obj] Ittai to/for to say to/for softly to/for me to/for youth to/for Absalom and all [the] people to hear: hear in/on/with to command [the] king [obj] all [the] ruler upon word: thing Absalom
Mfumu inalamulira Yowabu, Abisai ndi Itai kuti, “Mumukomere mtima Abisalomu chifukwa cha ine.” Ndipo asilikali onse anamva pamene mfumu imalamula izi za Abisalomu kwa wolamulira aliyense.
6 and to come out: come [the] people: soldiers [the] land: country to/for to encounter: toward Israel and to be [the] battle in/on/with (Ephraim) Forest (Forest of) Ephraim
Ankhondo anayenda kupita kukachita nkhondo ndi Israeli, ndipo nkhondo inachitika mʼnkhalango ya Efereimu.
7 and to strike there people: soldiers Israel to/for face: before servant/slave David and to be there [the] plague great: large in/on/with day [the] he/she/it twenty thousand
Aisraeli anagonjetsedwa kumeneko ndi ankhondo a Davide. Tsiku limenelo anaphedwa anthu okwanira 20,000.
8 and to be there [the] battle (to scatter *Q(K)*) upon face: surface all [the] land: country/planet and to multiply [the] wood to/for to eat in/on/with people from whence to eat [the] sword in/on/with day [the] he/she/it
Nkhondo inafalikira ku madera onse akumidzi ndipo anthu akufa chifukwa cha zoopsa za mʼnkhalango anali ambiri tsiku limenelo kuposa akufa ndi lupanga.
9 and to encounter: meet Absalom to/for face: before servant/slave David and Absalom to ride upon [the] mule and to come (in): come [the] mule underneath: under thicket [the] oak [the] great: large and to strengthen: hold head his in/on/with oak and to give: put between [the] heaven and between [the] land: country/planet and [the] mule which underneath: under him to pass
Tsono zinachitika kuti Abisalomu anakumana ndi asilikali a Davide. Iye anali atakwera bulu ndipo pamene buluyo amadutsa pansi pa nthambi zambiri za mtengo wa thundu, mutu wa Abisalomu unakodwa mu mtengomo. Iye anasiyidwa atatsakamira mʼmalele, pamene bulu amene anakwerapoyo amapitirira.
10 and to see: see man one and to tell to/for Joab and to say behold to see: see [obj] Absalom to hang in/on/with oak
Mmodzi mwa asilikali ataona zimenezi, anamuwuza Yowabu kuti, “Ine ndamuona Abisalomu ali lende mu mtengo wa thundu.”
11 and to say Joab to/for man [the] to tell to/for him and behold to see: see and why? not to smite him there land: soil [to] and upon me to/for to give: give to/for you ten silver: money and belt one
Yowabu anati kwa munthu amene anamuwuza zimenezi, “Ukuti chiyani! Unamuona? Nʼchifukwa chiyani sunamukanthire pansi pomwepo? Ndipo ine ndikanakupatsa ndalama za siliva khumi ndi lamba wausilikali.”
12 and to say [the] man to(wards) Joab (and if *Q(k)*) I to weigh upon palm my thousand silver: money not to send: reach hand my to(wards) son: child [the] king for in/on/with ear: hearing our to command [the] king [obj] you and [obj] Abishai and [obj] Ittai to/for to say to keep: guard who? in/on/with youth in/on/with Absalom
Koma munthuyo anayankha kuti, “Ngakhale atandipatsa mʼmanja mwanga ndalama zasiliva 1,000, sindingatambasule dzanja langa kupha mwana wa mfumu. Ife tikumva, mfumu inalamula inu Abisai ndiponso Itai kuti, ‘Mutetezeni mnyamatayo Abisalomu chifukwa cha ine!’
13 or to make: do (in/on/with soul: life my *Q(K)*) deception and all word: thing not to hide from [the] king and you(m. s.) to stand from before
Ndipo sindikanayika moyo wanga pa chiswe pakuti palibe chimene chimabisika pamaso pa mfumu komanso inu simukanditeteza.”
14 and to say Joab not so to wait: wait to/for face of your and to take: take three tribe: javelin in/on/with palm his and to blow them in/on/with heart Absalom still he alive in/on/with heart [the] oak
Yowabu anati, “Ine sinditayanso nthawi ndi iwe.” Ndipo anatenga mikondo itatu mʼmanja mwake ndipo anabaya pamtima pa Abisalomu, Abisalomuyo akanali ndi moyo pa mtengo wa thundu.
15 and to turn: surround ten youth to lift: bearing(armour) article/utensil Joab and to smite [obj] Absalom and to die him
Ndipo anthu khumi onyamula zida za Yowabu anazungulira Abisalomu, kumubaya ndi kumupha.
16 and to blow Joab in/on/with trumpet and to return: return [the] people: soldiers from to pursue after Israel for to withhold Joab [obj] [the] people: soldiers
Kenaka Yowabu analiza lipenga ndipo asilikali analeka kuthamangitsa Israeli pakuti Yowabu anawaletsa.
17 and to take: take [obj] Absalom and to throw [obj] him in/on/with wood to(wards) [the] pit [the] great: large and to stand upon him heap stone great: large much and all Israel to flee man: anyone (to/for tent: home his *Q(K)*)
Iwo anatenga Abisalomu ndi kumuponya mʼdzenje lalikulu mʼchipululumo ndipo anawunjikapo miyala ikuluikulu. Nthawiyi Aisraeli onse anathawa kupita ku nyumba zawo.
18 and Absalom to take: take and to stand to/for him (in/on/with life his *Q(K)*) [obj] pillar which in/on/with Valley (of Kings) [the] King's for to say nothing to/for me son: child in/on/with for the sake of to remember name my and to call: call by to/for pillar upon name his and to call: call by to/for her hand: themselves Absalom till [the] day: today [the] this
Abisalomu ali ndi moyo anadzimangira chipilala mʼchigwa cha mfumu, pakuti ankaganiza kuti, “Ine ndilibe mwana wamwamuna amene adzakhale chikumbutso changa.” Chipilalacho anachitchula dzina lake lomwe ndipo mpaka lero chimatchedwa chipilala cha Abisalomu.
19 and Ahimaaz son: child Zadok to say to run: run please and to bear tidings [obj] [the] king for to judge him LORD from hand: power enemy his
Tsono Ahimaazi mwana wa Zadoki anati, “Ndiloleni ndithamange ndi kukapereka uthenga kwa mfumu kuti Yehova wayipulumutsa mʼdzanja la adani ake.”
20 and to say to/for him Joab not man good news you(m. s.) [the] day [the] this and to bear tidings in/on/with day another and [the] day [the] this not to bear tidings for as that: since (as as *Q(K)*) son: child [the] king to die
Yowabu anamuwuza iye kuti, “Iwe si amene uti ukanene zimenezi lero. Ukapereka uthenga nthawi ina, koma usatero lero, chifukwa mwana wa mfumu wafa.”
21 and to say Joab to/for Ethiopian to go: went to tell to/for king which to see: see and to bow Ethiopian to/for Joab and to run: run
Kenaka Yowabu anawuza Mkusi kuti, “Pita ukawuze mfumu zimene waona.” Mkusiyo anawerama pamaso pa Yowabu ndipo anathamanga kupita.
22 and to add: again still Ahimaaz son: child Zadok and to say to(wards) Joab and to be what? to run: run please also I after [the] Ethiopian and to say Joab to/for what? this you(m. s.) to run: run son: child my and to/for you nothing good news to find
Ahimaazi mwana wa Zadoki ananenanso kwa Yowabu kuti, “Zivute zitani, chonde mundilole kuti ndipite pambuyo pa Mkusiyo.” Koma Yowabu anayankha kuti, “Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukufuna kupita? Ulibe nkhani yoti ukalandire nayo mphotho.”
23 and to be what? to run: run and to say to/for him to run: run and to run: run Ahimaaz way: road [the] talent and to pass [obj] [the] Ethiopian
Iye anati, “Zivute zitani ine ndikufuna kuti ndipite.” Choncho Yowabu anati “Pita!” Ndipo Ahimaazi anathamanga kudzera njira ya ku chigwa ndipo anamupitirira Mkusi uja.
24 and David to dwell between two [the] gate and to go: walk [the] to watch to(wards) roof [the] gate to(wards) [the] wall and to lift: look [obj] eye his and to see: see and behold man to run: run to/for alone him
Nthawi imeneyo nʼkuti Davide atakhala pakati pa zipata ziwiri, chakubwalo ndi chamʼkati. Mlonda anakwera pa khoma nakayimirira pa denga la chipata. Anati atayangʼana, anaona munthu akuthamanga yekhayekha.
25 and to call: call out [the] to watch and to tell to/for king and to say [the] king if to/for alone him good news in/on/with lip his and to go: come to go: come and approaching
Mlonda uja anapita kwa mfumu ndipo anafotokoza. Mfumu inati, “Ngati ali yekha ali ndi nkhani yabwino” Ndipo munthuyo anayandikira.
26 and to see: see [the] to watch man another to run: run and to call: call to [the] to watch to(wards) [the] gatekeeper and to say behold man to run: run to/for alone him and to say [the] king also this to bear tidings
Mlonda uja anaonanso munthu wina akuthamanga, ndipo anayitana woyangʼanira pa chipata, “Taona, munthu winanso akuthamanga ali yekha!” Mfumu inati, “Iye akubweretsanso nkhani yabwino.”
27 and to say [the] to watch I to see: examine [obj] running [the] first like/as running Ahimaaz son: child Zadok and to say [the] king man pleasant this and to(wards) good news pleasant to come (in): come
Mlonda uja anati, “Munthu akuthamanga patsogoloyo, kathamangidwe kake kakufanafana ndi mmene amathamangira Ahimaazi, mwana wa Zadoki.” Mfumu inati, “Ameneyo ndi munthu wabwino, ndipo akubwera ndi nkhani yabwino.”
28 and to call: call out Ahimaaz and to say to(wards) [the] king peace: well-being and to bow to/for king to/for face his land: soil [to] and to say to bless LORD God your which to shut [obj] [the] human which to lift: kindness [obj] hand their in/on/with lord my [the] king
Ndipo Ahimaazi anafuwula kwa mfumu, “Zonse zili bwino!” Iye anagwada pamaso pa mfumu nkhope yake atagunditsa pansi ndipo anati, “Yehova Mulungu wathu alemekezedwe! Iye wapereka mʼdzanja lathu anthu amene anawukira inu mbuye wanga mfumu.”
29 and to say [the] king peace: well-being to/for youth to/for Absalom and to say Ahimaaz to see: see [the] crowd [the] great: large to/for to send: depart [obj] servant/slave [the] king Joab and [obj] servant/slave your and not to know what?
Mfumu inafunsa, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Ahimaazi anayankha, “Pamene Yowabu amati azindituma ine mtumiki wanu ndinaona chipiringu cha anthu, koma sindikudziwa chinali chiyani.”
30 and to say [the] king to turn: turn to stand thus and to turn: turn and to stand: stand
Mfumu inati, “Ima apo ndipo udikire.” Kotero iye anapita pa mbali nayima pamenepo.
31 and behold [the] Ethiopian to come (in): come and to say [the] Ethiopian to bear tidings lord my [the] king for to judge you LORD [the] day from hand: power all [the] to arise: attack upon you
Kenaka Mkusi uja anafika ndipo anati, “Mbuye wanga mfumu imvani nkhani yabwino! Yehova wakupulumutsani inu lero kwa onse amene anakuwukirani.”
32 and to say [the] king to(wards) [the] Ethiopian peace: well-being to/for youth to/for Absalom and to say [the] Ethiopian to be like/as youth enemy lord my [the] king and all which to arise: attack upon you to/for distress: evil
Mfumu inafunsa Mkusiyo kuti, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Mkusiyo anayankha kuti, “Adani anu mbuye wanga mfumu, pamodzi ndi anthu onse amene amakuwukirani, ziwaonekere zomwe zamuonekera mnyamatayo.”
33 and to tremble [the] king and to ascend: rise upon upper room [the] gate and to weep and thus to say in/on/with to go: went he son: child my Absalom son: child my son: child my Absalom who? to give: if only! to die I I underneath: instead you Absalom son: child my son: child my
Mfumu inanthunthumira. Inapita ku chipinda cha mmwamba cha pa chipata kukalira. Pamene imapita, inkati: “Iwe mwana wanga Abisalomu! Mwana wanga! Mwana wanga Abisalomu! Zikanakhala bwino ndikanafa ndine mʼmalo mwako! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”