< 2 Samuel 16 >

1 and David to pass little from [the] head: top and behold Ziba youth Mephibosheth Mephibosheth to/for to encounter: meet him and pair donkey to saddle/tie and upon them hundred food: bread and hundred cluster and hundred summer and bag wine
Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
2 and to say [the] king to(wards) Ziba what? these to/for you and to say Ziba [the] donkey to/for house: household [the] king to/for to ride (and [the] food: bread *Q(K)*) and [the] summer to/for to eat [the] youth and [the] wine to/for to drink [the] weary in/on/with wilderness
Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
3 and to say [the] king and where? son: descendant/people lord your and to say Ziba to(wards) [the] king behold to dwell in/on/with Jerusalem for to say [the] day to return: return to/for me house: household Israel [obj] kingdom father my
Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
4 and to say [the] king to/for Ziba behold to/for you all which to/for Mephibosheth Mephibosheth and to say Ziba to bow to find favor in/on/with eye: seeing your lord my [the] king
Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
5 and to come (in): come [the] king David till Bahurim and behold from there man to come out: come from family house: household Saul and name his Shimei son: child Gera to come out: come to come out: come and to lighten
Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
6 and to stone in/on/with stone [obj] David and [obj] all servant/slave [the] king David and all [the] people and all [the] mighty man from right his and from left his
Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
7 and thus to say Shimei in/on/with to lighten he to come out: come to come out: come man [the] blood and man [the] Belial
Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
8 to return: pay upon you LORD all blood house: household Saul which to reign (underneath: instead him *Q(K)*) and to give: give LORD [obj] [the] kingship in/on/with hand: power Absalom son: child your and look! you in/on/with distress: evil your for man blood you(m. s.)
Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
9 and to say Abishai son: child Zeruiah to(wards) [the] king to/for what? to lighten [the] dog [the] to die [the] this [obj] lord my [the] king to pass please and to turn aside: remove [obj] head his
Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
10 and to say [the] king what? to/for me and to/for you son: child Zeruiah (thus *Q(K)*) to lighten (for *Q(K)*) LORD to say to/for him to lighten [obj] David and who? to say why? to make: do so
Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
11 and to say David to(wards) Abishai and to(wards) all servant/slave his behold son: descendant/people my which to come out: produce from belly my to seek [obj] soul: life my and also for now Benjaminite [the] Benjaminite to rest to/for him and to lighten for to say to/for him LORD
Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
12 perhaps to see: see LORD (in/on/with eye: sin my *Q(K)*) and to return: pay LORD to/for me welfare underneath: instead curse his [the] day: today [the] this
Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
13 and to go: went David and human his in/on/with way: road and Shimei to go: walk in/on/with side [the] mountain: mount to/for close him to go: went and to lighten and to stone in/on/with stone to/for close him and to throw in/on/with dust
Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
14 and to come (in): come [the] king and all [the] people which with him faint and be refreshed there
Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
15 and Absalom and all [the] people man Israel to come (in): come Jerusalem and Ahithophel with him
Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
16 and to be like/as as which to come (in): come Hushai [the] Archite friend David to(wards) Absalom and to say Hushai to(wards) Absalom to live [the] king to live [the] king
Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
17 and to say Absalom to(wards) Hushai this kindness your with neighbor your to/for what? not to go: went with neighbor your
Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
18 and to say Hushai to(wards) Absalom not for which to choose LORD and [the] people [the] this and all man Israel (to/for him *Q(K)*) to be and with him to dwell
Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
19 and [the] second to/for who? I to serve: minister not to/for face: before son: child his like/as as which to serve: minister to/for face: before father your so to be (to/for face of your *LAB(h)*)
Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
20 and to say Absalom to(wards) Ahithophel to give to/for you counsel what? to make: do
Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
21 and to say Ahithophel to(wards) Absalom to come (in): come to(wards) concubine father your which to rest to/for to keep: guard [the] house: home and to hear: hear all Israel for to stink with father your and to strengthen: strengthen hand all which with you
Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
22 and to stretch to/for Absalom [the] tent upon [the] roof and to come (in): come Absalom to(wards) concubine father his to/for eye: seeing all Israel
Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
23 and counsel Ahithophel which to advise in/on/with day [the] they(masc.) like/as as which (to ask man *Q(K)*) in/on/with word [the] God so all counsel Ahithophel also to/for David also to/for Absalom
Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.

< 2 Samuel 16 >