< 2 Kings 1 >

1 and to transgress Moab in/on/with Israel after death Ahab
Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
2 and to fall: fall Ahaziah about/through/for [the] latticework in/on/with upper room his which in/on/with Samaria and be weak: ill and to send: depart messenger and to say to(wards) them to go: went to seek in/on/with Baal-zebub Baal-zebub God Ekron if to live from sickness this
Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
3 and messenger: angel LORD to speak: speak to(wards) Elijah [the] Tishbite to arise: rise to ascend: rise to/for to encounter: meet messenger king Samaria and to speak: speak to(wards) them from without nothing God in/on/with Israel you(m. p.) to go: went to/for to seek in/on/with Baal-zebub Baal-zebub God Ekron
Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
4 and to/for so thus to say LORD [the] bed which to ascend: rise there not to go down from her for to die to die and to go: went Elijah
Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
5 and to return: return [the] messenger to(wards) him and to say to(wards) them what? this to return: return
Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
6 and to say to(wards) him man to ascend: rise to/for to encounter: meet us and to say to(wards) us to go: went to return: return to(wards) [the] king which to send: depart [obj] you and to speak: speak to(wards) him thus to say LORD from without nothing God in/on/with Israel you(m. s.) to send: depart to/for to seek in/on/with Baal-zebub Baal-zebub God Ekron to/for so [the] bed which to ascend: rise there not to go down from her for to die to die
Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
7 and to speak: speak to(wards) them what? justice [the] man which to ascend: rise to/for to encounter: meet you and to speak: speak to(wards) you [obj] [the] word: thing [the] these
Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
8 and to say to(wards) him man master: owning hair and girdle skin to gird in/on/with loin his and to say Elijah [the] Tishbite he/she/it
Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
9 and to send: depart to(wards) him ruler fifty and fifty his and to ascend: rise to(wards) him and behold to dwell upon head: top [the] mountain: mount and to speak: speak to(wards) him man [the] God [the] king to speak: speak to go down [emph?]
Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
10 and to answer Elijah and to speak: speak to(wards) ruler [the] fifty and if man God I to go down fire from [the] heaven and to eat [obj] you and [obj] fifty your and to go down fire from [the] heaven and to eat [obj] him and [obj] fifty his
Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
11 and to return: again and to send: depart to(wards) him ruler fifty another and fifty his and to answer and to speak: speak to(wards) him man [the] God thus to say [the] king haste to go down [emph?]
Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
12 and to answer Elijah and to speak: speak to(wards) them if man [the] God I to go down fire from [the] heaven and to eat [obj] you and [obj] fifty your and to go down fire God from [the] heaven and to eat [obj] him and [obj] fifty his
Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
13 and to return: again and to send: depart ruler fifty third and fifty his and to ascend: rise and to come (in): come ruler [the] fifty [the] third and to bow upon knee his to/for before Elijah and be gracious to(wards) him and to speak: speak to(wards) him man [the] God be precious please soul: life my and soul: life servant/slave your these fifty in/on/with eye: seeing your
Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
14 behold to go down fire from [the] heaven and to eat [obj] two ruler [the] fifty [the] first: previous and [obj] fifty their and now be precious soul: life my in/on/with eye: seeing your
Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
15 and to speak: speak messenger: angel LORD to(wards) Elijah to go down with him not to fear from face of his and to arise: rise and to go down with him to(wards) [the] king
Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
16 and to speak: speak to(wards) him thus to say LORD because which to send: depart messenger to/for to seek in/on/with Baal-zebub Baal-zebub God Ekron from without nothing God in/on/with Israel to/for to seek in/on/with word his to/for so [the] bed which to ascend: rise there not to go down from her for to die to die
Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
17 and to die like/as word LORD which to speak: speak Elijah and to reign Joram underneath: instead him in/on/with year two to/for Joram son: child Jehoshaphat king Judah for not to be to/for him son: child
Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
18 and remainder word: deed Ahaziah which to make: do not they(masc.) to write upon scroll: book Chronicles [the] day to/for king Israel
Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?

< 2 Kings 1 >