< 2 Kings 14 >
1 in/on/with year two to/for Joash son: child Joahaz king Israel to reign Amaziah son: child Joash king Judah
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 son: aged twenty and five year to be in/on/with to reign he and twenty and nine year to reign in/on/with Jerusalem and name mother his (Jehoaddan *Q(K)*) from Jerusalem
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 and to make: do [the] upright in/on/with eye: appearance LORD except not like/as David father his like/as all which to make: do Joash father his to make: do
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 except [the] high place not to turn aside: remove still [the] people to sacrifice and to offer: offer in/on/with high place
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 and to be like/as as which to strengthen: hold [the] kingdom in/on/with hand: power his and to smite [obj] servant/slave his [the] to smite [obj] [the] king father his
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 and [obj] son: child [the] to smite not to die like/as to write in/on/with scroll: book instruction Moses which to command LORD to/for to say not to die father upon son: child and son: child not to die upon father that if: except if: except man: anyone in/on/with sin his (to die *Q(K)*)
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 he/she/it to smite [obj] Edom in/on/with (Salt) Valley ((Valley of) Salt *Q(K)*) ten thousand and to capture [obj] [the] Sela in/on/with battle and to call: call by [obj] name her Joktheel till [the] day: today [the] this
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 then to send: depart Amaziah messenger to(wards) Jehoash son: child Jehoahaz son: child Jehu king Israel to/for to say to go: come! [emph?] to see: see face
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 and to send: depart Jehoash king Israel to(wards) Amaziah king Judah to/for to say [the] thistle which in/on/with Lebanon to send: depart to(wards) [the] cedar which in/on/with Lebanon to/for to say to give: give(marriage) [emph?] [obj] daughter your to/for son: child my to/for woman: wife and to pass living thing [the] land: wildlife which in/on/with Lebanon and to trample [obj] [the] thistle
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 to smite to smite [obj] Edom and to lift: enthuse you heart your to honor: honour and to dwell in/on/with house: home your and to/for what? to stir up in/on/with distress: harm and to fall: kill you(m. s.) and Judah with you
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 and not to hear: hear Amaziah and to ascend: rise Jehoash king Israel and to see: see face he/she/it and Amaziah king Judah in/on/with Beth-shemesh Beth-shemesh which to/for Judah
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 and to strike Judah to/for face: before Israel and to flee man: anyone (to/for tent: home his *Q(K)*)
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 and [obj] Amaziah king Judah son: child Jehoash son: child Ahaziah to capture Jehoash king Israel in/on/with Beth-shemesh Beth-shemesh (and to come (in): come *Q(K)*) Jerusalem and to break through in/on/with wall Jerusalem in/on/with gate Ephraim (Gate) till gate [the] Corner (Gate) four hundred cubit
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 and to take: take [obj] all [the] gold and [the] silver: money and [obj] all [the] article/utensil [the] to find house: temple LORD and in/on/with treasure house: home [the] king and [obj] son: type of [the] security and to return: return Samaria [to]
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 and remainder word: deed Jehoash which to make: do and might his and which to fight with Amaziah king Judah not they(masc.) to write upon scroll: book Chronicles [the] day to/for king Israel
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 and to lie down: be dead Jehoash with father his and to bury in/on/with Samaria with king Israel and to reign Jeroboam son: child his underneath: instead him
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 and to live Amaziah son: child Joash king Judah after death Jehoash son: child Jehoahaz king Israel five ten year
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 and remainder word: deed Amaziah not they(masc.) to write upon scroll: book Chronicles [the] day to/for king Judah
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 and to conspire upon him conspiracy in/on/with Jerusalem and to flee Lachish [to] and to send: depart after him Lachish [to] and to die him there
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 and to lift: bear [obj] him upon [the] horse and to bury in/on/with Jerusalem with father his in/on/with city David
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 and to take: take all people Judah [obj] Azariah and he/she/it son: aged six ten year and to reign [obj] him underneath: instead father his Amaziah
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 he/she/it to build [obj] Elath and to return: rescue her to/for Judah after to lie down: be dead [the] king with father his
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 in/on/with year five ten year to/for Amaziah son: child Joash king Judah to reign Jeroboam son: child Joash king Israel in/on/with Samaria forty and one year
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD not to turn aside: depart from all sin Jeroboam son: child Nebat which to sin [obj] Israel
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 he/she/it to return: rescue [obj] border: boundary Israel from Lebo Hamath till sea [the] (Sea of) the Arabah like/as word LORD God Israel which to speak: speak in/on/with hand: by servant/slave his Jonah son: child Amittai [the] prophet which from Gath-hepher [the] Gath-hepher
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 for to see: see LORD [obj] affliction Israel to rebel much and end to restrain and end to leave: release and nothing to help to/for Israel
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 and not to speak: speak LORD to/for to wipe [obj] name Israel from underneath: under [the] heaven and to save them in/on/with hand: power Jeroboam son: child Joash
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 and remainder word: deed Jeroboam and all which to make: do and might his which to fight and which to return: rescue [obj] Damascus and [obj] Hamath to/for Judah in/on/with Israel not they(masc.) to write upon scroll: book Chronicles [the] day to/for king Israel
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 and to lie down: be dead Jeroboam with father his with king Israel and to reign Zechariah son: child his underneath: instead him
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.