< 2 Chronicles 22 >

1 and to reign to dwell Jerusalem [obj] Ahaziah son: child his [the] small: young underneath: instead him for all [the] first: chief to kill [the] band [the] to come (in): come in/on/with Arabian to/for camp and to reign Ahaziah son: child Jehoram king Judah
Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 son: aged forty and two year Ahaziah in/on/with to reign he and year one to reign in/on/with Jerusalem and name mother his Athaliah daughter Omri
Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.
3 also he/she/it to go: walk in/on/with way: conduct house: household Ahab for mother his to be to advise him to/for be wicked
Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika.
4 and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD like/as house: household Ahab for they(masc.) to be to/for him to advise after death father his to/for destruction to/for him
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake.
5 also in/on/with counsel their to go: follow and to go: follow with Joram son: child Ahab king Israel to/for battle upon Hazael king Syria in/on/with Ramoth (Ramoth)-gilead and to smite [the] Syrian [obj] Joram
Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu,
6 and to return: return to/for to heal in/on/with Jezreel for [the] wound which to smite him in/on/with Ramah in/on/with to fight he with Hazael king Syria and Ahaziah son: child Jehoram king Judah to go down to/for to see: see [obj] Jehoram son: child Ahab in/on/with Jezreel for be weak: ill he/she/it
kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu. Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.
7 and from God to be ruin Ahaziah to/for to come (in): come to(wards) Joram and in/on/with to come (in): come he to come out: come with Joram to(wards) Jehu son: child Nimshi which to anoint him LORD to/for to cut: eliminate [obj] house: household Ahab
Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu.
8 and to be like/as to judge Jehu with house: household Ahab and to find [obj] ruler Judah and son: child brother: male-sibling Ahaziah to minister to/for Ahaziah and to kill them
Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha.
9 and to seek [obj] Ahaziah and to capture him and he/she/it to hide in/on/with Samaria and to come (in): bring him to(wards) Jehu and to die him and to bury him for to say son: descendant/people Jehoshaphat he/she/it which to seek [obj] LORD in/on/with all heart his and nothing to/for house: household Ahaziah to/for to restrain strength to/for kingdom
Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.
10 and Athaliah mother Ahaziah to see: see for to die son: child her and to arise: rise and to speak: subdue [obj] all seed: children [the] kingdom to/for house: household Judah
Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda.
11 and to take: take Jehoshabeath daughter [the] king [obj] Joash son: child Ahaziah and to steal [obj] him from midst son: child [the] king [the] to die and to give: put [obj] him and [obj] to suckle his in/on/with chamber [the] bed and to hide him Jehoshabeath daughter [the] king Jehoram woman: wife Jehoiada [the] priest for he/she/it to be sister Ahaziah from face: before Athaliah and not to die him
Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe.
12 and to be with them in/on/with house: temple [the] God to hide six year and Athaliah to reign upon [the] land: country/planet
Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.

< 2 Chronicles 22 >