< 2 Chronicles 21 >
1 and to lie down: be dead Jehoshaphat with father his and to bury with father his in/on/with city David and to reign Jehoram son: child his underneath: instead him
Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yehoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 and to/for him brother: male-sibling son: child Jehoshaphat Azariah and Jehiel and Zechariah and Azariah and Michael and Shephatiah all these son: child Jehoshaphat king Israel
Abale ake a Yehoramu, ana aamuna a Yehosafati, anali Azariya, Yehieli, Zekariya, Azariyahu, Mikayeli ndi Sefatiya. Onsewa anali ana a Yehosafati mfumu ya Israeli.
3 and to give: give to/for them father their gift many to/for silver: money and to/for gold and to/for precious thing with city fortress in/on/with Judah and [obj] [the] kingdom to give: give to/for Jehoram for he/she/it [the] firstborn
Abambo awo anawapatsa mphatso zambiri za siliva, golide ndi zinthu zina zamtengowapatali komanso mizinda yotetezedwa ya Yuda. Koma iye anapereka ufumu kwa Yehoramu chifukwa anali mwana wake woyamba kubadwa.
4 and to arise: rise Jehoram upon kingdom father his and to strengthen: strengthen and to kill [obj] all brother: male-sibling his in/on/with sword and also from ruler Israel
Yehoramu atakhazikika pa ufumu wa abambo ake, iye anapha abale ake ndi lupanga pamodzi ndi atsogoleri ena a Israeli.
5 son: aged thirty and two year Jehoram in/on/with to reign he and eight year to reign in/on/with Jerusalem
Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
6 and to go: walk in/on/with way: conduct king Israel like/as as which to make: do house: household Ahab for daughter Ahab to be to/for him woman: wife and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, pakuti anakwatira mwana wa Ahabu. Ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
7 and not be willing LORD to/for to ruin [obj] house: household David because [the] covenant which to cut: make(covenant) to/for David and like/as as which to say to/for to give: give to/for him lamp and to/for son: descendant/people his all [the] day: always
Komabe, chifukwa cha pangano limene Yehova anachita ndi Davide, Yehova sanafune kuwononga banja la Davide. Iye analonjeza kusungira nyale Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
8 in/on/with day his to transgress Edom from underneath: owning hand: owner Judah and to reign upon them king
Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
9 and to pass Jehoram with ruler his and all [the] chariot with him and to be to arise: rise night and to smite [obj] Edom [the] to turn: surround to(wards) him and [obj] ruler [the] chariot
Choncho Yehoramu anapita kumeneko pamodzi ndi atsogoleri ake ndi magaleta ake onse. Aedomu anamuzungulira pamodzi ndi atsogoleri ake koma iye ananyamuka ndi kuthawa usiku.
10 and to transgress Edom from underneath: owning hand: owner Judah till [the] day: today [the] this then to transgress Libnah in/on/with time [the] he/she/it from underneath: owning hand: owner his for to leave: forsake [obj] LORD God father his
Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira ulamuliro wa Yuda. Pa nthawi yomweyi, mzinda wa Libina unawukiranso chifukwa Yehoramu anasiya Yehova, Mulungu wa makolo ake.
11 also he/she/it to make high place in/on/with mountain: hill country Judah and to fornicate [obj] to dwell Jerusalem and to banish [obj] Judah
Iye anamanganso malo opembedzerapo mafano mʼmapiri a Yuda ndipo anachititsa anthu a mu Yerusalemu kukhala osakhulupirika. Choncho anasocheretsa anthu a ku Yuda.
12 and to come (in): come to(wards) him writing from Elijah [the] prophet to/for to say thus to say LORD God David father your underneath: because of which not to go: walk in/on/with way: conduct Jehoshaphat father your and in/on/with way: conduct Asa king Judah
Yehoramu analandira kalata yochokera kwa mneneri Eliya yonena kuti, “Yehova Mulungu wa Davide abambo ako akuti, ‘Iwe sunayende mʼnjira ya Yehosafati abambo ako kapena Asa mfumu ya Yuda.
13 and to go: walk in/on/with way: conduct king Israel and to fornicate [obj] Judah and [obj] to dwell Jerusalem like/as to fornicate house: household Ahab and also [obj] brother: male-sibling your house: household father your [the] pleasant from you to kill
Koma wayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo watsogolera anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kukhala osakhulupirika, monga linachitira banja la Ahabu. Waphanso abale ako, abale a banja la abambo ako, anthu amene anali abwino kuposa iweyo.
14 behold LORD to strike plague great: large in/on/with people your and in/on/with son: child your and in/on/with woman: wife your and in/on/with all property your
Kotero tsono Yehova ali pafupi kukantha anthu ako, ana ako, akazi ako ndi zinthu zako zonse, ndi chilango chachikulu.
15 and you(m. s.) in/on/with sickness many in/on/with sickness belly your till to come out: issue belly your from [the] sickness day upon day
Ndipo iwe udzadwala nthenda yoopsa yamʼmimba, mpaka nthendayo idzachititsa matumbo ako kutuluka.’”
16 and to rouse LORD upon Jehoram [obj] spirit: temper [the] Philistine and [the] Arabian which upon hand: to Ethiopian
Yehova anamuutsira Yehoramuyo mkwiyo wa Afilisti ndi Aarabu amene amakhala pafupi ndi Akusi.
17 and to ascend: rise in/on/with Judah and to break up/open her and to take captive [obj] all [the] property [the] to find to/for house: home [the] king and also son: child his and woman: wife his and not to remain to/for him son: child that if: except if: except Ahaziah small: young son: child his
Iwo anathira nkhondo Yuda. Analowanso ndi kutenga katundu yense amene anamupeza mʼnyumba ya mfumu pamodzi ndi ana ake ndi akazi ake. Palibe mwana amene anatsala kupatula mwana wake wamngʼono kwambiri, Ahaziya.
18 and after all this to strike him LORD in/on/with belly his to/for sickness to/for nothing healing
Izi zonse zitachitika, Yehova anakantha Yehoramu ndi nthenda yamʼmimba imene inali yosachiritsika.
19 and to be to/for day from day and like/as time to come out: extends [the] end to/for day: year two to come out: come belly his with sickness his and to die in/on/with disease bad: harmful and not to make to/for him people his fire like/as fire father his
Patapita nthawi, kumapeto kwa chaka chachiwiri, matumbo ake anatuluka chifukwa cha nthendayo, ndipo anafa imfa yopweteka kwambiri. Anthu ake sanasonkhe moto kumuchitira ulemu, monga anachitira ndi makolo ake.
20 son: aged thirty and two to be in/on/with to reign he and eight year to reign in/on/with Jerusalem and to go: went in/on/with not desire and to bury him in/on/with city David and not in/on/with grave [the] king
Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu. Iyeyo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu. Ndipo anamwalira popanda odandawula, nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati mʼmanda a mafumu.