< 2 Chronicles 13 >
1 in/on/with year eight ten to/for king Jeroboam and to reign Abijah upon Judah
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda,
2 three year to reign in/on/with Jerusalem and name mother his Micaiah daughter Uriel from Gibeah and battle to be between Abijah and between Jeroboam
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka zitatu. Dzina la amayi ake linali Maaka mwana wa Urieli wa ku Gibeya. Koma panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
3 and to bind Abijah [obj] [the] battle in/on/with strength: soldiers mighty man battle four hundred thousand man to choose and Jeroboam to arrange with him battle in/on/with eight hundred thousand man to choose mighty man strength
Abiya anapita ku nkhondo ndi asilikali odziwa bwino nkhondo 400,000, ndipo Yeroboamu anandandalitsa ankhondo, asilikali 800,000 odziwa bwino nkhondo, osankhidwa ndi amphamvu, woti amenyane naye.
4 and to arise: rise Abijah from upon to/for mountain: mount (Mount) Zemaraim which in/on/with mountain: hill country Ephraim and to say to hear: hear me Jeroboam and all Israel
Abiya anayima pa phiri la Zemaraimu, mʼdziko lamapiri la Efereimu, ndipo anati, “Yeroboamu ndi Aisraeli onse, tandimverani!
5 not to/for you to/for to know for LORD God Israel to give: give kingdom to/for David upon Israel to/for forever: enduring to/for him and to/for son: descendant/people his covenant salt
Kodi inu simukudziwa kuti Yehova, Mulungu wa Israeli, wapereka ufumu wa Israeli kwa Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya ndiponso pangano la mchere?
6 and to arise: rise Jeroboam son: child Nebat servant/slave Solomon son: child David and to rebel upon lord his
Komabe Yeroboamu mwana wa Nebati, mtumiki wa Solomoni mwana wa Davide, anawukira mbuye wake.
7 and to gather upon him human worthless son: type of Belial and to strengthen upon Rehoboam son: child Solomon and Rehoboam to be youth and tender heart and not to strengthen: prevail over to/for face of their
Ndipo anthu ena achabechabe anasonkhana kwa iye ndipo anatsutsana ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni pamene anali wamngʼono ndi wosalimba mtima ndi wopanda mphamvu kuti athe kulimbana nawo.
8 and now you(m. p.) to say to/for to strengthen: prevail over to/for face: before kingdom LORD in/on/with hand: power son: descendant/people David and you(m. p.) crowd many and with you calf gold which to make to/for you Jeroboam to/for God
“Ndipo tsopano inu mwakonzekera kutsutsana ndi ufumu wa Yehova, umene uli mʼmanja mwa zidzukulu za Davide. Inu ndithu mulipo ankhondo ambirimbiri ndipo muli ndi ana angʼombe agolide amene Yeroboamu anapanga kuti akhale milungu yanu.
9 not to banish [obj] priest LORD [obj] son: child Aaron and [the] Levi and to make to/for you priest like/as people [the] land: country/planet all [the] to come (in): come to/for to fill hand: donate his in/on/with bullock son: young animal cattle and ram seven and to be priest to/for not God
Koma kodi inu simunathamangitse ansembe a Yehova, ana a Aaroni ndiponso Alevi ndi kudzisankhira ansembe anuanu monga anthu ena amachitira? Aliyense amene amabwera kuti adzipatule atatenga mwana wangʼombe wamwamuna ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri amakhala wansembe wa zinthu zimene sizili milungu.
10 and we LORD God our and not to leave: forsake him and priest to minister to/for LORD son: child Aaron and [the] Levi in/on/with work
“Koma kunena za ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, ndipo sitinamusiye. Ansembe amene amatumikira Yehova ndi ana a Aaroni ndipo amathandizidwa ndi Alevi.
11 and to offer: offer to/for LORD burnt offering in/on/with morning in/on/with morning and in/on/with evening in/on/with evening and incense spice and row food: bread upon [the] table [the] pure and lampstand [the] gold and lamp her to/for to burn: burn in/on/with evening in/on/with evening for to keep: obey we [obj] charge LORD God our and you(m. p.) to leave: forsake [obj] him
Mmawa uliwonse ndi madzulo aliwonse amapereka nsembe zopsereza ndi kufukiza lubani kwa Yehova. Iwo amayika buledi pa tebulo loyeretsedwa monga mwa mwambo ndipo amayatsa nyale pa zoyikapo nyale zagolide madzulo aliwonse. Ife timachita zofuna za Yehova Mulungu wathu. Koma inu mwamusiya.
12 and behold with us in/on/with head: leader [the] God and priest his and trumpet [the] shout to/for to shout upon you son: child Israel not to fight with LORD God father your for not to prosper
Mulungu ali nafe pakuti ndiye mtsogoleri wathu. Ansembe ake atanyamula malipenga, adzayimba mfuwu wankhondo kulimbana nanu. Inu Aisraeli musalimbane ndi Yehova, Mulungu wa makolo anu, pakuti simungathe kupambana.”
13 and Jeroboam to turn: surround [obj] [the] ambush to/for to come (in): come from after them and to be to/for face: before Judah and [the] ambush from after them
Tsono Yeroboamu anali atatumiza asilikali kumbuyo mowazungulira, kotero kuti iye ali kutsogolo kwa anthu a ku Yuda, anthu owabisalira anali kumbuyo kwawo.
14 and to turn Judah and behold to/for them [the] battle face: before and back and to cry to/for LORD and [the] priest (to blow *Q(k)*) in/on/with trumpet
Asilikali a Yuda anatembenuka ndipo anaona kuti nkhondo imachitikira kutsogolo ndi kumbuyo. Ndipo iwo anafuwulira Yehova. Ansembe anayimba malipenga awo
15 and to shout man Judah and to be in/on/with to shout man Judah and [the] God to strike [obj] Jeroboam and all Israel to/for face: before Abijah and Judah
ndipo asilikali a Yuda anafuwula mawu ankhondo. Atafuwula mawu ankhondowo, Mulungu anagonjetsa Yeroboamu pamodzi ndi Aisraeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda.
16 and to flee son: descendant/people Israel from face: before Judah and to give: give them God in/on/with hand: power their
Aisraeli anathawa Ayuda. Ndipo Mulungu anawapereka mʼmanja mwawo.
17 and to smite in/on/with them Abijah and people his wound many and to fall: kill slain: killed from Israel five hundred thousand man to choose
Abiya pamodzi ndi anthu ake anapha anthu ambiri, kotero kuti Aisraeli 500,000 odziwa bwino nkhondo anaphedwa.
18 and be humble son: descendant/people Israel in/on/with time [the] he/she/it and to strengthen son: descendant/people Judah for to lean upon LORD God father their
Ankhondo a Israeli anagonjetsedwa pa nthawi imeneyi, ndipo ankhondo a Yuda anapambana chifukwa anadalira Yehova, Mulungu wa makolo awo.
19 and to pursue Abijah after Jeroboam and to capture from him city [obj] Bethel Bethel and [obj] daughter: village her and [obj] Jeshanah and [obj] daughter: village her and [obj] (Ephron *Q(K)*) and daughter: village her
Abiya anathamangitsa Yeroboamu ndipo anamulanda mizinda ya Beteli, Yesana, ndi Efroni pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
20 and not to restrain strength Jeroboam still in/on/with day Abijah and to strike him LORD and to die
Yeroboamu sanapezenso mphamvu nthawi ya Abiya. Ndipo Yehova anamukantha nafa.
21 and to strengthen: strengthen Abijah and to lift: marry to/for him woman: wife four ten and to beget twenty and two son: child and six ten daughter
Koma Abiya mphamvu zake zinakula. Iye anakwatira akazi 14 ndipo anali ndi ana aamuna 22 ndi ana aakazi 16.
22 and remainder word: deed Abijah and way: conduct his and word his to write in/on/with story [the] prophet Iddo
Zina ndi zina zokhudza Abiya, zimene anachita ndi zimene anayankhula, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mneneri Ido.