< 1 Samuel 8 >

1 and to be like/as as which be old Samuel and to set: make [obj] son: child his to judge to/for Israel
Samueli atakalamba anasankha ana ake kuti akhale oweruza Aisraeli.
2 and to be name son: child his [the] firstborn Joel and name second his Abijah to judge in/on/with Beersheba Beersheba
Mwana wake woyamba anali Yoweli, wachiwiri anali Abiya, ndipo ankaweruza ku Beeriseba.
3 and not to go: walk son: child his (in/on/with way: conduct his *Q(K)*) and to stretch after [the] unjust-gain and to take: take bribe and to stretch justice
Koma ana akewo sanatengere makhalidwe ake abwino. Iwo ankapotokera ku zoyipa namatsata phindu mwachinyengo. Ankalandira ziphuphu ndi kumaweruza mwachinyengo.
4 and to gather all old: elder Israel and to come (in): come to(wards) Samuel [the] Ramah [to]
Tsono akuluakulu onse a Israeli anasonkhana pamodzi ndipo anabwera kwa Samueli ku Rama.
5 and to say to(wards) him behold you(m. s.) be old and son: child your not to go: walk in/on/with way: conduct your now to set: appoint [emph?] to/for us king to/for to judge us like/as all [the] nation
Iwo anati kwa iye “Taonani, inu mwakula tsopano ndipo ana anu sakutsata makhalidwe anu abwino. Tsono mutipatse mfumu kuti izitilamulira, monga momwe ikuchitira mitundu ina yonseyi.”
6 and be evil [the] word: thing in/on/with eye: appearance Samuel like/as as which to say to give: give [emph?] to/for us king to/for to judge us and to pray Samuel to(wards) LORD
Koma mawu oti, “Mutipatse mfumu kuti izitilamulira,” sanakondweretse Samueli. Choncho anapemphera kwa Yehova.
7 and to say LORD to(wards) Samuel to hear: obey in/on/with voice [the] people to/for all which to say to(wards) you for not [obj] you to reject for [obj] me to reject from to reign upon them
Yehova anamuyankha nati, “Mvera zonse zimene anthuwa akukuwuza. Si ndiwe amene akumukana, koma akukana Ine kuti ndikhale mfumu yawo.
8 like/as all [the] deed which to make: do from day: today to ascend: establish I [obj] them from Egypt and till [the] day: today [the] this and to leave: forsake me and to serve God another so they(masc.) to make: do also to/for you
Kuyambira tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mpaka lero zochita zawo zakhala zondikana Ine nʼkumatumikira milungu ina. Tsopano akukukananso iwe.
9 and now to hear: obey in/on/with voice their surely for to testify to testify in/on/with them and to tell to/for them justice: custom [the] king which to reign upon them
Tsono amvere zimene akunena, koma uwachenjeze kwambiri ndipo uwawuzitse za khalidwe la mfumu imene idzawalamulire.”
10 and to say Samuel [obj] all word LORD to(wards) [the] people [the] to ask from with him king
Samueli anawawuza anthu amene amamupempha mfumu aja mawu onse a Yehova.
11 and to say this to be justice: custom [the] king which to reign upon you [obj] son: child your to take: take and to set: appoint to/for him in/on/with chariot his and in/on/with horse his and to run: run to/for face: before chariot his
Iye anati, “Zimene mfumu imene idzakulamulireniyo idzachite ndi izi: Izidzatenga ana anu aamuna kuti akhale ankhondo ake; ena pa magaleta ake, ena pa akavalo ake ndipo ena othamanga patsogolo pa magaleta akewo.
12 and to/for to set: appoint to/for him ruler thousand and ruler fifty and to/for to plow/plot plowing his and to/for to reap harvest his and to/for to make article/utensil battle his and article/utensil chariot his
Ena adzawayika kukhala olamulira asilikali 1,000, ena olamulira asilikali makumi asanu, ndi ena otipula minda yake, ndi kukolola ndiponso ena adzakhala osula zida zankhondo ndi zida za magaleta ake.
13 and [obj] daughter your to take: take to/for perfumer and to/for cook and to/for to bake
Iyo idzatenga ana anu akazi kuti akhale oyenga mafuta onunkhira, ophika chakudya ndi kupanga buledi.
14 and [obj] land: country your and [obj] vineyard your and olive your [the] pleasant to take: take and to give: give to/for servant/slave his
Idzatenga minda yanu yabwino ya mpesa ndi ya mitengo ya olivi ndipo adzayipereka kwa antchito ake.
15 and seed your and vineyard your to tithe and to give: give to/for eunuch his and to/for servant/slave his
Idzatenga gawo lakhumi la tirigu wanu ndi mphesa zanu ndi kupereka kwa nduna zake ndi akapitawo ake.
16 and [obj] servant/slave your and [obj] maidservant your and [obj] youth your [the] pleasant and [obj] donkey your to take: take and to make: do to/for work his
Mfumuyo idzatenga antchito anu aamuna ndi aakazi. Idzatenganso ngʼombe zanu zabwino ndi abulu anu nʼkumazingwiritsa ntchito.
17 flock your to tithe and you(m. p.) to be to/for him to/for servant/slave
Iyo idzatenga gawo lakhumi la zoweta zanu, ndipo inu eni mudzakhala akapolo ake.
18 and to cry out in/on/with day [the] he/she/it from to/for face: because king your which to choose to/for you and not to answer LORD [obj] you in/on/with day [the] he/she/it
Nthawi imeneyo ikadzafika inu mudzalira momvetsa chisoni chifukwa cha mfumu imene mwadzisankhira, koma Yehova sadzakuyankhani.”
19 and to refuse [the] people to/for to hear: obey in/on/with voice Samuel and to say not that if: except if: except king to be upon us
Koma anthu anakana kumumvera Samueli. Iwo anati, “Ayi! Ife tikufuna mfumu yotilamulira.
20 and to be also we like/as all [the] nation and to judge us king our and to come out: come to/for face: before our and to fight [obj] battle our
Kotero ifenso tidzakhala ngati mayiko ena. Mfumu yathu idzatiweruza ndiponso idzatuluka nafe kutitsogolera kukamenya nkhondo.”
21 and to hear: hear Samuel [obj] all word [the] people and to speak: speak them in/on/with ear: to ears LORD
Samueli atamva zonse zimene anthuwo ananena, iye anakazifotokozanso kwa Yehova.
22 and to say LORD to(wards) Samuel to hear: obey in/on/with voice their and to reign to/for them king and to say Samuel to(wards) human Israel to go: went man: anyone to/for city his
Yehova anamuyankha nati, “Amvere zimene akunena ndipo apatse mfumu.” Ndipo Samueli anati kwa Aisraeli aja, “Bwererani aliyense kwawo.”

< 1 Samuel 8 >