< 1 Kings 3 >

1 and be related Solomon with Pharaoh king Egypt and to take: marry [obj] daughter Pharaoh and to come (in): bring her to(wards) city David till to end: finish he to/for to build [obj] house: home his and [obj] house: temple LORD and [obj] wall Jerusalem around
Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
2 except [the] people to sacrifice in/on/with high place for not to build house: home to/for name LORD till [the] day [the] they(masc.)
Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
3 and to love: lover Solomon [obj] LORD to/for to go: walk in/on/with statute David father his except in/on/with high place he/she/it to sacrifice and to offer: offer
Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
4 and to go: went [the] king Gibeon [to] to/for to sacrifice there for he/she/it [the] high place [the] great: large thousand burnt offering to ascend: offer up Solomon upon [the] altar [the] he/she/it
Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
5 in/on/with Gibeon to see: see LORD to(wards) Solomon in/on/with dream [the] night and to say God to ask what? to give: give to/for you
Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
6 and to say Solomon you(m. s.) to make: do with servant/slave your David father my kindness great: large like/as as which to go: walk to/for face: before your in/on/with truth: faithful and in/on/with righteousness and in/on/with uprightness heart with you and to keep: obey to/for him [obj] [the] kindness [the] great: large [the] this and to give: give to/for him son: child to dwell upon throne his like/as day: today [the] this
Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
7 and now LORD God my you(m. s.) to reign [obj] servant/slave your underneath: instead David father my and I youth small not to know to come out: come and to come (in): come
“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
8 and servant/slave your in/on/with midst people your which to choose people many which not to count and not to recount from abundance
Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
9 and to give: give to/for servant/slave your heart to hear: understand to/for to judge [obj] people your to/for to understand between good to/for bad: evil for who? be able to/for to judge [obj] people your [the] heavy [the] this
Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
10 and be good [the] word: thing in/on/with eye: appearance Lord for to ask Solomon [obj] [the] word: thing [the] this
Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
11 and to say God to(wards) him because which to ask [obj] [the] word: thing [the] this and not to ask to/for you day many and not to ask to/for you riches and not to ask soul: life enemy your and to ask to/for you to understand to/for to hear: judge justice
Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
12 behold to make: do like/as word your behold to give: give to/for you heart wise and to understand which like you not to be to/for face: before your and after you not to arise: rise like you
Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
13 and also which not to ask to give: give to/for you also riches also glory which not to be like you man: anyone in/on/with king all day your
Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
14 and if to go: walk in/on/with way: conduct my to/for to keep: obey statute: decree my and commandment my like/as as which to go: walk David father your and to prolong [obj] day your
Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
15 and to awake Solomon and behold dream and to come (in): come Jerusalem and to stand: stand to/for face: before ark covenant Lord and to ascend: offer up burnt offering and to make: offer peace offering and to make feast to/for all servant/slave his
Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
16 then to come (in): come two woman to fornicate to(wards) [the] king and to stand: stand to/for face: before his
Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
17 and to say [the] woman [the] one please lord my I and [the] woman [the] this to dwell in/on/with house: home one and to beget with her in/on/with house: home
Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
18 and to be in/on/with day [the] third to/for to beget me and to beget also [the] woman [the] this and we together nothing be a stranger with us in/on/with house: home exception two we in/on/with house: home
Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
19 and to die son: child [the] woman [the] this night which to lie down: lay down upon him
“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
20 and to arise: rise in/on/with midst [the] night and to take: take [obj] son: child my from beside me and maidservant your sleeping and to lie down: lay down him in/on/with bosom: embrace her and [obj] son: child her [the] to die to lie down: lay down in/on/with bosom: embrace my
Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
21 and to arise: rise in/on/with morning to/for to suckle [obj] son: child my and behold to die and to understand to(wards) him in/on/with morning and behold not to be son: child my which to beget
Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
22 and to say [the] woman [the] another not for son: child my [the] alive and son: child your [the] to die and this to say not for son: child your [the] to die and son: child my [the] alive and to speak: speak to/for face: before [the] king
Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
23 and to say [the] king this to say this son: child my [the] alive and son: child your [the] to die and this to say not for son: child your [the] to die and son: child my [the] alive
Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
24 and to say [the] king to take: bring to/for me sword and to come (in): bring [the] sword to/for face: before [the] king
Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
25 and to say [the] king to cut [obj] [the] youth [the] alive to/for two and to give: give [obj] [the] half to/for one and [obj] [the] half to/for one
Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
26 and to say [the] woman which son: child her [the] alive to(wards) [the] king for to grow warm compassion her upon son: child her and to say please lord my to give: give to/for her [obj] [the] to beget [the] alive and to die not to die him and this to say also to/for me also to/for you not to be to cut
Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
27 and to answer [the] king and to say to give: give to/for her [obj] [the] to beget [the] alive and to die not to die him he/she/it mother his
Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
28 and to hear: hear all Israel [obj] [the] justice: judgement which to judge [the] king and to fear: revere from face of [the] king for to see: examine for wisdom God in/on/with entrails: among his to/for to make: do justice
Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.

< 1 Kings 3 >