< 1 Kings 22 >

1 and to dwell three year nothing battle between Syria and between Israel
Kwa zaka zitatu panalibe nkhondo pakati pa Aramu ndi Israeli.
2 and to be in/on/with year [the] third and to go down Jehoshaphat king Judah to(wards) king Israel
Koma pa chaka chachitatu, Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita kukacheza ndi mfumu ya ku Israeli.
3 and to say king Israel to(wards) servant/slave his to know for to/for us Ramoth (Ramoth)-gilead and we be silent from to take: take [obj] her from hand: power king Syria
Mfumu ya ku Israeli nʼkuti itawuza atumiki ake kuti, “Kodi inu simukudziwa kuti Ramoti Giliyadi ndi dera lathu ndipo ife palibe chimene tikuchita kuti tilitenge deralo mʼmanja mwa mfumu ya Aramu?”
4 and to say to(wards) Jehoshaphat to go: went with me to/for battle Ramoth Gilead and to say Jehoshaphat to(wards) king Israel like me like you like/as people my like/as people your like/as horse my like/as horse your
Tsono iye anafunsa Yehosafati kuti, “Kodi udzapita nane ku nkhondo ku Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha mfumu ya ku Israeli kuti, “Ine ndili monga inu, anthu anga monga anthu anu, akavalo anga monga akavalo anu.”
5 and to say Jehoshaphat to(wards) king Israel to seek please like/as day: today [obj] word LORD
Koma Yehosafati anawuzanso mfumu ya ku Israeli kuti, “Poyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
6 and to gather king Israel [obj] [the] prophet like/as four hundred man and to say to(wards) them to go: went upon Ramoth (Ramoth)-gilead to/for battle if to cease and to say to ascend: rise and to give: give Lord in/on/with hand: power [the] king
Choncho mfumu ya Israeli inasonkhanitsa pamodzi aneneri okwanira 400, ndipo inawafunsa kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena ndileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Ambuye waupereka mzindawo mʼmanja mwa mfumu.”
7 and to say Jehoshaphat nothing here prophet to/for LORD still and to seek from [obj] him
Koma Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi kuno kulibenso mneneri wina wa Yehova kumene ife tingakafunsireko nzeru?”
8 and to say king Israel to(wards) Jehoshaphat still man one to/for to seek [obj] LORD from [obj] him and I to hate him for not to prophesy upon me pleasant that if: except if: except bad: evil Micaiah son: child Imlah and to say Jehoshaphat not to say [the] king so
Mfumu ya ku Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife tingakafunsire kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa iyeyo samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa nthawi zonse. Dzina lake ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu musatero.”
9 and to call: call to king Israel to(wards) eunuch one and to say to hasten [emph?] Micaiah son: child Imlah
Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa atumiki ake ndipo inati, “Kayitane Mikaya mwana wa Imula msangamsanga.”
10 and king Israel and Jehoshaphat king Judah to dwell man: anyone upon throne his to clothe garment in/on/with threshing floor entrance gate Samaria and all [the] prophet to prophesy to/for face: before their
Atavala mikanjo yawo yaufumu, mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopondera tirigu pafupi ndi chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
11 and to make to/for him Zedekiah son: child Chenaanah horn iron and to say thus to say LORD in/on/with these to gore [obj] Syria till to end: destroy them
Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana nʼkuti atapanga nyanga zachitsulo ndipo iye ananenera kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi, inu mudzagunda nazo Aaramu mpaka iwo atawonongeka.’”
12 and all [the] prophet to prophesy so to/for to say to ascend: rise Ramoth (Ramoth)-gilead and to prosper and to give: give LORD in/on/with hand: power [the] king
Aneneri ena onse ananenera zomwezonso. Iwo anati, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
13 and [the] messenger which to go: went to/for to call: call to Micaiah to speak: speak to(wards) him to/for to say behold please word [the] prophet lip: according one pleasant to(wards) [the] king to be please (word your *Q(K)*) like/as word one from them and to speak: speak pleasant
Wamthenga amene anapita kukayitana Mikaya anamuwuza kuti, “Taonani, aneneri onse monga munthu mmodzi akunenera za kupambana kwa mfumu. Mawu anunso akhale ogwirizana ndi mawu awo, ndipo mukayankhule zabwino.”
14 and to say Micaiah alive LORD for [obj] which to say LORD to(wards) me [obj] him to speak: speak
Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndikawawuza zokhazo zimene Yehova akandiwuze.”
15 and to come (in): come to(wards) [the] king and to say [the] king to(wards) him Micaiah to go: went to(wards) Ramoth (Ramoth)-gilead to/for battle if to cease and to say to(wards) him to ascend: rise and to prosper and to give: give LORD in/on/with hand: power [the] king
Atafika, Ahabu anamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Pitani ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
16 and to say to(wards) him [the] king till like/as what? beat I to swear you which not to speak: speak to(wards) me except truth: true in/on/with name LORD
Ahabu anati kwa iye, “Kodi ndikulumbiritse kangati kuti undiwuze zoona zokhazokha mʼdzina la Yehova?”
17 and to say to see: see [obj] all Israel to scatter to(wards) [the] mountain: mount like/as flock which nothing to/for them to pasture and to say LORD not lord to/for these to return: return man: anyone to/for house: home his in/on/with peace
Pamenepo Mikaya anayankha kuti, “Ndinaona Aisraeli onse atamwazikana pa mapiri ngati nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mwamtendere.’”
18 and to say king Israel to(wards) Jehoshaphat not to say to(wards) you not to prophesy upon me pleasant that if: except if: except bad: evil
Mfumu ya ku Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti ameneyu samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa zokhazokha?”
19 and to say to/for so to hear: hear word LORD to see: see [obj] LORD to dwell upon throne his and all army [the] heaven to stand: stand upon him from right his and from left his
Mikaya anapitiriza kuyankhula nati, “Tsono imvani mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu, gulu lonse la kumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi ku dzanja lake lamanzere.
20 and to say LORD who? to entice [obj] Ahab and to ascend: rise and to fall: kill in/on/with Ramoth Gilead and to say this in/on/with thus and this to say in/on/with thus
Ndipo Yehova anati, ‘Kodi ndani amene akamukope Ahabu kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi, nʼkukafera komweko?’” “Wina anapereka maganizo ena ndipo winanso maganizo ena.
21 and to come out: come [the] spirit and to stand: stand to/for face: before LORD and to say I to entice him
Potsirizira, mzimu wina unabwera ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, ‘Ine ndidzamukopa.’”
22 and to say LORD to(wards) him in/on/with what? and to say to come out: come and to be spirit deception in/on/with lip all prophet his and to say to entice and also be able to come out: come and to make: do so
Yehova anafunsa kuti, “Ukamukopa bwanji?” Mzimuwo unati, “Ndidzapita ndi kukakhala mzimu wabodza pakamwa pa aneneri ake onse.” Yehova anati, “‘Iwe udzamukopadi. Pita kachite zomwezo.’
23 and now behold to give: put LORD spirit deception in/on/with lip all prophet your these and LORD to speak: promise upon you distress: harm
“Ndipo tsopano taonani, Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anu onsewa. Yehova waneneratu kuti mukaona mavuto.”
24 and to approach: approach Zedekiah son: child Chenaanah and to smite [obj] Micaiah upon [the] jaw and to say where? this to pass spirit LORD from with me to/for to speak: speak with you
Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi namenya Mikaya patsaya. Iye anafunsa Mikaya kuti, “Kodi mzimu wa Yehova unadzera njira iti pamene umatuluka mwa ine kuti uziyankhula ndi iwe?”
25 and to say Micaiah look! you to see: see in/on/with day [the] he/she/it which to come (in): come chamber in/on/with chamber to/for to hide
Mikaya anayankha kuti, “Udzaona pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
26 and to say king Israel to take: take [obj] Micaiah and to return: return him to(wards) Amon ruler [the] city and to(wards) Joash son: child [the] king
Pamenepo mfumu ya ku Israeli inalamula kuti, “Mugwireni Mikaya ndipo mubwerere naye kwa Amoni mkulu wa mzinda, ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu
27 and to say thus to say [the] king to set: put [obj] this house: home [the] prison and to eat him food: bread oppression and water oppression till to come (in): come I in/on/with peace
ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyikeni mʼndende munthu uyu ndipo musamupatse chakudya china koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwerera mwamtendere.’”
28 and to say Micaiah if to return: return to return: return in/on/with peace not to speak: speak LORD in/on/with me and to say to hear: hear people all their
Mikaya ananena kuti, “Ngati mudzabwerera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo iye anapitiriza kunena kuti, “Gwiritsitsani mawu angawa, anthu inu nonse!”
29 and to ascend: rise king Israel and Jehoshaphat king Judah Ramoth (Ramoth)-gilead
Choncho mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
30 and to say king Israel to(wards) Jehoshaphat to search and to come (in): come in/on/with battle and you(m. s.) to clothe garment your and to search king Israel and to come (in): come in/on/with battle
Mfumu ya ku Israeli inawuza Yehosafati kuti, “Ine ndidzalowa mu nkhondoyi modzibisa, koma inu muvale zovala zanu zaufumu.” Choncho mfumu ya ku Israeli inadzibisa ndi kupita ku nkhondo.
31 and king Syria to command [obj] ruler [the] chariot which to/for him thirty and two to/for to say not to fight with small and with great: large that if: except if: except with king Israel to/for alone him
Tsono mfumu ya ku Aramu nʼkuti italamulira anthu ake 32 olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu, koma mfumu ya ku Israeli.”
32 and to be like/as to see: see ruler [the] chariot [obj] Jehoshaphat and they(masc.) to say surely king Israel he/she/it and to turn aside: turn aside upon him to/for to fight and to cry out Jehoshaphat
Olamulira magaleta ataona Yehosafati, ankaganiza kuti, “Ndithu iyi ndiye mfumu ya ku Israeli.” Choncho anabwerera kukamenyana naye, koma Yehosafati atafuwula,
33 and to be like/as to see: see ruler [the] chariot for not king Israel he/she/it and to return: return from after him
olamulira akavalo anaona kuti sanali mfumu ya ku Israeli ndipo analeka kumuthamangitsa.
34 and man: anyone to draw in/on/with bow to/for integrity his and to smite [obj] king Israel between [the] joint and between [the] armor and to say to/for charioteer his to overturn hand: themselves your and to come out: send me from [the] camp for be weak: ill
Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndi kulasa mfumu ya ku Israeli polumikizira malaya ake odzitetezera. Mfumu inawuza woyendetsa galeta lake kuti, “Tembenuka ndipo undichotse pa nkhondo pano pakuti ndalasidwa.”
35 and to ascend: rise [the] battle in/on/with day [the] he/she/it and [the] king to be to stand: stand in/on/with chariot before Syria and to die in/on/with evening and to pour: pour blood [the] wound to(wards) bosom: lap [the] chariot
Nkhondo inakula kwambiri tsiku limenelo, ndipo mfumu inakhala tsonga mʼgaleta lake moyangʼanana ndi Aaramu. Magazi ake ankayenderera pansi kuchokera mʼgaleta, ndipo pa nthawi ya madzulo inamwalira.
36 and to pass [the] cry in/on/with camp like/as to come (in): (sun)set [the] sun to/for to say man: anyone to(wards) city his and man: anyone to(wards) land: country/planet his
Pamene dzuwa linkalowa, kunamveka mfuwu wa nkhondo kuti, “Munthu aliyense apite ku mzinda wa kwawo, aliyense apite ku dziko la kwawo!”
37 and to die [the] king and to come (in): come Samaria and to bury [obj] [the] king in/on/with Samaria
Ndipo mfumu ija inafa, nabwera nayo ku Samariya, ndipo anayika mʼmanda kumeneko.
38 and to overflow [obj] [the] chariot upon pool Samaria and to lick [the] dog [obj] blood his and [the] to fornicate to wash: wash like/as word LORD which to speak: speak
Anatsuka galeta lija pa dziwe la ku Samariya (pamene ankasamba akazi achiwerewere) ndipo agalu ananyambita magazi a mfumuyo, monga momwe Yehova ananenera.
39 and remainder word: deed Ahab and all which to make: do and house: home [the] tooth: ivory which to build and all [the] city which to build not they(masc.) to write upon scroll: book Chronicles [the] day to/for king Israel
Tsono ntchito zina za Ahabu, kuphatikiza zonse anazichita, nyumba yaufumu imene anamanga yokutidwa ndi minyanga ya njovu, mizinda yotetezedwa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
40 and to lie down: be dead Ahab with father his and to reign Ahaziah son: child his underneath: instead him
Ahabu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
41 and Jehoshaphat son: child Asa to reign upon Judah in/on/with year four to/for Ahab king Israel
Yehosafati, mwana wa Asa anakhala mfumu ya ku Yuda chaka chachinayi cha Ahabu mfumu ya ku Israeli.
42 Jehoshaphat son: aged thirty and five year in/on/with to reign he and twenty and five year to reign in/on/with Jerusalem and name mother his Azubah daughter Shilhi
Yehosafati anali wa zaka 35 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 25. Amayi ake anali Azuba mwana wa Silihi.
43 and to go: walk in/on/with all way: conduct Asa father his not to turn aside: turn aside from him to/for to make: do [the] upright in/on/with eye: seeing LORD surely [the] high place not to turn aside: remove still [the] people to sacrifice and to offer: offer in/on/with high place
Pa zinthu zonse, Yehosafati anayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanachite zotsutsana ndi machitidwe a abambo ake. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova. Komabe, malo azipembedzo sanawawononge, ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
44 and to ally Jehoshaphat with king Israel
Yehosafati anakhala mwamtendere ndi mfumu ya ku Israeli.
45 and remainder word: deed Jehoshaphat and might his which to make: do and which to fight not they(masc.) to write upon scroll: book word: deed [the] day to/for king Judah
Ntchito zake zina za Yehosafati, zinthu zimene anachita ndi zamphamvu zimene anaonetsa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Yuda?
46 and remainder [the] male cult prostitute which to remain in/on/with day Asa father his to burn: burn from [the] land: country/planet
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zachiwerewere mwa chipembedzo amene anatsalira pa nthawi ya ulamuliro wa Asa, abambo ake.
47 and king nothing in/on/with Edom to stand king
Nthawi imeneyo kunalibe mfumu ku Edomu, amene ankalamulira anali munthu woyikidwa ndi mfumu ya ku Yuda.
48 Jehoshaphat (to make: do *Q(K)*) fleet Tarshish to/for to go: went Ophir [to] to/for gold and not to go: went for (to break *Q(K)*) fleet in/on/with Ezion-geber Ezion-geber
Yehosafati anapanga sitima zapamadzi zopita ku Ofiri kukatenga golide, koma sitimazo sizinayende chifukwa zinawonongeka ku Ezioni Geberi.
49 then to say Ahaziah son: child Ahab to(wards) Jehoshaphat to go: went servant/slave my with servant/slave your in/on/with fleet and not be willing Jehoshaphat
Nthawi imeneyo Ahaziya mwana wa Ahabu anawuza Yehosafati kuti, “Anthu anga ayende pa madzi pamodzi ndi anthu anu,” koma Yehosafati anakana.
50 and to lie down: be dead Jehoshaphat with father his and to bury with father his in/on/with city David father his and to reign Jehoram son: child his underneath: instead him
Ndipo Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
51 Ahaziah son: child Ahab to reign upon Israel in/on/with Samaria in/on/with year seven ten to/for Jehoshaphat king Judah and to reign upon Israel year
Ahaziya mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya ku Israeli ku Samariya mʼchaka cha 17 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
52 and to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD and to go: walk in/on/with way: conduct father his and in/on/with way: conduct mother his and in/on/with way: conduct Jeroboam son: child Nebat which to sin [obj] Israel
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, chifukwa anayenda mʼnjira za abambo ndi amayi ake komanso mʼnjira za Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli.
53 and to serve: minister [obj] [the] Baal and to bow to/for him and to provoke [obj] LORD God Israel like/as all which to make: do father his
Potumikira ndi kupembedza Baala, iye anakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli, monga momwe anachitira abambo ake.

< 1 Kings 22 >