< Zechariah 2 >
1 And I lifted up eyes my and I saw and there! a man and [was] in hand his a cord of measurement.
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
2 And I said where? [are] you going and he said to me to measure Jerusalem to see how much? [is] breadth its and how much? [is] length its.
Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
3 And there! the angel who was speaking with me [was] going out and an angel another [was] going out to meet him.
Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
4 And he said (to him *Q(k)*) run speak to the young man this saying open regions it will remain Jerusalem from [the] multitude of person[s] and livestock in [the] midst of it.
ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
5 And I I will be to it [the] utterance of Yahweh a wall of fire all around and glory I will become in [the] middle of it.
Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
6 Alas! alas! flee from [the] land of [the] north [the] utterance of Yahweh that like [the] four [the] winds of the heavens I have scattered you [the] utterance of Yahweh.
“Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
7 Alas! O Zion escape O inhabitant[s] of [the] daughter of Babylon.
“Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
8 For thus he says Yahweh of hosts after honor he has sent me to the nations who plundered you for the [one who] touches you [is] touching [the] pupil of eye his.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
9 For here I [am] about to brandish hand my on them and they will be plunder for own slaves their and you will know that Yahweh of hosts he has sent me.
Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
10 Shout for joy and rejoice O daughter of Zion for here I [am] about to come and I will dwell in midst of you [the] utterance of Yahweh.
“Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
11 And they will join themselves nations many to Yahweh in the day that and they will become for me a people and I will dwell in midst of you and you will know that Yahweh of hosts he has sent me to you.
“Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
12 And he will inherit Yahweh Judah portion his on [the] land of holiness and he will choose again Jerusalem.
Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
13 Hush! O all flesh from before Yahweh for he has roused himself from [the] dwelling place of holiness his.
Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”