< Zechariah 10 >
1 Ask from Yahweh rain at [the] time of spring rain Yahweh [is] making thunder-clouds and rain of rain he gives to them to everyone vegetation in the field.
Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira; ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula. Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu, ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
2 For the teraphim they speak wickedness and the diviners they see falsehood and [the] dreams of worthlessness they speak futility they comfort! there-fore they have set out like sheep they are afflicted for there not [is] a shepherd.
Mafano amayankhula zachinyengo, owombeza mawula amaona masomphenya abodza; amafotokoza maloto onama, amapereka chitonthozo chopandapake. Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika chifukwa chosowa mʼbusa.
3 Towards the shepherds it has burned anger my and on the leaders I will visit [judgment] for he visits Yahweh of hosts flock his [the] house of Judah and he will make them like [the] horse of majesty his in battle.
“Ine ndawakwiyira kwambiri abusa, ndipo ndidzalanga atsogoleri; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira nkhosa zake, nyumba ya Yuda, ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
4 From it a corner from it a peg from it a bow of war from it he will come forth every ruler together.
Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya, mudzachokera chikhomo cha tenti, mudzachokera uta wankhondo, mudzachokera mtsogoleri aliyense.
5 And they will be like warriors treading down in [the] mud of [the] streets in battle and they will fight for Yahweh [will be] with them and they will put to shame riders of horses.
Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo. Chifukwa Yehova adzakhala nawo, adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.
6 And I will make strong - [the] house of Judah and [the] house of Joseph I will save and I will restore them for I have compassion on them and they will be just as not I had rejected them for I [am] Yahweh God their and I will answer them.
“Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe. Ndidzawabwezeretsa chifukwa ndawamvera chisoni. Adzakhala ngati kuti sindinawakane, chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo ndipo ndidzawayankha.
7 And they will be like a warrior Ephraim and it will be glad heart their like wine and children their they will see and they will be glad it may rejoice heart their in Yahweh.
Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo. Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala; mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
8 I will whistle for them and I will gather them for I have redeemed them and they will multiply as they multiplied.
Ndidzaliza mluzu ndi kuwasonkhanitsa pamodzi. Ndithu ndawawombola; adzachulukana ngati poyamba paja.
9 And I will sow them among the peoples and in the distant places they will remember me and they will live with children their and they will return.
Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu, koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira. Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka, ndipo adzabwerera.
10 And I will bring back them from [the] land of Egypt and from Assyria I will gather them and to [the] land of Gilead and Lebanon I will bring them and not it will be found for them.
Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya. Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni, mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
11 And he will pass in the sea trouble and he will strike in the sea waves and they will dry up all [the] depths of [the] River and it will be brought down [the] pride of Assyria and [the] scepter of Egypt it will depart.
Adzawoloka nyanja ya masautso; nyanja yokokoma idzagonja ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa. Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
12 And I will make strong them by Yahweh and in name his they will go about [the] utterance of Yahweh.
Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova ndipo adzayenda mʼdzina lake,” akutero Yehova.