< Ruth 3 >

1 And she said to her Naomi mother-in-law her O daughter my ¿ not will I seek for you a resting place that it will go well for you.
Tsiku lina Naomi anafunsa mpongozi wake Rute kuti, “Mwana wanga, kodi si kwabwino kuti ndikupezere kokhala kuti zinthu zizikuyendera bwino?
2 And therefore ¿ not [is] Boaz relative our whom you were with female servants his there! he [will be] winnowing [the] threshing floor of the barley this night.
Bowazi amene adzakazi ake wakhala nawo nthawi yonseyi, si wachibale wathu kodi? Usiku uno akhala akupeta barele ku malo opunthira.
3 And you will wash - and you will anoint yourself and you will put (garments your *Q(K)*) on yourself (and you will go down *Q(K)*) the threshing floor may not you make yourself known to the man until finishes he to eat and to drink.
Samba ndi kudzola mafuta onunkhira, ndipo uvale zovala zako zabwino kwambiri. Kenaka upite ku malo opunthirako tirigu ndi barele koma munthuyo asakakuzindikire kufikira atamaliza kudya ndi kumwa.
4 And let it be when lies down he and you will take note of the place where he will lie down there and you will go and you will uncover feet his (and you will lie down *Q(k)*) and he he will tell to you [that] which (you will do! *L(abh)*)
Akamakagona, iwe ukaonetsetse malo amene wagonawo. Kenaka upite ndi kuvundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona. Iyeyo akakuwuza zoti uchite.”
5 And she said to her all that (you are saying to me *Q(K)*) I will do.
Rute anayankha kuti, “Ndichita zonse zimene mwanena.”
6 And she went down the threshing floor and she did according to all that she had commanded her mother-in-law her.
Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.
7 And he ate Boaz and he drank and it was good heart his and he went to lie down at [the] end of the heap and she came in secrecy and she uncovered feet his and she lay down.
Atamaliza kudya ndi kumwa, Bowazi anakhala wosangalala, ndipo anakagona pa mbali pa mulu wa barele. Tsono Rute anapita mwa kachetechete, navundukula chofunda ku mapazi ake ndi kugona.
8 And it was in [the] middle of the night and he trembled the man and he twisted and there! a woman [was] lying down feet his.
Tsono pakati pa usiku Bowazi anadzidzimuka, natembenuka, ndipo anangoona mkazi akugona ku mapazi ake.
9 And he said who? [are] you and she said I [am] Ruth maidservant your and you will spread out skirt your over maidservant your for [are] a kinsman-redeemer you.
Iye anafunsa kuti, “Ndiwe yani?” Ndipo anayankha kuti, “Ndine mdzakazi wanu Rute. Popeza ndinu wachibale amene muyenera kundiwombola, ndiye mundilowe chokolo.”
10 And he said [be] blessed you by Yahweh O daughter my you have made good loyalty your latter more than former to not to go after the young men whether poor and or rich.
Ndipo Bowazi anati, “Mwana wanga, Yehova akudalitse popeza kukoma mtima kumene wasonyeza panoku kwaposa koyamba kaja. Iwe sunathamangire anyamata olemera kapena osauka.
11 And therefore O daughter my may not you fear all that you are saying I will do for you for [is] knowing all [the] gate of people my that [are] a woman of ability you.
Ndipo tsopano mwana wanga usaope. Ine ndidzakuchitira chilichonse udzapemphe popeza anzanga onse amʼmudzi muno akudziwa kuti ndiwe mkazi wa khalidwe labwino.
12 And therefore for truly that (*Q(K)*) [am] a kinsman-redeemer I and also there [is] a kinsman-redeemer near more than I.
Ngakhale kuti ndinedi wachibale woyenera kukusamala, koma alipo wachibale weniweni kuposa ine.
13 Stay - this night and it will be in the morning if he will redeem you good let him redeem and if not he will be willing to redeem you and I will redeem you I [by] [the] life of Yahweh lie down until the morning.
Gona konkuno usiku uno mpaka mmawa. Tsono ngati iyeyu adzakulowa chokolo, chabwino alowe. Koma ngati safuna kutero, ine ndikulumbira pamaso pa Yehova Wamoyo kuti ndidzakulowa chokolo. Ugone kuno mpaka mmawa.”
14 And she lay down (feet his *Q(K)*) until the morning and she arose (before *Q(K)*) he recognized anyone neighbor his and he said may not it be known that she came the woman the threshing floor.
Choncho Rute anagona ku mapazi ake mpaka mmawa, koma anadzuka mmamawa kusanayere chifukwa Bowazi anati, “Aliyense asadziwe kuti kopondera barele kunabwera mkazi.”
15 And he said give the shawl which [is] on you and take hold on it and she took hold on it and he measured out six barley and he put [it] on her and he came the city.
Bowazi anati kwa Rute, “Bwera nacho kuno chofunda wavalacho ndipo uchiyale pansi.” Ndipo atayala, Bowazi anathira makilogalamu makumi awiri a barele ndi kumusenzetsa Rute. Rute anapita nakalowa mu mzinda.
16 And she came to mother-in-law her and she said who? [are] you O daughter my and she told to her all that he had done for her the man.
Rute atafika kwa apongozi ake anamufunsa kuti, “Zinayenda bwanji mwana wanga?” Kenaka iye anafotokoza zonse zimene Bowazi anamuchitira.
17 And she said [the] six the barley these he gave to me for (he said to me *Q(K)*) may not you go empty to mother-in-law your.
Ndipo anati, “Munthuyo anandipatsa makilogalamu makumi awiri awa a barele, nandiwuza kuti usapite kwa apongozi ako wopanda kanthu.”
18 And she said sit down O daughter my until that you will know! how? will it fall out a matter for not he will be at peace the man that except he has finished the matter this day.
Kenaka Naomi anati, “Mwana wanga, dikira mpaka titaona mmene zinthu zikhalire chifukwa munthuyu salekera pomwepo, mpaka zinthuzi zitakonzeka lero.”

< Ruth 3 >