< Psalms 99 >
1 Yahweh he reigns let them tremble peoples [he is] sitting cherubim let it quake the earth.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 Yahweh in Zion [is] great and [is] exalted he over all the peoples.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Let them give thanks to name your great and to be feared [is] holy he.
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 And [the] strength of a king justice he loves you you have established uprightness justice and righteousness in Jacob - you you have done.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Exalt Yahweh God our and bow down to [the] footstool of feet his [is] holy he.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Moses and Aaron - [were] among priests his and Samuel [was] among [those who] call on name his [they were] calling out to Yahweh and he he answered them.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 In a pillar of cloud he spoke to them they kept testimonies his and a decree he gave to them.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 O Yahweh God our you you answered them a God forgiving you were them and avenging yourself on deeds their.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Exalt Yahweh God our and bow down to [the] mountain of holiness his for [is] holy Yahweh God our.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.