< Psalms 66 >
1 To the choirmaster a song a psalm shout for joy to God O all the earth.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 Sing praises [the] glory of name his make glory praise his.
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 Say to God how! awesome [are] deeds your in [the] greatness of strength your they cringe to you enemies your.
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 All the earth - they bow down to you so they may sing praises to you they sing praises to name your (Selah)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Come and see [the] works of God [who is] awesome of deed on [the] children of humankind.
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 He turned [the] sea - into dry land in the river they passed on foot there let us rejoice in him.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 [he is] ruling By might his - forever eyes his on the nations they keep watch the rebellious [people] - may not (they be exalted *Q(K)*) themselves (Selah)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 Bless O peoples - God our and make heard [the] sound of praise his.
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 [who] placed Self our in life and not he has permitted to slip foot our.
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 For you have tested us O God you have refined us as refine silver.
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 You have brought us in the net you have put affliction on hips our.
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 You have made ride a man to head our we have gone in fire and in water and you have brought out us to superfluity.
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 I will come house your with burnt offerings I will pay to you vows my.
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 Which they opened lips my and it spoke mouth my when it was distress to me.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 Burnt offerings of fatlings I will offer up to you with [the] smoke of rams I will offer cattle with goats (Selah)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 Come listen so let me recount O all [those] fearing God [that] which he has done for self my.
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 To him mouth my I called out and exaltation [was] under tongue my.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 Wickedness if I had considered in heart my not he will listen - [the] Lord.
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 Nevertheless he has heard God he has paid attention to [the] sound of prayer my.
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 [be] blessed God who not he has turned aside prayer my and covenant loyalty his from with me.
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!