< Psalms 57 >

1 To the choirmaster al-tashcheth of David a miktam when fled he from before Saul in the cave. Show favor to me O God - show favor to me for in you it takes refuge self my and in [the] shadow of wings your I take refuge until it will pass by destruction.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
2 I call out to God Most High to God [who] avenges on me.
Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 He will send from heaven - and he will save me he will reproach [one who] crushes me (Selah) he will send God covenant loyalty his and faithfulness his.
Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Self my - in among lions I lie with [those that] devour [the] children of humankind teeth their [are] a spear and arrows and tongue their [is] a sword sharp.
Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Be exalted! above the heavens O God [be] over all the earth glory your.
Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 A net - they prepared for feet my it bent down self my they dug before me a pit they have fallen in [the] midst of it (Selah)
Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
7 [is] steadfast Heart my O God [is] steadfast heart my I will sing and I will sing praises.
Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 Awake! O honor my awake! O lyre and harp I will waken [the] dawn.
Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 I will give thanks to you among the peoples - O Lord I will sing praises to you not nations.
Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 For [is] great to [the] heavens covenant loyalty your and to [the] clouds faithfulness your.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Be exalted! above [the] heavens O God [be] over all the earth glory your.
Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

< Psalms 57 >