< Psalms 37 >

1 Of David - may not you fret yourself in the evil-doers may not you be jealous of [those who] do unrighteousness.
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 For like grass quickly they will wither and like [the] greenery of vegetation they will fade!
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Trust in Yahweh and do good dwell [the] land and graze faithfulness.
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 And take delight on Yahweh so he may give to you [the] requests of heart your.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Roll on Yahweh way your and rely on him and he he will act.
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 And he will bring forth like the light righteousness your and justice your like the noontide.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Be still - to Yahweh and wait longingly for him may not you fret yourself in [one who] makes prosperous way his in a person [who] makes plots.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Refrain from anger and forsake rage may not you fret yourself only to do evil.
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 For evil-doers they will be cut off! and [those who] wait for Yahweh they they will possess [the] land.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 And yet a little and there not [will be the] wicked and you will look carefully on place his and there not [will be] he.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 And humble [people] they will possess [the] land and they will take delight on abundance of well-being.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 [is] plotting [the] wicked To the righteous and [is] gnashing towards him teeth his.
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 [the] Lord He laughs to him for he sees that it will come day his.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 A sword - they have drawn wicked [people] and they have bent bow their to make fall [the] poor and [the] needy to slaughter [people] upright of way.
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Sword their it will go in own heart their and bows their they will be broken.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 [is] good [the] little Of the righteous more than [the] wealth of wicked [people] many.
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 For [the] arms of wicked [people] they will be broken and [is] sustaining righteous [people] Yahweh.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 [is] knowing Yahweh [the] days of blameless [people] and inheritance their for ever it will be.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 Not they will be ashamed in a time evil and in days of famine they will be satisfied.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 For wicked [people] - they will perish and [the] enemies of Yahweh [will be] like a splendid [thing] of pastures they will come to an end in smoke they will come to an end.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 [is] borrowing [the] wicked And not he repays and [the] righteous [is] showing favor and giving.
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 For blessed [ones] his they will possess [the] land and cursed [ones] his they will be cut off.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 From Yahweh [the] steps of a man they are established and way his he delights in.
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 For he will fall not he will be thrown down for Yahweh [is] supporting hand his.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 A young man - I have been also I am old and not I have seen [the] righteous forsaken and offspring his seeking food.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 All the day [he is] showing favor and [he is] lending and offspring his [become] a blessing.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Turn away from evil and do good and dwell for ever.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 For Yahweh - [is] loving justice and not he will abandon faithful [people] his for ever they are preserved and [the] offspring of wicked [people] it is cut off.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 Righteous [people] they will possess [the] land so they may dwell for ever on it.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 [the] mouth of [the] righteous It utters wisdom and tongue his it speaks justice.
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 [the] law of God his [is] in heart his not it slips steps his.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 [is] watching A wicked [person] for righteous [person] and [is] seeking to kill him.
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 Yahweh not he will abandon him in hand his and not he will condemn as guilty him when is judged he.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Wait to Yahweh - and keep way his and he will exalt you to possess [the] land when are cut off wicked [people] you will see.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 I have seen a wicked [person] ruthless and spreading himself like a native tree luxuriant.
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 And he passed away and there! there not [was] he and I sought him and not he was found.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Watch [the] blameless and see [the] upright for a future [belongs] to a person of peace.
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 And transgressors they will be destroyed altogether [the] future of wicked [people] it will be cut off.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 And [the] salvation of righteous [people] [is] from Yahweh place of refuge their in a time of trouble.
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 And he helped them Yahweh and he delivered them he delivers them from wicked [people] and he saves them for they have taken refuge in him.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Psalms 37 >