< Psalms 33 >
1 Shout for joy O righteous [people] in Yahweh for upright [people] [is] fitting praise.
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 Give thanks to Yahweh with harp with lyre of ten make music to him.
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 Sing to him a song new do well to play with a shout of joy.
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 For [is] upright [the] word of Yahweh and all work his [is] in faithfulness.
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 [he is] loving Righteousness and justice [the] covenant loyalty of Yahweh it is full the earth.
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 By [the] word of Yahweh [the] heavens they were made and by [the] breath of mouth his all host their.
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 [he is] gathering Like heap [the] waters of the sea [he is] putting in storehouses [the] deeps.
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 Let them fear from Yahweh all the earth from him let them be afraid all [the] inhabitants of [the] world.
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
9 For he he spoke and it was he he commanded and it stood forth.
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 Yahweh he makes ineffectual [the] counsel of nations he frustrates [the] plans of peoples.
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 [the] counsel of Yahweh for ever it stands [the] plans of heart his to a generation and a generation.
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 How blessed! [is] the nation which Yahweh [is] God its the people - [which] he has chosen to an inheritance for himself.
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 From [the] heavens he looks Yahweh he sees all [the] children of humankind.
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
14 From [the] place of dwelling his he looks to all [the] inhabitants of the earth.
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 The [one who] forms together heart their the [one who] attends to all deeds their.
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
16 Not king [is] saved by greatness of army a warrior not he is delivered by greatness of strength.
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 [is] a vain hope Horse for victory and by [the] greatness of strength its not it delivers.
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Here! [the] eye of Yahweh [is] to [those] fearing him to [those who] hope for covenant loyalty his.
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 To deliver from death life their and to preserve alive them in famine.
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Self our it waits for Yahweh [is] help our and shield our he.
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 For in him it rejoices heart our for in [the] name of holiness his we trust.
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 May it be covenant loyalty your O Yahweh toward us just as we hope for you.
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.