< Psalms 2 >
1 Why? do they plot nations and peoples do they devise? vanity.
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 They take their stand - [the] kings of [the] earth and rulers they seat themselves together on Yahweh and on anointed his.
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Let us tear off fetters their and let us throw away from us ropes their.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 [the one who] sits In the heavens he laughs [the] Lord he mocks them.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Then he speaks to them in anger his and in fury his he terrifies them.
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 And I I have installed king my on Zion [the] mountain of holiness my.
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 I will recount concerning [the] decree of Yahweh he said to me [are] son my you I this day I have begotten you.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Ask from me so let me make nations inheritance your and possession your [the] ends of [the] earth.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 You will break them with a rod of iron like a vessel of a potter you will smash them.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 And therefore O kings act prudently let yourselves be instructed O rulers of [the] earth.
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Serve Yahweh with fear and rejoice with trembling.
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Kiss [the] son lest he should be angry - and you may perish way if it burns like a little anger his how blessed! [are] all [those who] seek refuge in him.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.