< Psalms 143 >
1 A psalm of David O Yahweh - hear prayer my give ear! to supplications my in faithfulness your answer me in righteousness your.
Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
2 And may not you go in judgment with servant your for not he is righteous before you any living [person].
Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
3 For he has pursued an enemy - self my he has crushed to the ground life my he has caused to dwell me in dark places like dead [people] of antiquity.
Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
4 And it has fainted away on me spirit my in [the] midst of me it is appalled heart my.
Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
5 I have remembered days - from antiquity I have meditated on every deed your on [the] work of hands your I meditate.
Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
6 I have spread out hands my to you throat my - like a land exhausted [is] to you (Selah)
Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
7 Hurry answer me - O Yahweh it is exhausted spirit my may not you hide face your from me and I will be equal with [those who] go down of [the] pit.
Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
8 Make hear me in the morning - covenant loyalty your for in you I have trusted make known to me [the] way which I will go for to you I lift up desire my.
Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
9 Deliver me from enemies my - O Yahweh to you I have covered.
Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
10 Teach me - to do will your for you [are] God my spirit your good may it lead me in a land of level ground.
Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
11 For [the] sake of name your O Yahweh you will preserve alive me in righteousness your - you will bring out from trouble life my.
Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
12 And in covenant loyalty your you will destroy enemies my and you will destroy all [the] opposers of life my for I [am] servant your.
Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.