< Psalms 120 >

1 [the] song of The ascents to Yahweh in distress of me I called out and he answered me.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 O Yahweh deliver! self my from a lip of falsehood from a tongue deceit.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 What? will anyone give to you and what? will anyone add to you O tongue deceit.
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Arrows of a warrior sharpened with burning coals of broom plants.
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 Woe! to me that I have sojourned Meshech I have dwelt with [the] tents of Kedar.
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 Much it has dwelt itself self my with [one who] hates peace.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 I [am] peace and that I speak they [are] for war.
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

< Psalms 120 >