< Psalms 119 >

1 How blessed! [are people] blameless of way those [who] walk in [the] law of Yahweh.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 How blessed! [are those who] observe testimonies his with all [the] heart they seek him.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Also not they do injustice in ways his they walk.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 You you have commanded precepts your to keep exceedingly.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 Would that! they will be steadfast ways my to keep decrees your.
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Then not I will be ashamed when look I to all commandments your.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 I will give thanks to you in uprightness of heart when learn I [the] judgments of righteousness your.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Decrees your I will keep may not you forsake me up to muchness.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 How? will he keep pure a youth path his by keeping [it] according to word your.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 With all heart my I seek you may not you allow to stray me from commandments your.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 In heart my I have hidden word your so that not I will sin to you.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 [be] blessed You O Yahweh teach me decrees your.
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 With lips my I recount all [the] judgments of mouth your.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 In [the] way of testimonies your I exult as on all wealth.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 On precepts your I will meditate and I will pay attention to paths your.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 In statutes your I will delight myself not I will forget word your.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Deal bountifully towards servant your I will live and I will keep word your.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Uncover eyes my so let me pay attention to wonderful [things] from law your.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 [am] a sojourner I on the earth may not you hide from me commandments your.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 It is crushed self my for longing to judgments your at every time.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 You rebuke arrogant [people] cursed [people] who go astray from commandments your.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Roll away from on me reproach and contempt for testimonies your I observe.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Also they sit officials in me they speak together servant your he meditates on decrees your.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Also testimonies your [are] delight my [the] people of counsel my.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 It clings to the dust self my preserve alive me according to word your.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Ways my I recounted and you answered me teach me decrees your.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 [the] way of Precepts your give understanding of me so let me meditate on wonders your.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 It weeps self my from grief strengthen me according to word your.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 A way of falsehood remove from me and law your show favor to me.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 A way of faithfulness I have chosen judgments your I have placed.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 I have clung to testimonies your O Yahweh may not you put to shame me.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 [the] way of Commandments your I run for you enlarge heart my.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Teach me O Yahweh [the] way of decrees your so I may observe it end.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Give understanding me so let me observe law your so I may keep it with all [the] heart.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Lead me in [the] path of commandments your for in it I delight.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Incline heart my to testimonies your and may not [it incline] to unjust gain.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Take away eyes my from looking at worthlessness in ways your preserve alive me.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Fulfill to servant your word your which [is] for fear your.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Take away reproach my which I dread for judgments your [are] good.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Here! I long for precepts your in righteousness your preserve alive me.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 And may they come to me covenant loyalti your O Yahweh salvation your according to word your.
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 So I may answer [the] [one who] taunts me a word for I trust in word your.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 And may not you take away from mouth my a word of faithfulness up to muchness for for judgments your I hope.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 And I will keep law your continually for ever and ever.
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 And I will walk about in the broad place for precepts your I have sought.
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 And I will speak in testimonies your before kings and not I will be ashamed.
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 And I may delight myself in commandments your which I love.
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 And I may lift up hands my to commandments your which I love and I will meditate on decrees your.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Remember [the] word to servant your on that you have made hope me.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 This [is] comfort my in affliction my that word your it has preserved alive me.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Arrogant [people] they have mocked me up to muchness from law your not I have turned aside.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 I remember judgments your from long ago - O Yahweh and I have comforted myself.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Burning indignation it has seized me from wicked [people] [who] forsake law your.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Songs they have been of me decrees your in [the] house of sojournings my.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 I have remembered in the night name your O Yahweh and I have kept! law your.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 This it has belonged to me that precepts your I have observed.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 [is] portion My Yahweh I have said to keep words your.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 I have entreated face your with all [the] heart show favor to me according to word your.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 I have thought about ways my and I have turned back! feet my to testimonies your.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 I have made haste and not I have delayed to keep commandments your.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 [the] ropes of Wicked [people] they have surrounded me law your not I have forgotten.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 [the] middle of [the] night I arise to give thanks to you on [the] judgments of righteousness your.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 [am] a companion I of all [those] who they fear you and of [those who] keep precepts your.
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Covenant loyalty your O Yahweh it is full the earth decrees your teach me.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Good you have done with servant your O Yahweh according to word your.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Goodness of discernment and knowledge teach me for in commandments your I trust.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Before I was afflicted I [was] going astray and now word your I keep.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 [are] good You and [are] doing good teach me decrees your.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 They have smeared on me falsehood arrogant [people] I with all [the] heart - I observe precepts your.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 It is insensitive like fat heart their I law your I delight.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 It was good for me that I was afflicted so that I may learn decrees your.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 [is] good For me [the] law of mouth your more than thousands of gold and silver.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Hands your they made me and they prepared me give understanding me so let me learn commandments your.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 [those] fearing You may they see me and they may rejoice for for word your I have hoped.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 I know O Yahweh that [are] righteousness judgments your and faithfulness you have afflicted me.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Let it be please covenant loyalty your to comfort me according to word your to servant your.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Let them come to me compassion your so I may live for law your [is] delight my.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Let them be ashamed arrogant [people] for falsehood they have subverted me I I will meditate on precepts your.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Let them turn to me [those] fearing you (and [those who] know *Q(K)*) testimonies your.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 May it be heart my blameless in decrees your so that not I will be ashamed.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 It is exhausted for salvation your being my for word your I hope.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 They are exhausted eyes my for word your saying when? will you comfort me.
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 For I have become like a skin-bottle in smoke decrees your not I have forgotten.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 How many? [are] [the] days of servant your when? will you do in [those who] harass me judgment.
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 They have dug for me arrogant [people] pits which not [are] according to law your.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 All commandments your [are] faithfulness falsehood they have harassed me help me.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 Like a little they have made an end of me on the earth and I not I have forsaken precepts your.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 According to covenant loyalty your preserve alive me so let me keep [the] testimony of mouth your.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 For ever O Yahweh word your [is] standing firm in the heavens.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 [is] to A generation and a generation faithfulness your you have established [the] earth and it endures.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 For judgments your they stand forth this day for everything [are] servants your.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 If not law your [had been] delight my then I perished in affliction my.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 For ever not I will forget precepts your for by them you have preserved alive me.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 [belong] to You I save me for precepts your I have sought.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 For me they have waited wicked [people] to destroy me testimonies your I will consider carefully.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 To all perfection I have seen an end [is] broad commandment your exceedingly.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 How! I love law your all the day it [is] meditation my.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 More than enemies my it makes wise me commandments your for for ever it [belongs] to me.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 More than all teachers my I have insight for testimonies your [are] a meditation of me.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 More than old [people] I gain understanding for precepts your I have observed.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 From every path evil I have restrained feet my so that I may keep word your.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 From judgments your not I have turned aside for you you have taught me.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 How! they are smooth to palate my word your more than honey to mouth my.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 From precepts your I gain understanding there-fore I hate - every path of falsehood.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 [is] a lamp For foot my word your and a light for pathway my.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 I have sworn an oath and I have confirmed! to keep [the] judgments of righteousness your.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 I have been afflicted up to muchness O Yahweh preserve alive me according to word your.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 [the] freewill offerings of Mouth my accept please O Yahweh and judgments your teach me.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Life my [is] in hand my continually and law your not I forget.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 They have set wicked [people] a snare for me and from precepts your not I have gone astray.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 I have inherited testimonies your for ever for [are] [the] joy of heart my they.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 I have turned heart my to do decrees your for ever end.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Half-hearted people I hate and law your I love.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 [are] hiding place My and shield my you for word your I hope.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Turn aside from me O evil-doers and let me observe [the] commandments of God my.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Sustain me according to word your so I may live and may not you put to shame me from hope my.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Uphold me so let me be saved and I may have regard for decrees your continually.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 You reject all [those who] go astray from decrees your for [is] falsehood deceitfulness their.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Dross you cause to cease all [the] wicked [people] of [the] earth therefore I love testimonies your.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 It trembles from dread of you flesh my and from judgments your I am afraid.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 I have done justice and righteousness not you will abandon me to oppressors my.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Stand surety for servant your for good may not they oppress me arrogant [people].
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Eyes my they are exhausted for deliverance your and for [the] word of righteousness your.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Do with servant your according to covenant loyalty your and decrees your teach me.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 [am] servant Your I give understanding me so let me know testimonies your.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 A time to act [belongs] to Yahweh people have broken law your.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 There-fore I love commandments your more than gold and more than pure gold.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 There-fore - all [the] precepts of everything I approve every path of falsehood I hate.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 [are] wonders Testimonies your there-fore it observes them self my.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 [the] opening of Words your it gives light [it is] giving understanding to simple people.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Mouth my I opened wide and I panted! for for commandments your I longed.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Turn to me and show favor to me according to custom to [those who] love name your.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Footsteps my direct by word your and may not it have power over me any wickedness.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Redeem me from oppression of humankind so let me keep precepts your.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Face your make shine on servant your and teach me decrees your.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Streams of water they have gone down eyes my because not people keep law your.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 [are] righteous You O Yahweh and [are] upright judgments your.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 You commanded righteousness testimonies your and faithfulness much.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 It has destroyed me zeal my for they have forgotten words your opponents my.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 [has been] refined Word your exceedingly and servant your he loves it.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 [am] insignificant I and [am] despised precepts your not I have forgotten.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Righteousness your [is] righteousness for ever and law your [is] truth.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Distress and anguish they have found me commandments your [are] delight my.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 [are] righteousness Testimonies your for ever give understanding me so I may live.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 I call out with all [the] heart answer me O Yahweh decrees your I will observe.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 I call out to you save me so let me keep testimonies your.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 I am early in the twilight and I cried for help! (for word your *Q(K)*) I hope.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 They anticipate eyes my [the] night-watches to meditate on word your.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Voice my hear! according to covenant loyalty your O Yahweh according to judgments your preserve alive me.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 They draw near [those who] pursue wickedness from law your they are distant.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 [are] near You O Yahweh and all commandments your [are] truth.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Antiquity I have known from testimonies your that for ever you have established them.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 See affliction my and rescue me for law your not I have forgotten.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Conduct! case my and redeem me to word your preserve alive me.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 [is] far From wicked [people] salvation for decrees your not they have sought.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Compassion your [are] great - O Yahweh according to judgments your preserve alive me.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 [are] many [those who] harass Me and foes my from testimonies your not I have turned aside.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 I see [those who] act treacherously and I felt disgust! that word your not they have kept.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 See that precepts your I love O Yahweh according to covenant loyalty your preserve alive me.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 [the] head of Word your [is] truth and [is] for ever every judgment of righteousness of your.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Icials they have harassed me without cause (and from word your *Q(K)*) it is in dread heart my.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 [am] rejoicing I on word your like [one who] brings out plunder much.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Falsehood I hate and I abhor law your I love.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Seven [times] in the day I praise you on [the] judgments of righteousness your.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Peace great [belongs] to [those who] love law your and not [belongs] to them a stumbling block.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 I wait for salvation your O Yahweh and commandments your I do.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 It keeps self my testimonies your and I have loved them exceedingly.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 I keep precepts your and testimonies your for all ways my [are] before you.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 May it draw near cry of entreaty my before you O Yahweh according to word your give understanding me.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 May it come supplication my before you according to word your deliver me.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 May they pour forth lips my praise for you teach me decrees your.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 May it sing tongue my word your for all commandments your [are] righteousness.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 May it be hand your [about] to help me for precepts your I have chosen.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 I long for salvation your O Yahweh and law your [is] delight my.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 May it live self my so it may praise you and judgments your may they help me.
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 I have gone astray like a sheep lost seek servant your for commandments your not I have forgotten.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalms 119 >