< Psalms 105 >

1 Give thanks to Yahweh call on name his make known among the peoples deeds his.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
2 Sing to him sing praises to him tell in all wonders his.
Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
3 Boast in [the] name of holiness his let it rejoice [the] heart of - [those who] seek Yahweh.
Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
4 Seek Yahweh and strength his seek face his continually.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
5 Remember wonders his which he did signs his and [the] judgments of mouth his.
Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
6 O offspring of Abraham servant his O children of Jacob chosen ones his.
inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
7 He [is] Yahweh God our [are] in all the earth judgments his.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
8 He remembers for ever covenant his [the] word [which] he commanded for a thousand generation[s].
Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
9 Which he made with Abraham and oath his to Isaac.
pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
10 And he confirmed it to Jacob to a decree to Israel a covenant of perpetuity.
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
11 Saying to you I will give [the] land of Canaan [the] portion of inheritance your.
“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
12 When were they men of number like a little and sojourners in it.
Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
13 And they went about from nation to nation from a kingdom to a people another.
ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
14 Not he permitted anyone to oppress them and he rebuked on them kings.
Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
15 May not you touch anointed [ones] my and to prophets my may not you do harm.
“Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
16 And he called a famine on the land every staff of bread he broke.
Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
17 He sent before them a man to a slave he was sold Joseph.
Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
18 People afflicted with shackle[s] (foot his *Q(K)*) iron it came neck his.
Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
19 Until [the] time came word his [the] word of Yahweh it tested him.
mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
20 He sent a king (and he set free him *LA(bh)*) a ruler of peoples and he set free him.
Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
21 He appointed him master of household his and ruler over every possession his.
Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
22 To bind officials his in will his and elders his he taught wisdom.
kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
23 And he came Israel Egypt and Jacob he sojourned in [the] land of Ham.
Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
24 And he made fruitful people his exceedingly and he made strong it more than foes its.
Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
25 He turned heart their to hate people his to deal deceptively with servants his.
amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
26 He sent Moses servant his Aaron whom he had chosen him.
Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
27 They performed among them [the] words of signs his and wonders in [the] land of Ham.
Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
28 He sent darkness and he made dark and not they rebelled against (word his. *Q(K)*)
Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
29 He turned water their into blood and he caused to die fish their.
Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
30 It swarmed land their frogs in [the] rooms of kings their.
Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
31 He spoke and it came a swarm of flies gnats in all territory their.
Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
32 He made rains their hail a fire of flames [was] in land their.
Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
33 And he struck down vine[s] their and fig tree[s] their and he broke down [the] tree[s] of territory their.
Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
34 He spoke and it came locust[s] and locust[s] and there not [was] a number.
Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
35 And it ate all [the] vegetation in land their and it ate [the] fruit of ground their.
zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
36 And he struck down every firstborn in land their [the] beginning of all manly vigor their.
Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
37 And he brought out them with silver and gold and there not among tribes his [was one who] stumbled.
Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
38 It was glad Egypt when went out they for it had fallen dread of them on them.
Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
39 He spread out a cloud to a covering and fire to give light night.
Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
40 He asked and he brought quail and bread of heavens he satisfied them.
Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
41 He opened a rock and they flowed out waters they went in the dry regions a river.
Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
42 For he remembered [the] word of holiness his Abraham servant his.
Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
43 And he brought out people his with joy with a shout of joy chosen ones his.
Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
44 And he gave to them lands of nations and [the] labor of peoples they took possession of.
Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
45 In order that - they may keep decrees his and laws his they may observe praise Yahweh.
kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalms 105 >