< Numbers 1 >

1 And he spoke Yahweh to Moses in [the] wilderness of Sinai in [the] tent of meeting on [day] one of the month second in the year second of going out their from [the] land of Egypt saying.
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
2 Lift up [the] head of all [the] congregation of [the] people of Israel to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names of every male to heads their.
“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
3 From a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare in Israel you will enroll them to military groups their you and Aaron.
Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
4 And with you they will be a man a man to the tribe a man [is the] head of [the] house of ancestors his he.
Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
5 And these [are] [the] names of the men who they will stand with you for Reuben Elizur [the] son of Shedeur.
Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
6 For Simeon Shelumiel [the] son of Zurishaddai.
Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
7 For Judah Nahshon [the] son of Amminadab.
Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
8 For Issachar Nethanel [the] son of Zuar.
Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
9 For Zebulun Eliab [the] son of Helon.
Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
10 For [the] sons of Joseph for Ephraim Elishama [the] son of Ammihud for Manasseh Gamaliel [the] son of Pedahzur.
Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
11 For Benjamin Abidan [the] son of Gideoni.
Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
12 For Dan Ahiezer [the] son of Ammishaddai.
Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
13 For Asher Pagiel [the] son of Ocran.
Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
14 For Gad Eliasaph [the] son of Deuel.
Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
15 For Naphtali Ahira [the] son of Enan.
Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
16 These ([were those] called *Q(K)*) [of] the congregation [the] leaders of [the] tribes of ancestors their [were] [the] heads of [the] families of Israel they.
Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
17 And he took Moses and Aaron the men these who they had been designated by names.
Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
18 And all the congregation they summoned on [day] one of the month second and they recorded their ancestry on clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards to heads their.
ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
19 Just as he had commanded Yahweh Moses and he enrolled them in [the] wilderness of Sinai.
monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
20 And they were [the] descendants of Reuben [the] firstborn of Israel genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names to heads their every male from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
21 Enrolled [men] their of [the] tribe of Reuben [were] six and forty thousand and five hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
22 Of [the] descendants of Simeon genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their enrolled [men] its by [the] number of names to heads their every male from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
23 Enrolled [men] their of [the] tribe of Simeon [were] nine and fifty thousand and three hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
24 Of [the] descendants of Gad genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
25 Enrolled [men] their of [the] tribe of Gad [were] five and forty thousand and six hundred and fifty.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
26 Of [the] descendants of Judah genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
27 Enrolled [men] their of [the] tribe of Judah [were] four and seventy thousand and six hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
28 Of [the] descendants of Issachar genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
29 Enrolled [men] their of [the] tribe of Issachar [were] four and fifty thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
30 Of [the] descendants of Zebulun genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
31 Enrolled [men] their of [the] tribe of Zebulun [were] seven and fifty thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
32 Of [the] descendants of Joseph of [the] descendants of Ephraim genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
33 Enrolled [men] their of [the] tribe of Ephraim [were] forty thousand and five hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
34 Of [the] descendants of Manasseh genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
35 Enrolled [men] their of [the] tribe of Manasseh [were] two and thirty thousand and two hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
36 Of [the] descendants of Benjamin genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
37 Enrolled [men] their of [the] tribe of Benjamin [were] five and thirty thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
38 Of [the] descendants of Dan genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
39 Enrolled [men] their of [the] tribe of Dan [were] two and sixty thousand and seven hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
40 Of [the] descendants of Asher genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
41 Enrolled [men] their of [the] tribe of Asher [were] one and forty thousand and five hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
42 [the] descendants of Naphtali genealogies their to clans their to [the] house of ancestors their by [the] number of names from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare.
Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
43 Enrolled [men] their of [the] tribe of Naphtali [were] three and fifty thousand and four hundred.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
44 These [were] the enrolled [men] whom he enrolled Moses and Aaron and [the] leaders of Israel two [plus] ten man a man one for [the] house of ancestors his they were.
Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
45 And they were all [those] enrolled of [the] people of Israel to [the] house of ancestors their from a son of twenty year[s] and up-wards every [one who] goes forth warfare in Israel.
Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
46 And they were all those enrolled six hundred thousand and three thousand and five hundred and fifty.
Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
47 And the Levites to [the] tribe of ancestors their not they were enrolled in midst of them.
Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
48 And he had spoken Yahweh to Moses saying.
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
49 Only [the] tribe of Levi not you will enroll and head their not you will lift up in among [the] people of Israel.
“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
50 And you appoint the Levites over [the] tabernacle of the testimony and over all articles its and over all that [belongs] to it they they will carry the tabernacle and all articles its and they they will serve it and around the tabernacle they will encamp.
Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
51 And when sets out the tabernacle they will take down it the Levites and when encamps the tabernacle they will raise up it the Levites and the stranger approaching he will be put to death.
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
52 And they will encamp [the] people of Israel everyone at camp his and everyone at standard his to military groups their.
Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
53 And the Levites they will encamp around [the] tabernacle of the testimony and not it will be wrath towards [the] congregation of [the] people Israel and they will keep the Levites [the] duty of [the] tabernacle of the testimony.
Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
54 And they did [the] people of Israel according to all that he had commanded Yahweh Moses so they did.
Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.

< Numbers 1 >