< Numbers 9 >
1 And he spoke Yahweh to Moses in [the] wilderness of Sinai in the year second of going out their from [the] land of Egypt in the month first saying.
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai pa mwezi woyamba wa chaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, nati,
2 Let them observe [the] people of Israel the passover at appointed time its.
“Aisraeli azichita Paska pa nthawi yake yoyikika.
3 On [the] four-teen day in the month this between the evenings you will observe it at appointed time its according to all statutes its and according to all judgments its you will observe it.
Muzichita Paska pa nthawi yake yoyikika, madzulo a tsiku la 14 la mwezi uno, potsata malamulo ndi malangizo ake.”
4 And he spoke Moses to [the] people of Israel to observe the passover.
Choncho Mose anawuza Aisraeli kuti azichita Paska,
5 And they observed the passover in the first [month] on [the] four-teen day of the month between the evenings in [the] wilderness of Sinai according to all that he had commanded Yahweh Moses so they did [the] people of Israel.
ndipo anachitadi Paskayo mʼchipululu cha Sinai madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 And it was people who they were unclean to a corpse of a person and not they were able to observe the passover on the day that and they drew near before Moses and before Aaron on the day that.
Koma ena a iwo sanathe kuchita nawo Paska pa tsiku limenelo chifukwa anali odetsedwa chifukwa chokhudza mtembo. Choncho anabwera kwa Mose ndi Aaroni tsiku lomwelo,
7 And they said the people those to him we [are] unclean to a corpse of a person why? are we restrained to not to bring near [the] offering of Yahweh at appointed time its in among [the] people of Israel.
ndipo anawuza Moseyo kuti, “Ife tadetsedwa chifukwa cha mtembo wa munthu. Nʼchifukwa chiyani taletsedwa kupereka nsembe kwa Yehova pamodzi ndi Aisraeli ena pa nthawi yake?”
8 And he said to them Moses stand so let me hear what? will he command Yahweh of you.
Mose anawayankha kuti, “Dikirani mpaka nditamva zimene Yehova walamula zokhudza Inu.”
9 And he spoke Yahweh to Moses saying.
Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
10 Speak to [the] people of Israel saying a man a man if he will be unclean - to a corpse or on a journey distant to you or to generations your and he will observe a passover to Yahweh.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene wina mwa inu kapena zidzukulu zanu adetsedwa chifukwa chokhudza mtembo wa munthu, kapena akakhala pa ulendo, akhoza kuchita nawo Paska ya Yehova.
11 In the month second on [the] four-teen day between the evenings they will observe it with unleavened bread and bitter herbs they will eat it.
Azichita chikondwererochi madzulo a pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Azidya mwana wankhosa wamwamuna pamodzi ndi buledi wopanda yisiti ndi ndiwo zowawa zamasamba.
12 Not they will leave over any of it until morning and a bone not they will break in it according to every statute of the passover they will observe it.
Iwo asasiye nyama ina iliyonse mpaka mmawa. Asaswe mafupa aliwonse. Pamene akuchita chikondwerero cha Paska, atsate malangizo onse.
13 And the person who he [was] pure and on a journey not he was and he failed to observe the passover and it will be cut off the person that from kinspeople its for - [the] offering of Yahweh not he brought near at appointed time its sin his he will bear the person that.
Koma ngati munthu wina ali woyeretsedwa ndipo sali pa ulendo koma alephera kuchita Paska, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake chifukwa sanabweretse chopereka cha Yehova pa nthawi yake. Munthu ameneyo adzalangidwa chifukwa cha tchimo lake.
14 And if he will sojourn with you a sojourner and he will observe a passover to Yahweh according to [the] statute of the passover and according to judgment its so he will do a statute one it will belong to you and to the sojourner and to [the] native-born of the land.
“‘Mlendo amene akukhala pakati panu, nafuna kuchita nawo Paska ya Yehova, achite nawo motsata malamulo ndi malangizo ake. Muzikhala ndi malangizo ofanana a Paska; mbadwa kapena mlendo.’”
15 And on [the] day set up the tabernacle it covered the cloud the tabernacle of [the] tent of the testimony and in the evening it was over the tabernacle like [the] appearance of fire until morning.
Pa tsiku limene anayimika chihema, tenti ya umboni, mtambo unaphimba chihemacho. Kuyambira madzulo mpaka mmawa, mtambo umene unali pamwamba pa chihemacho unkaoneka ngati moto.
16 Thus it was continually the cloud it covered it and [the] appearance of fire night.
Zinkachitika motere mosalekeza: mtambo unkakhala pamwamba pa chihema, ndipo usiku unkaoneka ngati moto.
17 And to [the] mouth of [the] taking up of the cloud from over the tent and after thus they set out [the] people of Israel and in [the] place where it settled down there the cloud there they encamped [the] people of Israel.
Nthawi ina iliyonse mtambo ukachoka pamwamba pa chihema, Aisraeli ankasamukanso, ndipo paliponse pamene mtambo wayima, Aisraeli ankamangapo misasa.
18 On [the] mouth of Yahweh they set out [the] people of Israel and on [the] mouth of Yahweh they encamped all [the] days which it settled down the cloud over the tabernacle they encamped.
Aisraeli ankasamuka pamalopo Yehova akawalamula, ndipo ankamanganso misasa Iyeyo akawalamula. Nthawi yonse imene mtambowo wayima pa chihema, ankakhalabe mʼmisasa yawo.
19 And when made long the cloud over the tabernacle days many and they kept [the] people of Israel [the] duty of Yahweh and not they set out.
Mtambowo ukakhala pa chihema nthawi yayitali, Aisraeli ankasungabe lamulo la Yehova ndipo iwo sankasamukanso.
20 And there [was] when it was the cloud days number over the tabernacle on [the] mouth of Yahweh they encamped and on [the] mouth of Yahweh they set out.
Nthawi zina mtambowo unkakhala pa chihemapo masiku owerengeka. Aisraeli ankamanga misasa molamulidwa ndi Yehova ndipo ankasamukanso molamulidwa ndi Iyeyo.
21 And there ([was] when *LA(bh)*) it was the cloud from evening until morning and it was taken up the cloud in the morning and they set out or by day and night and it was taken up the cloud and they set out.
Nthawi zina mtambo unkakhala kuyambira madzulo mpaka mmawa ndipo unkachoka mmawa mwake, ankasamuka. Kaya ndi masana kapena usiku, pamene mtambo wachoka, ankasamuka.
22 Or two days or a month or days when made long the cloud over the tabernacle to dwell over it they encamped [the] people of Israel and not they set out and when was taken up it they set out.
Ngakhale mtambo ukhale pa chihema masiku awiri kapena mwezi kapena chaka, Aisraeli ankakhalabe pa msasa osachoka. Koma ukachoka, ankasamuka.
23 On [the] mouth of Yahweh they encamped and on [the] mouth of Yahweh they set out [the] duty of Yahweh they kept on [the] mouth of Yahweh by [the] hand of Moses.
Molamulidwa ndi Yehova ankamanga misasa yawo ndipo ankasamukanso Yehova akawalamula. Ankamvera lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.