< Numbers 2 >

1 And he spoke Yahweh to Moses and to Aaron saying.
Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
2 Everyone at standard his with [the] signs of [the] house of ancestors their they will encamp [the] people of Israel from before around [the] tent of meeting they will encamp.
“Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”
3 And those [who] encamp east-ward east-ward [will be] [the] standard of [the] camp of Judah to military groups their and [the] leader of [the] descendants of Judah [was] Nahshon [the] son of Amminadab.
Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu.
4 And military group his and enrolled [men] their [were] four and seventy thousand and six hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.
5 And those [who] encamp on him [will be] [the] tribe of Issachar and [the] leader of [the] descendants of Issachar [was] Nethanel [the] son of Zuar.
Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara.
6 And military group his and enrolled [men] his [were] four and fifty thousand and four hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.
7 [the] tribe of Zebulun and [the] leader of [the] descendants of Zebulun [was] Eliab [the] son of Helon.
Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni.
8 And military group his and enrolled [men] his [were] seven and fifty thousand and four hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.
9 All those enrolled of [the] camp of Judah [were] one hundred thousand and eighty thousand and six thousand and four hundred to military groups their first they will set out.
Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.
10 [the] standard of [the] camp of Reuben [will be] south-ward to military groups their and [the] leader of [the] descendants of Reuben [was] Elizur [the] son of Shedeur.
Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri.
11 And military group his and enrolled [men] his [were] six and forty thousand and five hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.
12 And those [who] encamp on him [will be] [the] tribe of Simeon and [the] leader of [the] descendants of Simeon [was] Shelumiel [the] son of Zuri-shaddai.
Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai.
13 And military group his and enrolled [men] their [were] nine and fifty thousand and three hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.
14 And [the] tribe of Gad and [the] leader of [the] descendants of Gad [was] Eliasaph [the] son of Reuel.
Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli.
15 And military group his and enrolled [men] their [were] five and forty thousand and six hundred and fifty.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.
16 All those enrolled of [the] camp of Reuben [were] one hundred thousand and one and fifty thousand and four hundred and fifty to military groups their and second they will set out.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.
17 And it will set out [the] tent of meeting [the] camp of the Levites [will be] in [the] middle of the camps just as they will encamp so they will set out each on hand his to standards their.
Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.
18 [the] standard of [the] camp of Ephraim to military groups their [will be] west-ward and [the] leader of [the] descendants of Ephraim [was] Elishama [the] son of Ammihud.
Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi.
19 And military group his and enrolled [men] their [were] forty thousand and five hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.
20 And [will be] on him [the] tribe of Manasseh and [the] leader of [the] descendants of Manasseh [was] Gamaliel [the] son of Pedahzur.
Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri.
21 And military group his and enrolled [men] their [were] two and thirty thousand and two hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.
22 And [the] tribe of Benjamin and [the] leader of [the] descendants Benjamin [was] Abidan [the] son of Gideoni.
Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni.
23 And military group his and enrolled [men] their [were] five and thirty thousand and four hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.
24 All those enrolled of [the] camp of Ephraim [were] one hundred thousand and eight thousand and one hundred to military groups their and third they will set out.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.
25 [the] standard of [the] camp of Dan [will be] north-ward to military groups their and [the] leader of [the] descendants of Dan [was] Ahiezer [the] son of Ammishaddai.
Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 And military group his and enrolled [men] their [were] two and sixty thousand and seven hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.
27 And those [who] encamp on him [will be] [the] tribe of Asher and [the] leader of [the] descendants of Asher [was] Pagiel [the] son of Ocran.
Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani.
28 And military group his and enrolled [men] their [were] one and forty thousand and five hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.
29 And [the] tribe of Naphtali and [the] leader of [the] descendants of Naphtali [was] Ahira [the] son of Enan.
Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani.
30 And military group his and enrolled [men] their [were] three and fifty thousand and four hundred.
Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.
31 All those enrolled of [the] camp of Dan [were] one hundred thousand and seven and fifty thousand and six hundred to the last they will set out to standards their.
Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.
32 These [were] [the] [men] enrolled of [the] people of Israel to [the] house of ancestors their all [those] enrolled of the camps to military groups their [were] six hundred thousand and three thousand and five hundred and fifty.
Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo.
33 And the Levites not they were enrolled in among [the] people of Israel just as he had commanded Yahweh Moses.
Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.
34 And they did [the] people of Israel according to all that he had commanded Yahweh Moses so they camped to standards their and so they set out everyone to clans his on [the] house of ancestors his.
Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.

< Numbers 2 >