< Nehemiah 1 >
1 [the] words of Nehemiah [the] son of Hacaliah and it was in [the] month of (Kislev *Q(k)*) year twenty and I I was in Susa the citadel.
Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya: Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa,
2 And he came Hanani one of brothers my he and people from Judah and I asked them about the Jews the escaped remnant who they had survived from the captivity and on Jerusalem.
Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.
3 And they said to me the survivors who they have survived from the captivity there in the province [are] in trouble great and in disgrace and [the] wall of Jerusalem [has been] broken down and gates its they have been burned with fire.
Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”
4 And it was when heard I - the words these I sat down and I wept and I mourned! days and I was fasting and praying before [the] God of the heavens.
Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba.
5 And I said I beg you O Yahweh [the] God of the heavens the God great and awesome [who] keeps the covenant and covenant loyalty to [those who] love him and to [those who] keep commandments his.
Ndinkati: “Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu.
6 May it be please ear your attentive and eyes your open to listen to [the] prayer of servant your which I [am] praying before you this day by day and night on [the] people of Israel servants your and [am] confessing on [the] sins of [the] people of Israel which we have sinned to you and I and [the] house of father my we have sinned.
Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani.
7 Surely we have acted corruptly to you and not we have kept the commandments and the statutes and the judgments which you commanded Moses servant your.
Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.
8 Remember please the word which you commanded Moses servant your saying you you will act unfaithfully I I will scatter you among the peoples.
“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina.
9 And you will turn back to me and you will keep commandments my and you will observe them if it will be banished [one] your at [the] end of the heavens from there I will gather them (and I will bring them *Q(k)*) to the place where I have chosen to cause to dwell name my there.
Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’
10 And they [are] servants your and people your whom you redeemed by strength your great and by hand your mighty.
“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
11 I beg you O Lord may it be please ear your attentive to [the] prayer of servant your and to [the] prayer of servants your delighting to fear name your and grant success! please to servant your this day and give him compassion before the man this and I I was cup bearer of the king.
Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.” Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.