< Nahum 1 >
1 [the] oracle of Nineveh [the] document of [the] vision of Nahum the Elkoshite.
Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
2 [is] a God Jealous and avenging Yahweh [is] avenging Yahweh and a lord of rage [is] avenging Yahweh to opponents his and [is] maintaining he to enemies his.
Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
3 Yahweh [is] long of anger (and great of *Q(K)*) power and certainly not he will leave unpunished Yahweh [is] in storm-wind and in storm way his and [is] cloud [the] dust of feet his.
Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
4 [he is] rebuking the Sea and he made dry it and all the rivers he dries up it withers Bashan and Carmel and [the] blossom of Lebanon it withers.
Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
5 Mountains they quake from him and the hills they melt and it lifted up the earth from before him and [the] world and all [those who] dwell in it.
Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
6 Before indignation his who? will he stand and who? will he endure at [the] burning of anger his rage his it is poured out like fire and the rocks they are pulled down from him.
Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
7 [is] good Yahweh a refuge in a day of trouble and [he is] knowing [those who] take refuge in him.
Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
8 And with a flood [which] passes over complete destruction he will make place its and enemies his he will pursue darkness.
koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
9 Whatever you will plot! against Yahweh complete destruction he [will be] making not it will arise two times trouble.
Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
10 For to thorns interwoven and like drink their drunkards they will be consumed like stubble dry full.
Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
11 From you he has come out [one who] plots on Yahweh evil a counselor of worthlessness.
Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
12 Thus - he says Yahweh though complete and thus numerous and thus they will be cut down and he will pass away and I have afflicted you not I will afflict you again.
Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
13 And now I will break yoke-bar his from on you and fetters your I will tear apart.
Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
14 And he has commanded on you Yahweh not it will be sown from name your again from [the] house of gods your I will cut off idol and molten image I will make grave your for you are insignificant.
Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
15 There! on the mountains [the] feet of [one who] bears news [one who] proclaims peace celebrate a festival O Judah festivals your pay vows your for not he will repeat again (to pass *Q(k)*) in you a worthless person all of him it will be cut off.
Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.