< Mark 10 >

1 And from there having risen up He comes into the region of Judea (and *N(k)O*) (*k*) beyond the Jordan, And come together again crowds to Him, and as He had been accustomed again He was teaching them.
Ndipo Yesu anachoka pamalowo ndi kupita kudera la Yudeya ndi kutsidya la mtsinje wa Yorodani. Magulu a anthu anabweranso kwa Iye, ndipo monga mwachizolowezi chake anawaphunzitsa.
2 And having come to [him] (the *k*) Pharisees (were questioning *N(k)O*) Him if it is lawful for a husband a wife to divorce testing Him.
Afarisi ena anabwera kudzamuyesa pomufunsa kuti, “Kodi malamulo amalola kuti mwamuna asiye mkazi wake?”
3 And He answering said to them; What you did command Moses?
Iye anayankha kuti, “Kodi Mose anakulamulani chiyani?”
4 And they said; Permitted Moses a roll of divorce to write and to send [her] away.
Iwo anati, “Mose amaloleza mwamuna kulemba kalata ya chisudzulo ndi kumuchotsa mkazi.”
5 (and answering *k*) (But *no*) Jesus said to them; Because of the hardness of heart of you He wrote for you commandment this;
Yesu anayankha kuti, “Mose anakulemberani lamulo ili chifukwa chakuwuma kwa mitima yanu.
6 From however [the] beginning of creation Male and female He made them’ (*k*) (God; *K*)
Koma pachiyambi cha chilengedwe, Mulungu ‘analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.’
7 On account of this will leave a man the father of him and mother and will be joined to wife of him,
‘Pa chifukwa ichi mwamuna adzasiya abambo ake ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake,
8 and will be the two for flesh one’ Therefore no longer no longer they are two but one flesh.
ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.’ Potero sali awirinso, koma mmodzi.
9 What therefore God has joined together, man not should separate.
Chifukwa chake chimene Mulungu wachilumikiza pamodzi, munthu wina asachilekanitse.”
10 And (in the house *N(k)O*) again the disciples (of it *k*) concerning (the [meaning] of *k*) (this were questioning *N(k)O*) Him.
Pamene analinso mʼnyumba, ophunzira anamufunsa Yesu za izi.
11 And He says to them; Who[ever] (maybe *N(k)O*) shall divorce the wife of him and shall marry another, commits adultery against her.
Iye anayankha kuti, “Aliyense amene aleka mkazi wake ndi kukakwatira wina achita chigololo kulakwira mkaziyo.
12 And if (she *N(K)O*) (having divorced *N(k)O*) the husband of her (and *k*) (shall marry another, *N(k)O*) she commits adultery.
Ndipo akasiya mwamuna wake ndi kukakwatiwa ndi wina, achita chigololo.”
13 And they were bringing to Him little children that them He may touch; But the disciples (rebuked those *N(k)O*) (bringing [them]. *KO*)
Anthu anabweretsa ana kwa Yesu kuti awadalitse, koma ophunzira anawadzudzula.
14 Having seen now Jesus was indignant and He said to them; do permit the little children to come to Me, (and *k*) not do hinder them! To the for sof uch belongs the kingdom of God.
Pamene Yesu anaona zimenezi anayipidwa. Anati kwa iwo, “Lolani ana abwere kwa Ine, ndipo musawaletse, pakuti Ufumu wa Mulungu uli wa onga awa.
15 Amen I say to you, who[ever] (only *N(k)O*) unless shall receive the kingdom of God as a child, certainly not shall enter into it.
Ndikukuwuzani choonadi, aliyense amene sadzalandira Ufumu wa Mulungu ngati kamwana sadzalowamo.”
16 And having embraced them (he was greatly blessing *N(k)O*) having laid the hands on them.
Ndipo ananyamula ana mʼmanja ake, ndi kuyika manja ake pa iwo nawadalitsa.
17 And when is going forth He on [the] journey having run up one and he having knelt down to Him he was asking Him; Teacher good, what shall I do that life eternal I may inherit? (aiōnios g166)
Yesu atanyamuka, munthu wina anamuthamangira nagwa mogwada pamaso pake. Iye anafunsa kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
18 And Jesus said to him; Why Me you call good? No [one is] good only except one God.
Yesu anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukunditchula wabwino? Palibe wabwino koma Mulungu yekha.
19 The commandments you know: Not shall you murder not shall you commit adultery not shall you steal, not shall you bear false witness, not shall you defraud, do honor the father of you and the mother.’
Iwe umadziwa malamulo: ‘Usaphe, usachite chigololo, usabe, usapereke umboni wonama, usachite chinyengo, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
20 And (answering *ko*) (he was saying *N(k)O*) to Him; Teacher, these all I have kept from [the] youth of me.
Iye anati, “Aphunzitsi zonsezi ndinazisunga kuyambira ndili mnyamata.”
21 And Jesus having looked upon him He loved him and He said to him; One thing (to you *N(k)O*) is lacking; do go, as much as you have do sell and do give to the poor and you will have treasure in heaven. and come, do follow Me (having taken up cross. *K*)
Yesu anamuyangʼana ndi kumukonda nati, “Ukusowa chinthu chimodzi. Pita, kagulitse zonse zimene uli nazo ndipo kapereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Ndipo ukabwere ndi kunditsata Ine.”
22 And having been sad at the word he went away grieving; he was [one] for having possessions many.
Pa chifukwa ichi nkhope yake inagwa. Anachoka ali wachisoni, chifukwa anali ndi chuma chambiri.
23 And having looked around Jesus says to the disciples of Him; How difficultly those riches having into the kingdom of God will enter!
Yesu anayangʼanayangʼana ndipo anati kwa ophunzira ake, “Nʼkovutadi kuti achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!”
24 And the disciples were astonished at the words of Him. But Jesus again answering He says to them; Children, how difficult it is (having trusted upon *KO*) (*K*) (riches *KO*) into the kingdom of God to enter!
Ophunzira anadabwa ndi mawu ake. Koma Yesu anatinso, “Ananu, nʼkovutadi kulowa mu ufumu wakumwamba!
25 Easier it is [for] a camel through the eye of the needle (to pass *N(k)O*) than [for] a rich man into the kingdom of God to enter.
Ndi kwapafupi kwa ngamira kuti idzere pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kuti alowe mu ufumu wa Mulungu.”
26 And exceedingly they were astonished saying among (themselves; *NK(O)*) Then who is able to be saved?
Ophunzira anadabwa kwambiri, ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
27 Having looked (now *k*) on them Jesus says; With men [it is] impossible but not [is impossible] with (*k*) God; all things for [are] possible (is *k*) with God.
Yesu anawayangʼana ndipo anati, “Kwa munthu zimenezi nʼzosatheka, koma osati ndi Mulungu; zinthu zonse zimatheka ndi Mulungu.”
28 (and *k*) Began to say Peter to Him; Behold we ourselves left all and (have followed *N(k)O*) You.
Petro anati kwa Iye, “Ife tasiya zonse ndi kukutsatani!”
29 (answering *ko*) (now *k*) (Was saying *N(k)O*) Jesus; Amen I say to you, no [one] there is who has left house or brothers or sisters or mother or father (or wife *K*) or children or lands because of me and (because *no*) of the gospel,
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti palibe aliyense amene wasiya nyumba kapena abale kapena alongo kapena amayi kapena abambo kapena ana kapena minda chifukwa cha Ine ndi Uthenga Wabwino
30 only unless shall take a hundredfold now in time this — houses and brothers and sisters and (mothers *NK(o)*) and children and lands with persecutions — and in the age which is coming life eternal. (aiōn g165, aiōnios g166)
adzalephera kulandira 100 (nyumba, abale, alongo, amayi, ana ndi minda, pamodzi ndi mazunzo) mʼbado uno ndi moyo wosatha nthawi ya mʼtsogolo. (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Many however will be first last and the last first.
Koma ambiri amene ndi woyambirira adzakhala omalizira, ndipo omalizira adzakhala oyambirira.”
32 They were then on the way going up to Jerusalem, and was going on before them Jesus, and they were astonished; (those *no*) (then *N(k)O*) following were afraid. And having brought to [Himself] again the Twelve He began them to tell the [things] are being soon to Him to happen
Ali pa ulendo wawo wopita ku Yerusalemu, Yesu ali patsogolo, ophunzira ake anadabwa, ndipo amene amamutsatira amachita mantha. Anatenganso ophunzira ake khumi ndi awiri pa mbali ndipo anawawuza zimene zikamuchitikire Iye.
33 that Behold we go up to Jerusalem, and the Son of Man will be betrayed to the chief priests and to the scribes, and they will condemn Him to death and will betray Him to the Gentiles
Iye anati, “Ife tikupita ku Yerusalemu ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo. Adzamuweruza kuti aphedwe ndipo adzamupereka kwa anthu a mitundu ina,
34 And they will mock Him and will spit upon Him and will flog Him and will kill (him *ko*) and (on [the] third day *N(k)O*) He will rise again.
amene adzamuchita chipongwe ndi kumuthira malovu, kumukwapula ndi kumupha. Patatha masiku atatu adzauka.”
35 And come up to Him James and John, the (two *O*) sons of Zebedee, saying (to Him; *no*) Teacher, we desire that whatever if we shall ask (you *no*) You shall do for us.
Ndipo Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anabwera kwa Iye ndipo anati, “Aphunzitsi, tikufuna kuti mutichitire ife chilichonse chimene tipemphe.”
36 And He said to them; What do you desire Me (I may do *N(k)O*) for you?
Iye anafunsa kuti, “Kodi mukufuna ndikuchitireni chiyani?”
37 And they said to Him; do grant to us that one of [us] at right [hand] and one at (left [hand] *N(k)O*) (of you *k*) let us sit in the glory of You.
Iwo anayankha kuti, “Timafuna kuti mmodzi wa ife adzakhale kumanja ndi wina kumanzere mu ulemerero wanu.”
38 And Jesus said to them; Not you know what you ask. Are you able to drink the cup which I myself drink (or *N(k)O*) the baptism which I myself am baptized to be baptized [with]?
Yesu anati, “Simukudziwa chimene mukupempha. Kodi mungamwere chikho chimene ndidzamwera kapena kubatizidwa ndi ubatizo umene ndibatizidwe nawo?”
39 And they said to Him; We are able. And Jesus said to them; The (indeed *k*) cup which I myself drink you will drink, and the baptism which I myself am baptized you will be baptized [with];
Iwo anayankha kuti, “Tikhoza.” Yesu anawawuza kuti, “Mudzamweradi chikho chimene Ine ndidzamwera, ndi kubatizidwa ndi ubatizo umene Ine ndidzabatizidwe nawo,
40 but to sit at [the] right hand of Me (or *N(k)O*) at [the] left hand (of me *k*) not is Mine to give but [to those] for whom it has been prepared.
koma kukhala kumanja kapena kumanzere si Ine wopereka. Malo awa ndi a amene anasankhidwiratu.”
41 And having heard [this] the ten began to be indignant about James and John.
Ophunzira khumiwo otsalawo atamva izi anapsera mtima Yakobo ndi Yohane.
42 (*k*) (And *no*) (now *k*) having called near them Jesus says to them; You know that those being accounted to rule over the Gentiles exercise lordship over them, and those great ones of them exercise authority over them.
Yesu anawayitana pamodzi nati, “Inu mukudziwa kuti iwo amene amadziyesa ngati atsogoleri a anthu amitundu ina amadyera anthu awo masuku pamutu. Akuluakulu awonso amaonetsadi mphamvu zawo pa iwo.
43 Not thus however (is it *N(k)O*) among you, Instead who[ever] (maybe *N(k)O*) shall desire great to become among you, will be your servant;
Sizili choncho ndi inu. Mʼmalo mwake, amene akufuna kukhala wamkulu pakati panu ayenera kukhala wotumikira,
44 and who[ever] (maybe *NK(o)*) shall desire (among *no*) (you to become *N(k)O*) first, will be of all slave.
ndipo aliyense amene akufuna kukhala wamkulu akhale kapolo wa onse.
45 Even for the Son of Man not came to be served but to serve and to give the life of Him [as] a ransom for many.
Pakuti ngakhale Mwana wa Munthu sanabwere kudzatumikiridwa, koma kudzatumikira, ndi kupereka moyo wake kuti ukhale dipo la anthu ambiri.”
46 And they come to Jericho. And when was going out He from Jericho — and the disciples of Him and a crowd large — (the *no*) son of Timaeus Bartimaeus, (the *k*) blind (beggar, *N(k)O*) was sitting beside the road.
Ndipo anafika ku Yeriko. Pamene Yesu ndi ophunzira ake, pamodzi ndi gulu lalikulu la anthu, ankatuluka mu mzinda, munthu wosaona, Bartumeyu (mwana wa Tumeyu), amakhala mʼmbali mwa msewu ali kupempha.
47 And having heard that Jesus (of Nazareth *N(k)O*) it is, he began to cry out and to say; (O *k*) Son of David Jesus, do have mercy on me.
Pamene anamva kuti anali Yesu wa ku Nazareti, anayamba kufuwula kuti, “Yesu, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
48 And were rebuking him many that he may be silent. but much more he was crying out; Son of David, do have mercy on me.
Ambiri anamukalipira ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulitsabe kuti, “Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
49 And having stopped Jesus commanded: (do call *N(k)O*) him. And they call the blind [man] saying to him; take courage! (do rise up *N(k)O*) He calls you.
Yesu anayima nati, “Muyitaneni.” Ndipo anamuyitana kuti, “Kondwera! Imirira! Akukuyitana.”
50 And having cast away the cloak of him (having jumped up *N(k)O*) he came to Jesus.
Anaponya mkanjo wake kumbali, analumpha nabwera kwa Yesu.
51 And answering to him Jesus (said; *N(k)O*) What to you do you desire I may do And the blind [man] said to Him; Rabboni, that I may receive sight.
Yesu anamufunsa kuti, “Ukufuna ndikuchitire chiyani?” Wosaonayo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndikufuna ndione.”
52 (And *no*) (now *ko*) Jesus said to him; do go, the faith of you has healed you. And immediately he received sight and he was following (Him *N(k)O*) (Jesus *k*) on the way.
Yesu anati, “Pita, chikhulupiriro chako chakuchiritsa!” Nthawi yomweyo anapenya, nʼkumatsatira Yesu pa ulendowo.

< Mark 10 >