< Malachi 2 >
1 And now [is] to you the commandment this O priests.
“Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.”
2 If not you will listen and if not you will put on heart to give honor to name my he says Yahweh of hosts and I will send on you the curse and I will curse blessings your and also I have cursed it for not you [are] putting on heart.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”
3 Here I [am] about to rebuke of you the offspring and I will spread dung on faces your [the] dung of festivals your and someone will carry away you with it.
“Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.”
4 And you will know that I have sent to you the commandment this to be covenant my with Levi he says Yahweh of hosts.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire.
5 Covenant my - it was with him life and well-being and I gave them to him fear and he feared me and because of name my he was in awe he.
Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa.
6 Instruction of truth it was in mouth his and unrighteousness not it was found on lips his in peace and in uprightness he walked with me and many [people] he turned away from iniquity.
Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.
7 For [the] lips of a priest they will preserve knowledge and instruction people will seek from mouth his for [is] [the] messenger of Yahweh of hosts he.
“Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse.
8 And you you have turned aside from the way you have caused to stumble many [people] by the instruction you have corrupted [the] covenant of Levi he says Yahweh of hosts.
Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 And also I I have made you despised and lowly to all the people according to [the] mouth of that not you [are] keeping ways my and [you are] lifting up faces in instruction.
“Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”
10 ¿ Not [does] a father one [belong] to all of us ¿ not God one did he create us why? do we deal treacherously each with brother his to profane [the] covenant of ancestors our.
Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?
11 It has acted treacherously Judah and an abomination it has been done in Israel and in Jerusalem for - it has profaned Judah [the] sanctuary of Yahweh which he loves and it has married a daughter of a god of foreignness.
Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo.
12 May he cut off Yahweh the person who he does it a protector and [one who] answers from [the] tents of Jacob and [one who] brings near an offering to Yahweh of hosts.
Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.
13 And this second [thing] you do to cover tear[s] [the] altar of Yahweh weeping and groaning from not still turning to the offering and to take pleasure from hand your.
China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu.
14 And you say concerning what? on for Yahweh he has testified between you and between - [the] wife of youth your whom you you have dealt treacherously with her and she [was] companion your and [the] wife of covenant your.
Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.
15 And not one he made and a remnant of spirit to him and what? [was] the one seeking offspring of God and you will take heed in spirit your and with [the] wife of youth your may not anyone deal treacherously.
Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.
16 For he hates sending away he says Yahweh [the] God of Israel and he will cover violence over clothing his he says Yahweh of hosts and you will take heed in spirit your and not you must act treacherously.
Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.
17 You have wearied Yahweh with words your and you say how? did we weary [him] by saying you every [one who] does evil [is] good - in [the] eyes of Yahweh and in them he he delights or where? [is] [the] God of justice.
Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu. Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?” Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”