< Leviticus 16 >

1 And he spoke Yahweh to Moses after [the] death of [the] two [the] sons of Aaron when drew near they before Yahweh and they died.
Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
2 And he said Yahweh to Moses speak to Aaron brother your and may not he come at every time into the holy place from inside to the curtain to [the] face of the atonement cover which [is] on the ark and not he will die for in the cloud I will appear over the atonement cover.
Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
3 With this he will come Aaron into the holy place with a bull a young one of [the] herd to a sin offering and a ram to a burnt offering.
“Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
4 A tunic of linen of holiness he will wear and undergarments of linen they will be on flesh his and with a sash of linen he will gird himself and with a turban of linen he will wind [are] garments of holiness they and he will wash with water body his and he will put on them.
Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
5 And from with [the] congregation of [the] people of Israel he will take two male goats of goats to a sin offering and a ram one to a burnt offering.
Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
6 And he will present Aaron [the] bull of the sin offering which [is] for himself and he will make atonement for himself and for household his.
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
7 And he will take [the] two the male goats and he will station them before Yahweh [the] entrance of [the] tent of meeting.
Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
8 And he will put Aaron on [the] two the male goats lots a lot one for Yahweh and a lot one for [the] escape goat.
Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
9 And he will present Aaron the male goat which it came up on it the lot for Yahweh and he will offer it a sin offering.
Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
10 And the male goat which it came up on it the lot for [the] escape goat it will be stationed alive before Yahweh to make atonement on it by sending away it to [the] escape goat the wilderness towards.
Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
11 And he will present Aaron [the] bull of the sin offering which [is] for himself and he will make atonement for himself and for household his and he will cut [the] throat of [the] bull of the sin offering which [is] for himself.
“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
12 And he will take fullness of censer coals of fire from on the altar from to before Yahweh and [the] fullness of hands his incense of perfume fine and he will bring [them] from inside to the curtain.
Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
13 And he will put the incense on the fire before Yahweh and it will cover - [the] cloud of the incense the atonement cover which [is] on the testimony and not he will die.
Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
14 And he will take some of [the] blood of the bull and he will spatter [it] with finger his on [the] face of the atonement cover east-ward and before the atonement cover he will spatter seven times some of the blood with finger his.
Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
15 And he will cut [the] throat of [the] male goat of the sin offering which [is] for the people and he will bring blood its to from inside to the curtain and he will do with blood its just as he did to [the] blood of the bull and he will spatter it on the atonement cover and before the atonement cover.
“Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
16 And he will make atonement on the holy place from [the] uncleanness of [the] people of Israel and from transgressions their to all sins their and thus he will do to [the] tent of meeting which dwells with them in among uncleanness their.
Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
17 And any person not he will be - in [the] tent of meeting when goes he to make atonement in the holy place until comes out he and he has made atonement for himself and for household his and for all [the] assembly of Israel.
Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
18 And he will go out to the altar which [is] before Yahweh and he will make atonement on it and he will take some of [the] blood of the bull and some of [the] blood of the male goat and he will put [it] on [the] horns of the altar all around.
“Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
19 And he will spatter on it some of the blood with finger his seven times and he will purify it and he will set apart as holy it from [the] uncleanness of [the] people of Israel.
Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
20 And he will finish from making atonement for the holy place and [the] tent of meeting and the altar and he will present the male goat living.
“Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
21 And he will lean Aaron [the] two (hands his *Q(K)*) on [the] head of the male goat living and he will confess over it all [the] iniquities of [the] people of Israel and all transgressions their to all sins their and he will put them on [the] head of the male goat and he will send [it] away by [the] hand of a man ready the wilderness towards.
Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
22 And it will bear the male goat on itself all iniquities their into a land infertile and he will let go the male goat in the wilderness.
Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
23 And he will go Aaron into [the] tent of meeting and he will strip off [the] garments of linen which he wore when went he into the holy place and he will leave them there.
“Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
24 And he will wash body his with water in a place holy and he will put on garments his and he will come out and he will offer burnt offering his and [the] burnt offering of the people and he will make atonement for himself and for the people.
Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
25 And [the] fat of the sin offering he will make smoke the altar towards.
Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
26 And the [one who] let go the male goat to [the] escape goat he will wash garments his and he will wash body his with water and after thus he will come into the camp.
“Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
27 And [the] bull of the sin offering and - [the] male goat of the sin offering which it was brought blood their to make atonement in the holy place someone will bring out to from [the] outside of the camp and people will burn with fire hides their and flesh their and offal their.
Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
28 And the [one who] burns them he will wash garments his and he will wash body his with water and after thus he will come into the camp.
Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
29 And it will become for you a statute of perpetuity in the month seventh on the ten of the month you will afflict selves your and any work not you will do the native-born and the sojourner who sojourns in midst of you.
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
30 For on the day this he will make atonement on you to purify you from all sins your before Yahweh you will be pure.
chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
31 [is] a sabbath of Sabbath observance it to you and you will afflict selves your a statute of perpetuity.
Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
32 And he will make atonement the priest whom someone will anoint him and whom someone will fill hand his to serve as priest in place of father his and he will wear [the] garments of linen [the] garments of holiness.
Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
33 And he will make atonement for [the] sanctuary of holiness and [the] tent of meeting and the altar he will make atonement for and on the priests and on all [the] people of the assembly he will make atonement.
Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
34 And it will become this for you a statute of perpetuity to make atonement on [the] people of Israel from all sins their one [time] in the year and he did just as he had commanded Yahweh Moses.
“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.

< Leviticus 16 >