< Leviticus 14 >

1 And he spoke Yahweh to Moses saying.
Yehova anawuza Mose kuti,
2 This it will be [the] legal [procedure] of the [one who] has a serious skin disease on [the] day of purification his and he will be brought to the priest.
“Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
3 And he will go out the priest to from [the] outside of the camp and he will see the priest and there! it has been healed [the] plague of the serious skin disease from the [one who] had a serious skin disease.
Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
4 And he will command the priest and someone will take for the [one] purifying himself two birds living pure and wood of cedar and scarlet of a worm and hyssop.
wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
5 And he will command the priest and someone will cut [the] throat of the bird one into a vessel of earthenware over water living.
Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
6 The bird living he will take it and [the] wood of cedar and [the] scarlet of the worm and the hyssop and he will dip them and - the bird living in [the] blood of the bird [which] had the throat cut over the water living.
Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
7 And he will spatter [it] on the [one] purifying himself from the serious skin disease seven times and he will declare pure him and he will let go the bird living over [the] surface of the field.
Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
8 And he will wash the [one] purifying himself garments his and he will shave all hair his and he will wash with water and he will be pure and after he will come into the camp and he will remain from [the] outside of tent his seven days.
“Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
9 And it will be on the day seventh he will shave all hair his head his and beard his and [the] eyebrows of eyes his and all hair his he will shave and he will wash garments his and he will wash body his with water and he will be pure.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
10 And on the day eighth he will take two male lambs unblemished and a ewe-lamb one a daughter of year its unblemished and three tenths fine flour a grain offering mixed with oil and a log one oil.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
11 And he will station the priest who declares pure the person who is purifying himself and with them before Yahweh [the] entrance of [the] tent of meeting.
Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
12 And he will take the priest the male lamb one and he will present it to a guilt offering and [the] log of oil and he will wave them a wave-offering before Yahweh.
“Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
13 And he will cut [the] throat of the male lamb in [the] place where someone cuts [the] throat of the sin offering and the burnt offering in [the] place of holiness for like the sin offering the guilt offering it [belongs] to the priest [is] a holy thing of holy things it.
Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
14 And he will take the priest some of [the] blood of the guilt offering and he will put [it] the priest on [the] lobe of [the] ear of the [one] purifying himself right and on [the] thumb of hand his right and on [the] big toe of foot his right.
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
15 And he will take the priest some of [the] log of oil and he will pour [it] on [the] palm of the priest left.
Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
16 And he will dip the priest finger his right some of the oil which [is] on palm his left and he will spatter some of the oil with finger his seven times before Yahweh.
aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
17 And some of [the] remainder of the oil which [is] on palm his he will put the priest on [the] lobe of [the] ear of the [one] purifying himself right and on [the] thumb of hand his right and on [the] big toe of foot his right on [the] blood of the guilt offering.
Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
18 And the remainder in the oil which [is] on [the] palm of the priest he will put on [the] head of the [one] purifying himself and he will make atonement on him the priest before Yahweh.
Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
19 And he will offer the priest the sin offering and he will make atonement on the [one] purifying himself from uncleanness his and after he will cut [the] throat of the burnt offering.
“Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
20 And he will offer up the priest the burnt offering and the grain offering the altar towards and he will make atonement on him the priest and he will be clean.
ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
21 And if [is] poor he and not hand his [is] reaching and he will take a male lamb one a guilt offering to a wave-offering to make atonement on himself and a tenth of fine flour one mixed with oil to a grain offering and a log of oil.
“Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
22 And two turtle-doves or two young ones of a dove which it will reach hand his and it will be one [bird] a sin offering and the one a burnt offering.
Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
23 And he will bring them on the day eighth for purification his to the priest to [the] entrance of [the] tent of meeting before Yahweh.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
24 And he will take the priest [the] male lamb of the guilt offering and [the] log of oil and he will wave them the priest a wave-offering before Yahweh.
Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
25 And he will cut [the] throat of [the] male lamb of the guilt offering and he will take the priest some of [the] blood of the guilt offering and he will put [it] on [the] lobe of [the] ear of the [one] purifying himself right and on [the] thumb of hand his right and on [the] big toe of foot his right.
Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
26 And some of the oil he will pour the priest on [the] palm of the priest left.
Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
27 And he will spatter the priest with finger his right some of the oil which [is] on palm his left seven times before Yahweh.
ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
28 And he will put the priest some of the oil - which [is] on palm his on [the] lobe of [the] ear of the [one] purifying himself right and on [the] thumb of hand his right and on [the] big toe of foot his right on [the] place of [the] blood of the guilt offering.
Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
29 And the remainder of the oil which [is] on [the] palm of the priest he will put on [the] head of the [one] purifying himself to make atonement on him before Yahweh.
Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
30 And he will offer the one of the turtle-doves or of [the] young ones of the dove from [that] which it will reach hand his.
Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
31 [that] which It will reach hand his the one [bird] a sin offering and the one a burnt offering with the grain offering and he will make atonement the priest on the [one] purifying himself before Yahweh.
imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
32 This [is] [the] legal [procedure] of [one] whom [was] in him a plague of a serious skin disease who not it will reach hand his for purification his.
“Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
33 And he spoke Yahweh to Moses and to Aaron saying.
“Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
34 That you will go into [the] land of Canaan which I [am] about to give to you to a possession and I will put a plague of a serious disease in [the] house of [the] land of possession your.
Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
35 And he will come [the one] whom [belongs] to him the house and he will tell to the priest saying like a plague it has appeared to me in the house.
mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
36 And he will command the priest and people will make clear the house before he will go the priest to see the plague and not it will be unclean all that [is] in the house and after thus he will go the priest to see the house.
Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
37 And he will see the plague and there! the plague [is] in [the] walls of the house depressions greenish or reddish and appearance their [is] deep more than the wall.
Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
38 And he will go out the priest from the house to [the] entrance of the house and he will shut up the house seven days.
wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
39 And he will return the priest on the day seventh and he will see and there! it has spread the plague in [the] walls of the house.
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
40 And he will command the priest and people will tear out the stones which [is] in them the plague and they will throw them to from [the] outside of the city to a place unclean.
wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
41 And the house he will scrape from inside all around and they will pour out the dust which they have scraped off to from [the] outside of the city to a place unclean.
Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
42 And they will take stones other and they will bring [them] to in place of the stones and dust other he will take and he will plaster the house.
Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
43 And if it will return the plague and it will break out in the house after tears out the stones and after has scraped the house and after was plastered.
“Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
44 And he will come the priest and he will see and there! it has spread the plague in the house [is] a serious disease malignant it in the house [is] unclean it.
wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
45 And he will pull down the house stones its and wood its and all [the] dust of the house and he will take [them] out to from [the] outside of the city to a place unclean.
Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
46 And the [one who] goes into the house all [the] days [which] he has shut up it he will be unclean until the evening.
“Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
47 And the [one who] lies down in the house he will wash garments his and the [one who] eats in the house he will wash garments his.
Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
48 And if indeed he will come the priest and he will see and there! not it has spread the plague in the house after was plastered the house and he will declare pure the priest the house for it has been healed the plague.
“Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
49 And he will take to cleanse from sin the house two birds and wood of cedar and scarlet of a worm and hyssop.
Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
50 And he will cut [the] throat of the bird one into a vessel of earthenware over water living.
Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
51 And he will take [the] wood of cedar and the hyssop and - [the] scarlet of the worm and the bird living and he will dip them in [the] blood of the bird [which] had the throat cut and in the water living and he will spatter [it] to the house seven times.
Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
52 And he will cleanse from sin the house with [the] blood of the bird and with the water living and with the bird living and with [the] wood of cedar and with the hyssop and with [the] scarlet of the worm.
Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
53 And he will let go the bird living to from [the] outside of the city to [the] surface of the field and he will make atonement on the house and it will be pure.
Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
54 This [is] the legal [procedure] to every plague of serious skin disease and to scall.
Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
55 And to [the] serious disease of clothing and to house.
nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
56 And to swelling and to flaking skin and to bright spot.
khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
57 To teach on [the] day of the unclean [thing] and on [the] day of the pure [thing] this [is] [the] legal [procedure] of serious skin disease.
kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.

< Leviticus 14 >