< Judges 8 >
1 And they said to him [the] man of Ephraim what? [is] the thing this [which] you have done to us to not to summon us that you went to fight against Midian and they quarreled! with him with force.
Aefereimu anafunsa Gideoni kuti, “Nʼchifukwa chiyani watichita zimenezi? Bwanji sunatiyitane pamene umakamenyana ndi Amidiyani?” Iwo anamudzudzula kwambiri.
2 And he said to them what? have I done now like you ¿ not good [are] [the] gleanings of Ephraim more than [the] grape harvest of Abiezer.
Koma iye anawayankha kuti, “Nʼchiyani ndachita kuyerekeza ndi zimene mwachita inu? Kodi zimene mwachita inu Aefereimu si zazikulu kuposa zimene fuko langa la Abiezeri lachita?
3 In hand your he has given God [the] commanders of Midian Oreb and Zeeb and what? have I been able to do like you then it relaxed spirit their from on him when said he the word this.
Mulungu wapereka mafumu a Midiyani, Orebu ndi Zeebu mʼmanja mwanu. Ndachita chiyani kuyerekeza ndi zimene mwachita inu?” Atanena izi, anthuwo mitima yawo inatsika.
4 And he came Gideon the Jordan towards [was] passing over he and three hundred the man who [were] with him [were] exhausted and pursuing.
Gideoni anafika ndi kuwoloka mtsinje wa Yorodani pamodzi ndi anthu 300 amene anali naye. Ngakhale kuti anali otopa anapirikitsabe adani awo.
5 And he said to [the] people of Succoth give please round loaves of bread to the people which [is] at feet my for [are] exhausted they and I [am] pursuing after Zebah and Zalmunna [the] kings of Midian.
Atafika ku Sukoti anapempha anthu a kumeneko kuti, “Chonde apatseniko buledi ankhondo angawa pakuti atopa. Koma ine ndikupirikitsa Zeba ndi Zalimuna, mafumu a Midiyani.”
6 And he said [the] officials of Succoth ¿ [is] [the] hand of Zebah and Zalmunna now in hand your that we will give to army your bread.
Koma atsogoleri a Sukoti anayankha kuti, “Kodi Zeba ndi Zalimuna mwawagonjetsa kale kuti tipatse buledi ankhondo akowa?”
7 And he said Gideon therefore when gives Yahweh Zebah and Zalmunna in hand my and I will thresh flesh your with thorns of the wilderness and with briers.
Gideoni anayankha kuti, “Mwatero! Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna mʼdzanja langa, ndidzakukwapulani ndi matsatsa a minga ya mʼchipululu.”
8 And he went up from there Penuel and he spoke to them like this and they answered him [the] men of Penuel just as they had answered [the] men of Succoth.
Atachoka pamenepo anapita ku Penueli ndipo anapemphanso buledi kwa anthu a kumeneko, koma iwo anamuyankha monga anayankhira anthu a ku Sukoti aja.
9 And he said also to [the] men of Penuel saying when return I in peace I will tear down the tower this.
Gideoni anawawuzanso kuti, “Ndikamadzabwerera nditawagonjetsa, ndidzagwetsa nsanja iyi.”
10 And Zebah and Zalmunna [were] in Karkor and armies their [were] with them about fif-teen thousand all those [who] remained of all [the] army of [the] people of [the] east and those [who] fell [were] one hundred and twenty thousand man [who] drew [the] sword.
Nthawi iyi nʼkuti Zeba ndi Zalimuna ali ku Karikori ndi ankhondo pafupifupi 15,000. Amenewa ndiwo anatsalako mwa ankhondo a anthu akummawa; pakuti anafa ankhondo 120,000.
11 And he went up Gideon [the] way of those [who] dwell in tents from [the] east of Nobah and Jogbehah and he attacked the army and the army it was security.
Gideoni anadzera njira ya anthu a matenti kummawa kwa Noba ndi Yogibeha ndipo anawathira nkhondo popeza ankhondo awo anali osakonzekera.
12 And they fled Zebah and Zalmunna and he pursued after them and he captured [the] two - [the] kings of Midian Zebah and Zalmunna and all the army he routed.
Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri a Amidiyani anathawa koma Gideoni anawathamangitsa mpaka kuwagwira. Koma ankhondo awo onse anathawa ndi mantha.
13 And he returned Gideon [the] son of Joash from the battle from to [the] ascent of Heres.
Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi, pobwera kuchokera ku nkhondo anadzera njira ya ku chikweza cha Heresi.
14 And he captured a young man one of [the] men of Succoth and he enquired of him and he wrote down to him [the] officials of Succoth and elders its seventy and seven man.
Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti.
15 And he came to [the] men of Succoth and he said here! Zebah and Zalmunna whom you taunted me saying ¿ [is] [the] hand of Zebah and Zalmunna now in hand your that we will give to men your weary bread.
Kenaka Gideoni anabwera kwa anthu a ku Sukoti ndi kunena kuti, “Awa ndi Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri munkandinena nawo aja kuti, ‘Kodi Zeba ndi Zalimuna wawagonjetsa kale mmene ukuti tiwapatse buledi anthu ako otopawa?’”
16 And he took [the] elders of the city and [the] thorns of the wilderness and the briers and he taught with them [the] men of Succoth.
Tsono Gideoni anatenga akuluakulu a mu mzindawo ndipo anagwira matsatsa a minga za mʼchipululu ndi kuwakwapula nawo.
17 And [the] tower of Penuel he tore down and he killed [the] men of the city.
Anagwetsa nsanja ya ku Penueli ndi kupha amuna onse a mu mzindawo.
18 And he said to Zebah and to Zalmunna where? [are] the men whom you killed at Tabor (and they said *L(abh)*) like you like them one [was] like [the] appearance of [the] sons of the king.
Kenaka anafunsa Zeba ndi Zalimuna kuti, “Kodi anthu a ku Tabori amene munawapha aja anali a maonekedwe otani?” Iwo anayankha kuti, “Anali anthu a maonekedwe ngati inu. Aliyense ankaoneka ngati mwana wa mfumu?” Iwo anayankha kuti, “Anthu ngati inu, aliyense wooneka ngati mwana wa mfumu.”
19 And he said [were] brothers my [the] sons of mother my they [by] [the] life of Yahweh if you had let live them not I killed you.
Ndipo Gideoni anayankha kuti, “Ndikulumbira pa Mulungu, mukanapanda kuwapha nanenso sindikanakuphani. Ndi abale anga amenewo, ana a amayi anga enieni.”
20 And he said to Jether firstborn his arise kill them and not he drew the young man sword his for he was afraid for still he [was] a young man.
Tsono anawuza Yetero, mwana wake wachisamba kuti, “Tiye, ipha anthu amenewa!” Koma chifukwa Yeteri anali wamngʼono sanasolole lupanga lake, popeza anachita mantha.
21 And he said Zebah and Zalmunna arise you and fall on us for [is] like the man strength his and he arose Gideon and he killed Zebah and Zalmunna and he took the ornaments which [were] on [the] necks of camels their.
Tsono Zeba ndi Zalimuna anawuza Gideoni kuti, “Bwera utiphe ndiwe chifukwa uli ndi mphamvu za munthu wamkulu.” Choncho Gideoni anapita nawapha natenganso zokongoletsera zimene zinali pa makosi a ngamira zawo.
22 And they said [the] man of Israel to Gideon rule over us both you as well as son your as well as [the] son of son your for you have delivered us from [the] hand of Midian.
Aisraeli anati kwa Gideoni, “Inu muzitilamulira, mwana wanu ndi zidzukulu zanu, chifukwa mwatipulumutsa mʼmanja mwa Amidiyani.”
23 And he said to them Gideon not I will rule I over you and not he will rule son my over you Yahweh he will rule over you.
Koma Gideoni anawawuza kuti, “Sindidzakulamulirani, mwana wanganso sadzakulamulirani. Koma Yehova ndiye adzakulamulirani.”
24 And he said to them Gideon let me ask from you a petition and give to me everyone earring of plunder his for earrings of gold [belonged] to them for [were] Ishmaelites they.
Gideoni anatinso, “Ine ndikupemphani chinthu chimodzi. Aliyense wa inu andipatse ndolo zomwe anafunkha ku nkhondo.” (Adani aja anali ndi ndolo zagolide popeza anali Aismaeli).
25 And they said certainly we will give [them] and they spread out the garment and they threw there towards everyone earring of plunder his.
Iwo anayankha kuti, “Ife tikupatsani ndithu ndolozi.” Choncho anayala chinsalu, ndipo aliyense anaponyapo ndolo zimene anafunkha.
26 And it was [the] weight of [the] earrings of gold which he asked for one thousand and seven hundred gold apart from the ornaments and the pendants and [the] garments of purple that [were] on [the] kings of Midian and apart from the necklaces which [were] on [the] necks of camels their.
Tsono kulemera kwa ndolo zagolide zimene anapereka kunali makilogalamu makumi awiri, osawerengera kulemera kwa mphande, mkanda wamʼkhosi, zovala zapepo za mafumu a Midiyani ndiponso malamba azitsulo za mʼmakosi a ngamira zawo.
27 And he made it Gideon into an ephod and he placed it in city his in Ophrah and they acted as prostitutes all Israel after it there and it became for Gideon and for household his a snare.
Gideoni anagwiritsa ntchito golide uja kupanga efodi, ndipo anakamuyika ku mzinda wake ku Ofura. Tsono Aisraeli onse anasiya kupembedza Yehova nayamba kupembedza efodiyo kumeneko. Ichi chinasanduka msampha kwa Gideoni ndi banja lake lonse.
28 And it was subdued Midian before [the] people of Israel and not they repeated to lift up head their and it was at peace the land forty year[s] in [the] days of Gideon.
Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo.
29 And he went Jerub-Baal [the] son of Joash and he dwelt in own house his.
Yeru-Baala mwana wa Yowasi anapita kukakhala kwawo.
30 And to Gideon they belonged seventy sons [who] came out of thigh his for wives many they belonged to him.
Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri.
31 And concubine his who [was] in Shechem she bore to him also she a son and he made name his Abimelech.
Mdzakazi wake amene anali ku Sekemu, anabereka naye mwana wamwamuna, amene anamutcha Abimeleki.
32 And he died Gideon [the] son of Joash in old age good and he was buried in [the] tomb of Joash father his in Ophrah of [the] Abi-ezrite[s].
Gideoni mwana wa Yowasi anamwalira atakalamba ndipo anayikidwa mʼmanda a abambo ake, Yowasi ku Ofura mzinda wa Mwabiezeri.
33 And it was just when he had died Gideon and they turned back [the] people of Israel and they acted as prostitutes after the Baals and they made for themselves Baal-Berith into god.
Atangomwalira Gideoni, Aisraeli anayambanso kupembedza Abaala. Iwo anasandutsa Baala-Beriti kukhala mulungu wawo.
34 And not they remembered [the] people of Israel Yahweh God their who delivered them from [the] hand of all enemies their from round about.
Aisraeli sanakumbukirenso Yehova Mulungu wawo amene anawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo mbali zonse.
35 And not they did loyalty with [the] house of Jerub-Baal Gideon according to all the good which he had done with Israel.
Ndiponso sanachite zinthu zokomera banja la Yeru-Baala (ndiye kuti Gideoni) chifukwa cha zabwino zonse zimene iye anawachitira.