< Judges 2 >
1 And he went up [the] angel of Yahweh from Gilgal to Bokim. And he said I brought up you from Egypt and I brought you into the land which I swore to ancestors your and I said not I will break covenant my with you for ever.
Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
2 And you not you must make a covenant to [the] inhabitants of the land this altars their you will pull down! and not you have listened to voice my what? this have you done.
ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
3 And also I say not I will drive out them from before you and they will become for you sides and gods their they will become for you a snare.
Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
4 And it was when spoke [the] angel of Yahweh the words these to all [the] people of Israel and they lifted up the people voice their and they wept.
Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
5 And they called [the] name of the place that Bokim and they sacrificed there to Yahweh.
ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
6 And he sent away Joshua the people and they went [the] people of Israel everyone to own inheritance his to take possession of the land.
Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
7 And they served the people Yahweh all [the] days of Joshua and all - [the] days of the old [men] who they made long days after Joshua who they had seen all [the] work of Yahweh great which he had done for Israel.
Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
8 And he died Joshua [the] son of Nun [the] servant of Yahweh a son of a hundred and ten years.
Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
9 And people buried him in [the] territory of inheritance his in Timnath Heres in [the] hill country of Ephraim from [the] north of [the] mountain of Gaash.
Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
10 And also all the generation that they gathered to ancestors its and it arose a generation another after them which not they knew Yahweh and also the work which he had done for Israel.
Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
11 And they did [the] people of Israel the evil in [the] eyes of Yahweh and they served the Baals.
Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
12 And they forsook Yahweh - [the] God of ancestors their who brought out them from [the] land of Egypt and they went after - gods other some of [the] gods of the peoples which [were] around them and they bowed down to them and they provoked to anger Yahweh.
Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
13 And they forsook Yahweh and they served the Baal and the Ashtaroth.
Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
14 And it burned [the] anger of Yahweh on Israel and he gave them in [the] hand of plunderers and they plundered them and he sold them in [the] hand of enemies their from round about and not they were able still to stand before enemies their.
Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
15 In every - where they went out [the] hand of Yahweh it was on them for harm just as he had spoken Yahweh and just as he had sworn Yahweh to them and it was distress to them exceedingly.
Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
16 And he raised up Yahweh judges and they delivered them from [the] hand of plunderers their.
Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
17 And also to judges their not they listened for they acted as prostitutes after gods other and they bowed down to them they turned aside quickly from the way which they had walked fathers their to obey [the] commandments of Yahweh not they did so.
Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
18 And if he raised up Yahweh - for them judges and he was Yahweh with the judge and he delivered them from [the] hand of enemies their all [the] days of the judge for he had compassion Yahweh from groaning their because of [those who] oppressed them and [those who] oppressed them.
Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
19 And it was - when died the judge they turned back and they acted corruptly more than fathers their by walking after gods other to serve them and to bow down to them not they let drop any of deeds their and any of way their stubborn.
Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
20 And it burned [the] anger of Yahweh on Israel and he said because that they have transgressed the nation this covenant my which I commanded ancestors their and not they have listened to voice my.
Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
21 Also I not I will increase to dispossess anyone from before them any of the nations which he left Joshua and he died.
Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
22 So as to put to [the] test by them Israel ¿ [be] keeping [will] they [the] way of Yahweh by walking in them just as they kept [it] ancestors their or? not.
Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
23 And he left Yahweh the nations these to not to dispossess them quickly and not he gave them in [the] hand of Joshua.
Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.