< Joshua 8 >

1 And he said Yahweh to Joshua may not you fear and may not you be dismayed take with you all [the] people of war and arise go up Ai see - I have given in hand your [the] king of Ai and people his and city his and land his.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
2 And you will do to Ai and to king its just as you did to Jericho and to king its only booty its and livestock its you will plunder for yourselves set for yourself an ambush for the city behind it.
Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
3 And he arose Joshua and all [the] people of war to go up Ai and he chose Joshua thirty thousand man [the] mighty [men] of strength and he sent out them night.
Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
4 And he commanded them saying see you [are] lying in wait for the city behind the city may not you go far away from the city very and you will be all of you prepared.
nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
5 And I and all the people which [is] with me we will draw near to the city and it will be that they will come out to meet us just as at the first [time] and we will flee before them.
Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
6 And they will come out after us until have drawn out we them from the city for they will say [they are] fleeing before us just as at the first [time] and we will flee before them.
Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
7 And you you will arise from the ambush and you will take possession of the city and he will give it Yahweh God your in hand your.
inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
8 And it will be when have captured you the city you will set on fire the city with fire according to [the] word of Yahweh you will do see I have commanded you.
Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
9 And he sent out them Joshua and they went to the ambush and they remained between Beth-el and between Ai from [the] west of Ai and he stayed Joshua in the night that in among the people.
Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
10 And he rose early Joshua in the morning and he mustered the people and he went up he and [the] elders of Israel before the people Ai.
Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
11 And all the people of war which [was] with him they went up and they approached and they came before the city and they encamped from [the] north of Ai and the valley ([was] between it *Q(k)*) and between Ai.
Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
12 And he took about five thousand man and he set them an ambush between Beth-el and between Ai from [the] west of the city.
Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
13 And they set the people all the camp which [was] from [the] north of the city and rearguard its from [the] west of the city and he went Joshua in the night that in [the] middle of the valley.
Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
14 And it was when saw [the] king of Ai and they hurried and they rose early and they went out [the] men of the city to meet Israel for battle he and all people his to the appointed place before the Arabah and he not he knew that an ambush for him [was] behind the city.
Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
15 And they were struck Joshua and all Israel before them and they fled [the] direction of the wilderness.
Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
16 And they were called together all the people which ([was] in Ai *Q(K)*) to pursue after them and they pursued after Joshua and they were drawn out from the city.
Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
17 And not he remained anyone in Ai and Beth-el who not they went out after Israel and they left the city open and they pursued after Israel.
Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
18 And he said Yahweh to Joshua stretch out with the javelin which [is] in hand your to Ai for in hand your I will give it and he stretched out Joshua with the javelin which [was] in hand his to the city.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
19 And the ambush it arose quickly from place its and they ran when stretched out hand his and they went the city and they captured it and they hurried and they set on fire the city with fire.
Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
20 And they turned [the] men of Ai behind them and they saw and there! it went up [the] smoke of the city the heavens towards and not it was in them hands to flee hither and hither and the people which was fleeing the wilderness it turned back against the pursuer.
Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
21 And Joshua and all Israel they saw that it had captured the ambush the city and that it went up [the] smoke of the city and they turned back and they attacked [the] men of Ai.
Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
22 And these [men] they came out from the city to meet them and they were to Israel in the middle these from this and these from this and they struck down them until not he had left to him a survivor and a fugitive.
Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
23 And [the] king of Ai they captured alive and they brought near him to Joshua.
kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
24 And it was when had finished Israel to kill all [the] inhabitants of Ai in the open country in the wilderness which they had pursued them in it and they had fallen all of them to [the] mouth of [the] sword until were finished they and they returned all Israel Ai and they attacked it to [the] mouth of [the] sword.
Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
25 And it was all those [who] fell on the day that from man and unto woman two [plus] ten thousand all [the] people of Ai.
Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
26 And Joshua not he drew back hand his which he had stretched out with the javelin until that he had totally destroyed all [the] inhabitants of Ai.
Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
27 Only the livestock and [the] booty of the city that they plundered for themselves Israel according to [the] word of Yahweh which he had commanded Joshua.
Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
28 And he burned Joshua Ai and he made it a mound of perpetuity a desolation until the day this.
Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
29 And [the] king of Ai he hanged on the tree until [the] time of the evening and just as went the sun he commanded Joshua and they took down corpse his from the tree and they threw it to [the] entrance of [the] gate of the city and they set up over him a heap of stones great until the day this.
Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
30 Then he built Joshua an altar to Yahweh [the] God of Israel on [the] mountain of Ebal.
Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
31 Just as he had commanded Moses [the] servant of Yahweh [the] people of Israel according to [what] is written in [the] book of [the] law of Moses an altar of stones complete which not anyone has wielded on them iron and they offered up on it burnt offerings to Yahweh and they sacrificed peace offerings.
Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
32 And he wrote there on the stones copy of [the] law of Moses which he had written before [the] people of Israel.
Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
33 And all Israel and elders its and officials - and judges its [were] standing from this - and from this - of the ark before the priests the Levites [the] bearers of - [the] ark of [the] covenant of Yahweh as the sojourner as the native half of it to [the] front of [the] mountain of Gerizim and half of it to [the] front of [the] mountain of Ebal just as he had commanded Moses [the] servant of Yahweh to bless the people Israel at the former [time].
Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
34 And after thus he read aloud all [the] words of the law the blessing and the curse according to every [thing] written in [the] book of the law.
Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
35 Not it was anything from all that he had commanded Moses which not he read aloud Joshua before all [the] assembly of Israel and the women and the little one[s] and the sojourner[s] who went in midst their.
Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.

< Joshua 8 >