< Joshua 7 >

1 And they acted unfaithfully [the] people of Israel unfaithfulness in the devoted thing[s] and he took Achan [the] son of Carmi [the] son of Zabdi [the] son of Zerah of [the] tribe of Judah some of the devoted thing[s] and it burned [the] anger of Yahweh on [the] people of Israel.
Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
2 And he sent Joshua men from Jericho Ai which [is] beside Beth Aven from [the] east of Beth-el and he said to them saying go up and spy out the land and they went up the men and they spied out Ai.
Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
3 And they returned to Joshua and they said to him may not it go up all the people about two thousand man or about three thousand man let them go up and they may attack Ai may not you make go wearily there towards all the people for [are] few they.
Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
4 And they went up some of the people there about three thousand man and they fled before [the] men of Ai.
Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
5 And they struck down of them [the] men of Ai about thirty and six man and they pursued them before the gate to Shebarim and they struck down them at the descent and it melted [the] heart of the people and it became water.
Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
6 And he tore Joshua clothes his and he fell on face his [the] ground towards before [the] ark of Yahweh until the evening he and [the] elders of Israel and they made go up dust on head their.
Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
7 And he said Joshua alas! - O Lord Yahweh why? have you brought over at all the people this the Jordan to give us in [the] hand of the Amorite[s] to destroy us and if we had been willing and we had remained on [the] other side of the Jordan.
Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
8 Pardon me O Lord what? will I say after that it has turned Israel a neck before enemies its.
Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
9 And they may hear the Canaanite[s] and all [the] inhabitants of the land and they will surround us and they will cut off name our from the earth and what? will you do for name your great.
Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
10 And he said Yahweh to Joshua stand up for yourself why? this [are] you falling on face your.
Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
11 It has sinned Israel and also they have transgressed covenant my which I commanded them and also they have taken some of the devoted thing[s] and also they have stolen and also they have deceived and also they have put [them] among things their.
Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
12 And not they are able [the] people of Israel to stand before enemies their a neck they turn before enemies their for they have become a devoted thing not I will repeat to be with you if not you will destroy the devoted thing[s] from midst your.
Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
13 Arise consecrate the people and you will say consecrate yourselves for tomorrow for thus he says Yahweh [the] God of Israel devoted thing[s] [are] in midst your O Israel not you will be able to stand before enemies your until remove you the devoted thing[s] from midst your.
“Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
14 And you will bring yourselves near in the morning to tribes your and it will be the tribe which he will take it Yahweh it will draw near to the families and the family which he will take it Yahweh it will draw near to the households and the household which he will take it Yahweh it will draw near to the men.
“Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
15 And it will be the [one who] is taken by lot with the devoted thing[s] he will be burned with fire him and all that [belongs] to him for he has transgressed covenant of Yahweh and for he has done disgraceful folly in Israel.
Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
16 And he rose early Joshua in the morning and he brought near Israel to tribes its and it was taken by lot [the] tribe of Judah.
Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
17 And he brought near [the] family of Judah and he took [the] family of the Zerahite[s] and he brought near [the] family of the Zerahite[s] to the men and he was taken by lot Zabdi.
Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
18 And he brought near household his to the men and he was taken by lot Achan [the] son of Carmi [the] son of Zabdi [the] son of Zerah of [the] tribe of Judah.
Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
19 And he said Joshua to Achan O son my put please glory to Yahweh [the] God of Israel and give to him confession and tell please to me what? have you done may not you hide [it] from me.
Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
20 And he answered Achan Joshua and he said truly I I have sinned to Yahweh [the] God of Israel and like this and like this I have done.
Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
21 (And I saw *Q(k)*) among the booty cloak of Shinar one good and two hundred shekels silver and a wedge of gold one [was] fifty shekels weight its and I desired them and I took them and there they [are] hidden in the ground in [the] midst of tent my and the silver [is] under it.
Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
22 And he sent Joshua messengers and they ran the tent towards and there! [it was] hidden in tent his and the silver [was] under it.
Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
23 And they took them from [the] midst of the tent and they brought them to Joshua and to all [the] people of Israel and they poured out them before Yahweh.
Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
24 And he took Joshua Achan [the] son of Zerah and the silver and the cloak and [the] wedge of gold and sons his and daughters his and ox[en] his and donkey[s] his and sheep his and tent his and all that [belonged] to him and all Israel with him and they brought up them [the] valley of Achor.
Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
25 And he said Joshua why? have you brought trouble to us he will bring trouble to you Yahweh on the day this and they stoned him all Israel stone[s] and they burned them with fire and they stoned them with stones.
Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
26 And they set up over him a heap of stones great until the day this and he turned back Yahweh from [the] burning of anger his there-fore someone called [the] name of the place that [the] valley of Achor until the day this.
Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.

< Joshua 7 >