< Jonah 3 >
1 And it came [the] word of Yahweh to Jonah a second [time] saying.
Ndipo Yehova anayankhula ndi Yona kachiwiri kuti,
2 Arise go to Nineveh the city great and call out against it the proclamation which I [am] speaking to you.
“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire uthenga umene ndikupatsa.”
3 And he arose Jonah and he went to Nineveh according to [the] word of Yahweh and Nineveh it was a city great to God a journey of three days.
Yona anamvera mawu a Yehova ndipo anapita ku Ninive. Tsono Ninive unali mzinda waukulu kwambiri; wofunika masiku atatu kuwudutsa.
4 And he began Jonah to go in the city a journey of a day one and he proclaimed and he said yet forty day[s] and Nineveh [is] about to be overturned.
Yona analowa mu mzindawo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi. Iye ankalalikira kuti, “Atsala masiku makumi anayi kuti Ninive awonongedwe.”
5 And they believed [the] people of Nineveh in God and they proclaimed a fast and they wore sackcloth from great their and unto insignificant their.
Anthu a ku Ninive anakhulupirira Mulungu. Analengeza kuti aliyense, wamkulu ndi wamngʼono yemwe asale zakudya ndipo avale chiguduli.
6 And it reached the word to [the] king of Nineveh and he arose from throne his and he took off cloak his from on him and he covered sackcloth and he sat on ash[es].
Mfumu ya ku Ninive itamva nkhaniyi, inatsika pa mpando wake waufumu, nivula mkanjo wake waufumu ndipo inavala chiguduli ndi kukhala pansi pa fumbi.
7 And he had a proclamation made and he said in Nineveh from [the] decree of the king and great [people] his saying the people and the livestock the cattle and the flock[s] may not they taste anything may not they graze and water may not they drink.
Tsono mfumuyo inalengeza mu Ninive kuti, “Mwa lamulo lochokera kwa mfumu ndi akalonga ake: “Munthu aliyense kapenanso nyama, ngʼombe kapena nkhosa, zisadye kanthu kalikonse; musazilole kuti zidye kapena kumwa.
8 And they may cover themselves sackcloth the people and the livestock and let them call out to God with strength and let them turn back everyone from way his evil and from the violence which [is] in palms their.
Koma anthu avale ziguduli, ndipo nyamanso aziveke ziguduli. Munthu aliyense azifuwula kwa Mulungu ndi mphamvu zake zonse. Anthuwo asiye makhalidwe awo oyipa ndi machitidwe achiwawa.
9 Who? [is] knowing he will turn and he will relent God and he will turn back from [the] burning of anger his and not we will perish.
Angadziwe ndani? Mwina Mulungu nʼkutikhululukira ndipo mwa chifundo chake nʼkuleka kutikwiyira, ifeyo osawonongedwa.”
10 And he saw God deeds their that they turned back from way their evil and he relented God on the evil which he had said to do to them and not he did [it].
Mulungu ataona zimene anthuwo anachita, ndi mmene anasiyira makhalidwe awo oyipa, anawachitira chifundo ndipo sanabweretse chiwonongeko chimene anawaopseza nacho.