< Job 20 >
1 And he answered Zophar the Naamathite and he said.
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 Therefore disquieting thoughts my they make respond me and in order to agitate I in me.
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 [the] correction of Insult my I have heard and a spirit from understanding my it answers me.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 ¿ This do you know from antiquity from when put humankind on earth.
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 That [the] cry of joy of wicked [people] [is] from near and [the] gladness of [the] godless [is] until a moment.
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Though it will go up to the heavens loftiness his and head his to the cloud[s] it will reach.
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 Like own dung his to perpetuity he will perish [those who] saw him they will say where [is]? he.
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 Like a dream he will fly away and not people will find him and he may be chased away like a vision of [the] night.
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 An eye it caught sight of him and not it will repeat and not again it will see him place his.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 Children his they will seek [the] favor of poor [people] and own hands his they will give back wealth his.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Bones his they were full (youthful vigor his *Q(K)*) and with him on [the] dust it will lie down.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 Though it is sweet in mouth his evil he hides it under tongue his.
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 He spares it and not he lets loose it and he withholds it in [the] midst of mouth his.
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 Food his in inward parts his it is changed venom of cobras in inward part[s] his.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Wealth he swallows and he has vomited up it from belly his he drives out it God.
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 [the] poison of Cobras he sucks it slays him [the] tongue of a viper.
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 May not he look on streams rivers of torrents of honey and curd.
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 [he is] restoring [the] gain And not he swallows [it] according to [the] wealth of trading his not he will rejoice.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 For he has crushed he has neglected poor [people] a house he has seized and not he had built it.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 For - not he knows quiet in belly his among desired [things] his not he delivers.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 There not [is] a survivor to devour he there-fore not it will endure prosperity his.
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 When is full sufficiency his it will be distress to him every hand of a sufferer it will come to him.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 May he be - [about] to fill belly his he will send on him [the] burning of anger his and he will send rain on him in bowel[s] his.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 He will flee from a weapon of iron it will cut through him a bow of bronze.
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 He will draw [it] out and it came out from [the] back and lightning from gall-bladder his it will come on him terrors.
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 All darkness [is] hidden for treasured [things] his it will consume him fire [which] not it has been fanned it will be evil a survivor in tent his.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 They will reveal [the] heavens iniquity his and [the] earth [will] rise up to him.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 It will depart [the] produce of house his torrents on [the] day of anger his.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 This - [is the] portion of a person wicked from God and [the] inheritance of decree his from God.
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”