< Job 17 >

1 Spirit my it is broken days my they are extinguished grave [belong] to me.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 Not mockeries [are] with me and on rebelling they may it dwell eye my.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 Make! please stand surety for me with yourself who? that to hand my will he strike himself.
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 For heart their you have kept from understanding there-fore not you will exalt [them].
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 For a share he tells friends and [the] eyes of children his they will fail.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 And he has set me to use a proverb peoples and a spitting to [the] face I am.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 And it has grown dim from grief eye my and members my [are] like shadow all of them.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 They are appalled upright [people] on this and [the] innocent on [the] godless he will rouse himself.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 And he may hold [the] righteous way his and [the] clean of hands he will increase strength.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 And but all of them you will return and come please and not I will find among you a wise [person].
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 Days my they have passed plans my they have been torn apart [the] wishes of heart my.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Night into day they make light [is] near from before darkness.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 If I will hope for Sheol home my in the darkness I have spread out beds my. (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 To the pit I have called out [are] father my you O mother my and sister my to the maggot.
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 And where? then [is] hope my and hope my who? will he observe it.
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 [the] poles of Sheol will they go down? or? together to [the] dust will we descend. (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Job 17 >